Mkazi
1Ine ndine duwa la ku Saroni,
duwa lokongola la ku zigwa.
Mwamuna
2Monga duwa lokongola pakati pa minga
ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.
Mkazi
3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango
ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.
Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,
ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.
4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,
ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.
5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,
unditsitsimutse ndi ma apulosi,
pakuti chikondi chandifowoketsa.
6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,
ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani
pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:
Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa
mpaka pamene chifunire ichocho.
8Tamverani bwenzi langa!
Taonani! Uyu akubwera apayu,
akulumphalumpha pa mapiri,
akujowajowa pa zitunda.
9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.
Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,
akusuzumira mʼmazenera,
akuyangʼana pa mpata wa zenera.
10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,
“Dzuka bwenzi langa,
wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.
11Ona, nyengo yozizira yatha;
mvula yatha ndipo yapitiratu.
12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;
nthawi yoyimba yafika,
kulira kwa njiwa kukumveka
mʼdziko lathu.
13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;
mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.
Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga
tiye tizipita.”
Mwamuna
14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,
mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,
onetsa nkhope yako,
nʼtamvako liwu lako;
pakuti liwu lako ndi lokoma,
ndipo nkhope yako ndi yokongola.
15Mutigwirire nkhandwe,
nkhandwe zingʼonozingʼono
zimene zikuwononga minda ya mpesa,
minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.
Mkazi
16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;
amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.
17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira
ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,
unyamuke bwenzi langa,
ndipo ukhale ngati gwape
kapena ngati mwana wa mbawala
pakati pa mapiri azigwembezigwembe.
1I am the rose of Sharon, and the lily of the valleys. 2As the lily among thorns, so is my love among the daughters.
3As the apple tree among the trees of the wood, so is my beloved among the sons. I sat down under his shadow with great delight, and his fruit was sweet to my taste.2.3 I sat…: Heb. I delighted and sat down, etc2.3 taste: Heb. palate 4He brought me to the banqueting house, and his banner over me was love.2.4 banqueting…: Heb. house of wine 5Stay me with flagons, comfort me with apples: for I am sick of love.2.5 comfort…: Heb. straw me with apples 6His left hand is under my head, and his right hand doth embrace me. 7I charge you, O ye daughters of Jerusalem, by the roes, and by the hinds of the field, that ye stir not up, nor awake my love, till he please.2.7 I charge…: Heb. I adjure you
8¶ The voice of my beloved! behold, he cometh leaping upon the mountains, skipping upon the hills. 9My beloved is like a roe or a young hart: behold, he standeth behind our wall, he looketh forth at the windows, shewing himself through the lattice.2.9 shewing…: Heb. flourishing 10My beloved spake, and said unto me, Rise up, my love, my fair one, and come away. 11For, lo, the winter is past, the rain is over and gone; 12The flowers appear on the earth; the time of the singing of birds is come, and the voice of the turtle is heard in our land; 13The fig tree putteth forth her green figs, and the vines with the tender grape give a good smell. Arise, my love, my fair one, and come away.
14¶ O my dove, that art in the clefts of the rock, in the secret places of the stairs, let me see thy countenance, let me hear thy voice; for sweet is thy voice, and thy countenance is comely. 15Take us the foxes, the little foxes, that spoil the vines: for our vines have tender grapes.
16¶ My beloved is mine, and I am his: he feedeth among the lilies. 17Until the day break, and the shadows flee away, turn, my beloved, and be thou like a roe or a young hart upon the mountains of Bether.2.17 of Bether: or, of division