Yesaya 34 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 34:1-17

Chiweruzo cha Anthu a Mitundu Yonse

1Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve:

tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse:

Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,

dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!

2Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse;

wapsera mtima magulu awo onse ankhondo.

Iye adzawawononga kotheratu,

nawapereka kuti aphedwe.

3Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja,

mitembo yawo idzawola ndi kununkha;

mapiri adzafiira ndi magazi awo.

4Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka

ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala;

nyenyezi zonse zidzayoyoka

ngati masamba ofota a mphesa,

ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.

5Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba;

taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu,

anthu amene ndawawononga kotheratu.”

6Lupanga la Yehova lakhuta magazi,

lakutidwa ndi mafuta;

magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi,

mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna.

Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira

ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.

7Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati,

ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe.

Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha,

ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.

8Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira

ndi kulanga adani a Ziyoni.

9Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula,

ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule;

dziko lake lidzasanduka phula lamoto!

10Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana;

utsi wake udzafuka kosalekeza.

Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado;

palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.

11Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu;

amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo.

Mulungu adzatambalitsa pa Edomu

chingwe choyezera cha chisokonezo

ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.

12Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko;

akalonga ake onse adzachotsedwa.

13Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa,

khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake.

Ankhandwe azidzadya mʼmenemo;

malo okhalamo akadzidzi.

14Avumbwe adzakumana ndi afisi,

ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana.

Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa

ndi kupeza malo opumulirako.

15Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira,

adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake;

akamtema adzasonkhananso kumeneko,

awiriawiri.

16Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga:

mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa;

sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake.

Pakuti Yehova walamula kuti zitero,

ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.

17Yehova wagawa dziko lawo;

wapatsa chilichonse chigawo chake.

Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya

ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

King James Version

Isaiah 34:1-17

1Come near, ye nations, to hear; and hearken, ye people: let the earth hear, and all that is therein; the world, and all things that come forth of it.34.1 all that…: Heb. the fulness thereof 2For the indignation of the LORD is upon all nations, and his fury upon all their armies: he hath utterly destroyed them, he hath delivered them to the slaughter. 3Their slain also shall be cast out, and their stink shall come up out of their carcases, and the mountains shall be melted with their blood. 4And all the host of heaven shall be dissolved, and the heavens shall be rolled together as a scroll: and all their host shall fall down, as the leaf falleth off from the vine, and as a falling fig from the fig tree. 5For my sword shall be bathed in heaven: behold, it shall come down upon Idumea, and upon the people of my curse, to judgment. 6The sword of the LORD is filled with blood, it is made fat with fatness, and with the blood of lambs and goats, with the fat of the kidneys of rams: for the LORD hath a sacrifice in Bozrah, and a great slaughter in the land of Idumea. 7And the unicorns shall come down with them, and the bullocks with the bulls; and their land shall be soaked with blood, and their dust made fat with fatness.34.7 unicorns: or, rhinocerots34.7 soaked: or, drunken 8For it is the day of the LORD’s vengeance, and the year of recompences for the controversy of Zion.

9And the streams thereof shall be turned into pitch, and the dust thereof into brimstone, and the land thereof shall become burning pitch. 10It shall not be quenched night nor day; the smoke thereof shall go up for ever: from generation to generation it shall lie waste; none shall pass through it for ever and ever.

11¶ But the cormorant and the bittern shall possess it; the owl also and the raven shall dwell in it: and he shall stretch out upon it the line of confusion, and the stones of emptiness.34.11 cormorant: or, pelican 12They shall call the nobles thereof to the kingdom, but none shall be there, and all her princes shall be nothing. 13And thorns shall come up in her palaces, nettles and brambles in the fortresses thereof: and it shall be an habitation of dragons, and a court for owls.34.13 owls: or, ostriches: Heb. daughters of the owl 14The wild beasts of the desert shall also meet with the wild beasts of the island, and the satyr shall cry to his fellow; the screech owl also shall rest there, and find for herself a place of rest.34.14 The wild beasts of the desert: Heb. Ziim34.14 the wild beasts of the island: Heb. Ijim34.14 screech…: or, night monster 15There shall the great owl make her nest, and lay, and hatch, and gather under her shadow: there shall the vultures also be gathered, every one with her mate.

16¶ Seek ye out of the book of the LORD, and read: no one of these shall fail, none shall want her mate: for my mouth it hath commanded, and his spirit it hath gathered them. 17And he hath cast the lot for them, and his hand hath divided it unto them by line: they shall possess it for ever, from generation to generation shall they dwell therein.