Yesaya 35 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 35:1-10

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

1Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;

dziko lowuma lidzakondwa

ndi kuchita maluwa. 2Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka

lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.

Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,

maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,

ukulu wa Mulungu wathu.

3Limbitsani manja ofowoka,

limbitsani mawondo agwedegwede;

4nenani kwa a mitima yamantha kuti;

“Limbani mtima, musachite mantha;

Mulungu wanu akubwera,

akubwera kudzalipsira;

ndi kudzabwezera chilango adani anu;

akubwera kudzakupulumutsani.”

5Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso

ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.

6Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,

ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.

Akasupe adzatumphuka mʼchipululu

ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,

7mchenga wotentha udzasanduka dziwe,

nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.

Pamene panali mbuto ya ankhandwe

padzamera udzu ndi bango.

8Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;

ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.

Anthu odetsedwa

sadzayendamo mʼmenemo;

zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.

9Kumeneko sikudzakhala mkango,

ngakhale nyama yolusa sidzafikako;

sidzapezeka konse kumeneko.

Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.

10Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.

Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;

kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.

Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,

ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

King James Version

Isaiah 35:1-10

1The wilderness and the solitary place shall be glad for them; and the desert shall rejoice, and blossom as the rose. 2It shall blossom abundantly, and rejoice even with joy and singing: the glory of Lebanon shall be given unto it, the excellency of Carmel and Sharon, they shall see the glory of the LORD, and the excellency of our God.

3¶ Strengthen ye the weak hands, and confirm the feeble knees. 4Say to them that are of a fearful heart, Be strong, fear not: behold, your God will come with vengeance, even God with a recompence; he will come and save you.35.4 fearful: Heb. hasty

5Then the eyes of the blind shall be opened, and the ears of the deaf shall be unstopped. 6Then shall the lame man leap as an hart, and the tongue of the dumb sing: for in the wilderness shall waters break out, and streams in the desert. 7And the parched ground shall become a pool, and the thirsty land springs of water: in the habitation of dragons, where each lay, shall be grass with reeds and rushes.35.7 grass…: or, a court for reeds, etc 8And an highway shall be there, and a way, and it shall be called The way of holiness; the unclean shall not pass over it; but it shall be for those: the wayfaring men, though fools, shall not err therein.35.8 but…: or, for he shall be with them 9No lion shall be there, nor any ravenous beast shall go up thereon, it shall not be found there; but the redeemed shall walk there: 10And the ransomed of the LORD shall return, and come to Zion with songs and everlasting joy upon their heads: they shall obtain joy and gladness, and sorrow and sighing shall flee away.