Yesaya 3 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 3:1-26

Chiweruzo pa Yerusalemu ndi Yuda

1Taonani tsopano, Ambuye

Yehova Wamphamvuzonse,

ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda

zinthu pamodzi ndi thandizo;

adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,

2anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,

oweruza ndi aneneri,

anthu olosera ndi akuluakulu,

3atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka,

aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.

4Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo;

ana akhanda ndiwo adzawalamulire.

5Anthu adzazunzana,

munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake.

Anthu wamba adzanyoza

akuluakulu.

6Munthu adzagwira mʼbale wake

mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati,

“Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu;

lamulira malo opasuka ano!”

7Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti,

“Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake.

Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga;

musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”

8Yerusalemu akudzandira,

Yuda akugwa;

zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova,

sakulabadira ulemerero wa Mulungu.

9Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa;

amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu;

salibisa tchimo lawolo.

Tsoka kwa iwo

odziputira okha mavuto.

10Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino,

pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.

11Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo!

Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.

12Achinyamata akupondereza anthu anga,

ndipo amene akuwalamulira ndi akazi.

Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani;

akukuchotsani pa njira yanu.

13Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu;

wakonzeka kuti aweruze anthu ake.

14Yehova akuwazenga milandu

akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake:

“Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa;

nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.

15Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga,

nʼkudyera masuku pamutu amphawi?”

Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

16Yehova akunena kuti,

“Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri,

akuyenda atakweza makosi awo,

akukopa amuna ndi maso awo

akuyenda monyangʼama

akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo

17Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo;

Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”

18Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi, 19ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope, 20maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa, 21mphete ndi zipini, 22zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama, 23magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.

24Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha,

mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe;

mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi;

mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli;

mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.

25Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga,

asilikali ako adzafera ku nkhondo.

26Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira;

Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

Asante Twi Contemporary Bible

Yesaia 3:1-26

Yerusalem Ne Yuda Atemmuo

1Afei hwɛ, Awurade,

Asafo Awurade,

rebɛgyae deɛ ɔde ma

wɔ Yerusalem ne Yuda nyinaa:

aduane ne nsuo a ɔde ma wɔn nyinaa.

2Nnɔmmarima ne akofoɔ,

ɔtemmufoɔ ne odiyifoɔ,

nkɔmhyɛni ne ɔpanin,

3aduonum so panin ne deɛ ɔwɔ diberɛ,

ɔfotufoɔ, odwumfoɔ nyansafoɔ ne nkaberɛkyerefoɔ oniferefoɔ.

4“Mede mmerantewaa bɛyɛ wɔn nnwuma so mpanimfoɔ;

na mmɔfra adi wɔn so.”

5Nnipa bɛhyɛ wɔn ho wɔn ho so,

ɔbarima bɛtia ɔbarima, ɔyɔnko bɛtia ne yɔnko.

Mmabunu bɛsɔre atia wɔn mpanimfoɔ,

apapahwekwaa bɛtia onimuonyamfoɔ.

6Ɔbarima bɛsɔ ne nuanom baako mu

wɔ nʼagya efie aka sɛ,

“Wowɔ atadeɛ, bɛyɛ yɛn dikanfoɔ;

wɔ kuro a adane mmubuiɛ sie yi so.”

7Nanso, ɛda no ɔbɛteam sɛ,

“Menni deɛ mede bɛyɛ.

Menni aduane anaa ntoma wɔ me fie;

mfa me nyɛ nnipa no so dikanfoɔ.”

8Yerusalem retɔ ntintan,

Yuda rehwe ase;

wɔn nsɛm ne nneyɛeɛ tia Awurade.

Wɔmmu nʼanimuonyam a ɛwɔ wɔn mu.

9Sɛdeɛ wɔn anim teɛ no di adanseɛ tia wɔn;

wɔda wɔn bɔne adi te sɛ Sodom;

wɔmmfa nsie.

Nnome nka wɔn!

Wɔakɔfa amanehunu aba wɔn ho so.

10Ka kyerɛ teneneefoɔ sɛ ɛbɛsi wɔn yie,

ɛfiri sɛ wɔbɛdi wɔn nneyɛeɛ so aba.

11Nnome nka amumuyɛfoɔ!

Amanehunu wɔ wɔn so!

Wɔbɛtua wɔn so ka

wɔ deɛ wɔn nsa ayɛ no ho.

12Mmabunu hyɛ me nkurɔfoɔ so,

mmaa di wɔn so.

Ao me nkurɔfoɔ, mo akwankyerɛfoɔ ma mo yera;

wɔma mo mane firi kwantempɔn no so.

13Awurade tena ase wɔ nʼasɛnniiɛ.

Ɔma ne mu so bu nkurɔfoɔ no atɛn.

14Awurade bu atɛn

de tia ne nkurɔfoɔ mpanimfoɔ ne akannifoɔ sɛ,

“Mo na moasɛe me bobe turo;

apoobɔdeɛ a ɛfiri ahiafoɔ nkyɛn wɔ mo afie mu.

15Aseɛ ne sɛn enti na modwɛre me nkurɔfoɔ

na mode ahiafoɔ anim twitwiri fam?”

Sɛdeɛ Asafo Awurade seɛ nie.

16Awurade kasa sɛ,

“Sion mmammaa yɛ ahantan;

wɔnante toto wɔn kɔn,

wɔdeda wɔn ani akyi,

wɔtutu wɔn anammɔn ntiawa ntiawa,

na wɔn nan ase nkawa gyegye.

17Enti Awurade bɛma tikuro abɛgu Sion mmaa tiri ho.

Awurade bɛma wɔn tiri so apa.”

18Ɛda no Awurade bɛyiyi wɔn afɛfɛdeɛ: nkawa, ntomaban ne kɔnmuadeɛ, 19nsomuadeɛ, nkapo ne nkatanimu, 20Wɔn mmɔtire, ananse ntweaban, abɔwomu, nnuhwam ntoa ne nkaberɛ, 21ntimsoɔ mpɛtea ne hwenemu nkawa, 22ntadetenten pa, ngugusoɔ tiawa a ɛnni nsa, ntadeɛ yuu ne sika nkotokuo; 23nhwehwɛ, serekye ntadeɛ, tirinwi so nkawa ne abatiri so ngugusoɔ.

24Nkabɔne bɛsi deɛ ɛyɛ hwam anan mu;

ntampehoma bɛsi nkatakɔnmu anan mu;

tire a ɛso apa bɛsi tirinwi a wɔasiesie anan mu;

ayitoma bɛsi ntoma pa anan mu;

honam ani atwaatwa bɛsi ahoɔfɛ anan mu.

25Wo mmarima bɛtotɔ akofena ano,

wʼakofoɔ bɛtotɔ wɔ ɔko mu.

26Sion apono bɛtwa adwo, adi awerɛhoɔ;

na deɛ ɔnnibie bɛtena fam asu.