Yesaya 1 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

Asante Twi Contemporary Bible

Yesaia 1:1-31

1Saa anisoadehunu a ɛfa Yuda ne Yerusalem ho no baa Amos babarima Yesaia so wɔ Yuda ahemfo Usia, Yotam, Ahas ne Hesekia berɛ so.

Atuateman

2Ao, ɔsoro, montie! Ao, asase yɛ aso!

Na Awurade akasa:

“Matete mma ama wɔanyini,

nanso wɔate me so atua.

3Nantwie nim ne wura,

afunumu nso nim ne wura mmoa adididaka,

nanso Israel nnim,

me nkurɔfoɔ nte aseɛ.”

4Aa, amumuyɛ ɔman,

ɔman a afɔdie adesoa ahyɛ wɔn ma,

nnebɔneyɛfoɔ kuo,

mma a porɔeɛ ahyɛ wɔn ma!

Wɔatwe wɔn ho afiri Awurade ho;

Wɔapo Israel Kronkronni no,

wɔadane wɔn akyi akyerɛ no.

5Adɛn enti na mopɛ sɛ wɔkɔ so boro mo?

Adɛn enti na moda so te atua?

Wɔapira mo tiri,

na mo akoma nso di yea.

6Ɛfiri mo nan ase kɔsi mo tiri so

ahomeka biara nni mu,

apirakuro ne nsoasoaeɛ nko ara

akuro a anim deda hɔ

na wɔnhohoro so anaa Wɔnkyekyereeɛ

anaa wɔmfaa ngo nsrasraa so.

7Mo ɔman ada mpan,

wɔde ogya ahyehye mo nkuropɔn;

ananafoɔ regye mo mfuo

a mo ani tua,

na asɛe sɛdeɛ ɛyɛɛ ɛberɛ a ahɔhoɔ tuu mo guiɛ no.

8Wɔagya Ɔbabaa Sion

te sɛ bobe turo mu sese

te sɛ akuraa a ɛsi ɛferɛ afuo mu,

te sɛ kuropɔn a atamfoɔ atwa ho ahyia.

9Awurade

tumfoɔ no annya yɛn asefoɔ a,

anka yɛayɛ sɛ Sodom,

na yɛadane ayɛ sɛ Gomora.

10Montie Awurade asɛm,

mo Sodom sodifoɔ;

montie yɛn Onyankopɔn mmara,

mo Gomorafoɔ!

11“Mo afɔrebɔ ahodoɔ bebree no,

ɛdeɛn na ɛyɛ ma me?”

Sɛdeɛ Awurade seɛ nie.

“Mewɔ ɔhyeɛ afɔrebɔdeɛ ma ɛboro so,

deɛ ɛyɛ nnwennini ne mmoa a wɔadɔre sradeɛ;

mʼani nnye

anantwinini, nnwammaa ne mpapo mogya ho.

12Sɛ moba mʼanim a

hwan na ɔbisa yei firi mo hɔ?

Hwan na ɔsomaa mo sɛ monnantenante me efie yi?

13Monnyae afɔrebɔdeɛ a mode ba a ɛmfra no!

Mo aduhwam yɛ me tan.

Ɔbosome foforɔ, home nna ne nhyiamu ahodoɔ ne

mo nhyiamu fi no afono me.

14Mo bosome foforɔ afahyɛ ne mo apontoɔ a moahyehyɛ no,

me kra kyiri.

Ayɛ adesoa ama me;

masoa mabrɛ.

15Sɛ mopagya mo nsa bɔ mpaeɛ a,

mɛyi mʼani ato nkyɛn.

Sɛ mobɔ mpaeɛ bebree mpo a

merentie.

“Mogya bebree agu mo nsa ho fi.

16“Monnwira mo ho na mo ho nte.

Monnyi mo nnebɔne mfiri mʼani so!

Monnyae bɔne yɛ.

17Monyɛ papa; monhwehwɛ atɛntenenee

Monhyɛ wɔn a wɔhyɛ wɔn so nkuran.

Monni mma nwisiaa,

monka akunafoɔ nsɛm mma wɔn.

18“Afei mommra na yɛnnwene mmɔ mu,”

sɛdeɛ Awurade seɛ nie.

“Sɛ mo bɔne te sɛ kɔben a,

ɛbɛyɛ fitaa sɛ sukyerɛmma;

mpo sɛ ɛyɛ kɔkɔɔ te sɛ mogya a

ɛbɛyɛ fitaa sɛ asaawa foturo.

19Sɛ mopene so na moyɛ ɔsetie a,

mobɛdi asase no so nnepa.

20Na sɛ moampene na mote atua a,

akofena bɛdi mo nam.”

Awurade na wakasa.

21Hwɛ sɛdeɛ kuropɔn nokwafoɔ no

adane odwamanfoɔ.

Ɛberɛ bi na atɛntenenee ahyɛ no ma

na anka tenenee te ne mu,

nanso seesei awudifoɔ ahyɛ mu ma!

22Wo dwetɛ adane adeɛ a ɛho nni mfasoɔ,

wɔde nsuo afra wo nsã papa mu.

23Wo sodifoɔ yɛ atuatefoɔ,

akorɔmfoɔ yɔnkonom;

wɔn nyinaa pɛ adanmudeɛ,

na wɔpere akyɛdeɛ ho.

Wɔnni mma nwisiaa;

na akunafoɔ nsɛm nkɔ wɔn anim.

24Enti, Awurade, Otumfoɔ Awurade,

deɛ ɔyɛ Kɛseɛ ma Israel no ka sɛ,

“Aa, mɛnya ahomegyeɛ afiri mʼatamfoɔ hɔ

na matɔ wɔn so were.

25Mɛma me nsa so, atia mo;

mɛhohoro wo ho fi korakora

na mayi mo ho nkekaawa nyinaa.

26Mɛma mo atemmufoɔ bio sɛ kane no,

ne mo afutufoɔ sɛdeɛ na ɛteɛ, ahyɛaseɛ no.

Yei akyi no, wɔbɛfrɛ wo

Kuropɔn Tenenee

Kuropɔn Nokwafoɔ.”

27Wɔde atɛntenenee bɛgye Sion bio,

na wɔn a wɔnu wɔn ho no, wɔde tenenee bɛgye wɔn.

28Nanso atuatefoɔ ne nnebɔneyɛfoɔ deɛ, wɔbɛdwɛre wɔn abɔ mu,

na wɔn a wɔpa Awurade akyi bɛyera.

29“Mo ani bɛwu ɛsiane odum anyame a

monyaa wɔn mu anigyeɛ no;

wɔbɛgu mo anim ase ɛsiane nturo

a mosom abosom wɔ mu no enti.

30Mobɛyɛ sɛ odum a ne nhahan apo,

ne turo a ɛnnya nsuo.

31Ɔhoɔdenfoɔ bɛyɛ sɛ adeɛ a ɛhye ntɛm;

nʼadwuma bɛyɛ sɛ ogya nturueɛ;

ne mmienu no bɛhye abɔ mu,

a obiara rentumi nnum.”