Yesaya 2 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 2:1-22

Phiri la Yehova

1Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

2Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,

lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

3Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

4Iye adzaweruza pakati pa mayiko,

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

5Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,

tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

6Inu Yehova mwawakana anthu anu,

nyumba ya Yakobo.

Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;

amawombeza mawula ngati Afilisti,

ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.

7Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;

ndipo chuma chawo ndi chosatha.

Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;

ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.

8Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;

iwo amapembedza ntchito ya manja awo,

amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.

9Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa

ndi kutsitsidwa.

Inu Yehova musawakhululukire.

10Lowani mʼmatanthwe,

bisalani mʼmaenje,

kuthawa kuopsa kwa Yehova

ndi ulemerero wa ufumu wake!

11Kudzikuza kwa anthu kudzatha,

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku

limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,

ndipo adzagonjetsa

onse amphamvu,

13tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,

ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,

14tsiku la mapiri onse ataliatali

ndiponso la zitunda zonse zazitali,

15tsiku la nsanja zonse zazitali

ndiponso malinga onse olimba,

16tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi

ndiponso la mabwato onse okongola.

17Kudzikuza kwa munthu kudzatha

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,

18ndipo mafano onse adzatheratu.

19Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndi mʼmaenje a nthaka,

kuthawa mkwiyo wa Yehova,

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

20Tsiku limenelo anthu adzatayira

mfuko ndi mileme

mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,

amene anawapanga kuti aziwapembedza.

21Adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka

kuthawa mkwiyo wa Yehova

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22Lekani kudalira munthu,

amene moyo wake sukhalira kutha.

Iye angathandize bwanji wina aliyense?

Asante Twi Contemporary Bible

Yesaia 2:1-22

Awurade Bepɔ No

1Yei ne deɛ Amos babarima Yesaia hunuiɛ, a ɛfa Yuda ne Yerusalem ho.

2Nna a ɛdi akyire no mu no,

Awurade asɔredan bepɔ no bɛtim

sɛ mmepɔ no nyinaa ti;

ɛbɛgye edin aboro nkokoɔ nyinaa so

na aman nyinaa bɛbɔ yuu akɔ hɔ.

3Nnipa bebree bɛba abɛka sɛ,

“Mommra mma yɛnkɔ Awurade bepɔ no so,

nkɔ Yakob Onyankopɔn efie.

Ɔbɛkyerɛkyerɛ yɛn nʼakwan

sɛdeɛ ɛbɛyɛ a yɛbɛnante nʼakwantempɔn so.”

Mmara no bɛfiri Sion aba

na Awurade asɛm afiri Yerusalem.

4Ɔbɛbu amanaman ntam atɛn

na ɔbɛsiesie nnipa bebree ntam asɛm;

wɔde wɔn akofena bɛbobɔ nsɔ

na wɔde wɔn mpea ayɛ nsɔsɔ.

Ɔman bi rentwe ɔman foforɔ so akofena,

na wɔrenyɛ ahoboa biara mma ɔko bio.

5Mommra, Ao Yakob fiefoɔ,

momma yɛnnante Awurade hann mu.

Awurade Da No

6Awurade, Woagya wo nkurɔfoɔ,

Yakob fiefoɔ.

Gyedihunu a ɛfiri apueeɛ fam ahyɛ wɔn ma;

wɔhyɛ nkɔm sɛ Filistifoɔ

na wɔ ne abosonsomfoɔ di hwebom.

7Dwetɛ ne sikakɔkɔɔ ahyɛ wɔn asase no so ma;

wɔn ademudeɛ dɔɔso bebree.

Apɔnkɔ ayɛ wɔn asase no so ma;

na wɔn nteaseɛnam dodoɔ nni ano.

8Ahoni ahyɛ wɔn asase no so ma;

wɔkoto sɔre wɔn ankasa nsa ano adwuma,

deɛ wɔn nsateaa ayɛ.

9Enti, Awurade bɛbrɛ onipa ase

na wama adasamma aboto.

Ɔmmfa wɔn ho nkyɛ wɔn.

10Kɔhyɛne abotan no mu,

fa wo ho kɔsie asase no mu ɛsiane Awurade ho hu

ne nʼanimuonyam kɛseyɛ nti!

11Wɔbɛbrɛ ɔhantanni ase,

na wɔde nnipa ahomasoɔ ahwe fam;

Awurade nko ara na wɔbɛma no so da no.

12Asafo Awurade ahyɛ da bi

ama ahomasofoɔ nyinaa

ne deɛ ɛma ne ho so nyinaa

(wɔbɛbrɛ wɔn ase),

13Lebanon2.13 Lebanon yɛ ɔmantam bi a na ɛda Yordan apueeɛ fam a, ɛnam ntweneduro ne anantwie a na ɛwɔ hɔ no enti, agye din. ntweneduro nyinaa, atentene ne deɛ ɛkrɔn,

ne Basan odum nnua no,

14mmepɔ atentene nyinaa

ne nkokoɔ a ɛwowareɛ nyinaa,

15ne abantenten a ɛkorɔn

ne ɔfasuo biara a ɛyɛ den,

16adwadie hyɛn biara

ne ɛhyɛn kɛseɛ fɛfɛ biara.

17Wɔbɛbrɛ ɔhantanni ase,

na wɔde nnipa ahomasoɔ ahwe fam;

Awurade nko ara na wɔbɛma no so da no,

18na ahoni no bɛyera korakora.

19Nnipa bɛdwane akɔhyɛ abodan a ɛwɔ abotan mu

ne ntokuro a ɛdeda asase mu

ɛsiane Awurade ho hu

ne nʼanimuonyam kɛseyɛ enti,

ɛberɛ a ɔbɛsɔre awoso asase.

20Saa ɛda no, nnipa bɛto

wɔn dwetɛ ne sikakɔkɔɔ ahoni

a wɔyɛɛ sɛ wɔbɛsom no

agu ama akusie ne mpan.

21Wɔbɛdwane akɔhyɛne abotan mu ntokuro mu

ne abotan mpaapaeɛ mu

ɛsiane Awurade ho hu

ne nʼanimuonyam kɛseyɛ enti,

ɛberɛ a ɔbɛsɔre awoso asase.

22Monnyae sɛ mode mo ho to nnipa,

a wɔwɔ ahome kɛkɛ so.

Wɔyɛ ɛdeɛn koraa?