1Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Mkazi
2Undipsompsone ndi milomo yako
chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;
dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.
Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!
Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.
Abwenzi
Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,
tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.
Mkazi
Amachita bwinotu potamanda iwe!
5Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,
inu akazi a ku Yerusalemu,
ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,
ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,
ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.
Alongo anga anandikwiyira
ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;
munda wangawanga sindinawusamalire.
7Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako
ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.
Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere
pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Abwenzi
8Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,
ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa
ndipo udyetse ana ambuzi
pambali pa matenti a abusa.
Mwamuna
9Iwe bwenzi langa,
uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,
khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11Tidzakupangira ndolo zagolide
zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Mkazi
12Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,
mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,
kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,
ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Mwamuna
15Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,
maso ako ali ngati nkhunda.
Mkazi
16Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!
Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Mwamuna
17Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,
phaso lake ndi la mtengo wa payini.
1The song of songs, which is Solomon’s.
2Let him kiss me with the kisses of his mouth: for thy love is better than wine.1.2 thy…: Heb. thy loves 3Because of the savour of thy good ointments thy name is as ointment poured forth, therefore do the virgins love thee. 4Draw me, we will run after thee: the king hath brought me into his chambers: we will be glad and rejoice in thee, we will remember thy love more than wine: the upright love thee.1.4 the upright…: or, they love thee uprightly 5I am black, but comely, O ye daughters of Jerusalem, as the tents of Kedar, as the curtains of Solomon. 6Look not upon me, because I am black, because the sun hath looked upon me: my mother’s children were angry with me; they made me the keeper of the vineyards; but mine own vineyard have I not kept.
7Tell me, O thou whom my soul loveth, where thou feedest, where thou makest thy flock to rest at noon: for why should I be as one that turneth aside by the flocks of thy companions?1.7 as one…: or, as one that is veiled
8¶ If thou know not, O thou fairest among women, go thy way forth by the footsteps of the flock, and feed thy kids beside the shepherds’ tents. 9I have compared thee, O my love, to a company of horses in Pharaoh’s chariots. 10Thy cheeks are comely with rows of jewels, thy neck with chains of gold. 11We will make thee borders of gold with studs of silver.
12¶ While the king sitteth at his table, my spikenard sendeth forth the smell thereof. 13A bundle of myrrh is my wellbeloved unto me; he shall lie all night betwixt my breasts. 14My beloved is unto me as a cluster of camphire in the vineyards of En-gedi.1.14 camphire: or, cypress 15Behold, thou art fair, my love; behold, thou art fair; thou hast doves’ eyes.1.15 my love: or, my companion 16Behold, thou art fair, my beloved, yea, pleasant: also our bed is green. 17The beams of our house are cedar, and our rafters of fir.1.17 rafters: or, galleries