Yesaya 14 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 14:1-32

1Yehova adzachitira chifundo Yakobo;

adzasankhanso Israeli

ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo.

Alendo adzabwera kudzakhala nawo

ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.

2Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli

ku dziko lawo.

Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja

kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova.

Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo.

Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.

3Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani, 4mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti,

Wopsinja uja watha!

Ukali wake uja watha!

5Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa,

Iye waphwanya ndodo ya olamulira.

6Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali

powamenya kosalekeza,

Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali

ndikuwazunza kosalekeza.

7Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere;

ndipo akuyimba mokondwa.

8Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni

ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti,

“Chigwetsedwere chako pansi,

palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”

9Ku manda kwatekeseka

kuti akulandire ukamabwera;

mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri

a dziko lapansi, yadzutsidwa.

Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu

ayimiritsidwa pa mipando yawo.

10Onse adzayankha;

adzanena kwa iwe kuti,

“Iwenso watheratu mphamvu ngati ife;

Iwe wafanana ndi ife.”

11Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda,

pamodzi ndi nyimbo za azeze ako;

mphutsi zayalana pogona pako

ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi.

12Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba,

iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha!

Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi,

Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!

13Mu mtima mwako unkanena kuti,

“Ndidzakwera mpaka kumwamba;

ndidzakhazika mpando wanga waufumu

pamwamba pa nyenyezi za Mulungu;

ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako,

pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.

14Ndidzakwera pamwamba pa mitambo;

ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”

15Koma watsitsidwa mʼmanda

pansi penipeni pa dzenje.

16Anthu akufa adzakupenyetsetsa

nadzamalingalira za iwe nʼkumati,

“Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi

ndi kunjenjemeretsa maufumu,

17munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu,

amene anagwetsa mizinda yake

ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”

18Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu

aliyense mʼmanda akeake.

19Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako,

ngati nthambi yowola ndi yonyansa.

Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa;

amene anabayidwa ndi lupanga,

anatsikira mʼdzenje lamiyala

ngati mtembo woponderezedwa.

20Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu,

chifukwa unawononga dziko lako

ndi kupha anthu ako.

Zidzukulu za anthu oyipa

sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.

21Konzani malo woti muphere ana ake aamuna

chifukwa cha machimo a makolo awo;

kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi

ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.

22Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni.

Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo.

Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,”

akutero Yehova.

23“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu

ndiponso dambo lamatope;

ndidzawusesa ndi tsache lowononga,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Za Kulangidwa kwa Asiriya

24Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti,

“Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho,

ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.

25Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa;

ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga;

ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga,

ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”

26Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi,

ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.

27Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse?

Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?

Za Kulangidwa kwa Afilisti

28Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:

29Musakondwere inu Afilisti nonse

kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa;

chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri,

ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.

30Osaukitsitsa adzapeza chakudya

ndipo amphawi adzakhala mwamtendere.

Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala,

ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.

31Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda!

Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse!

Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto,

ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.

32Kodi tidzawayankha chiyani

amithenga a ku Filisitiya?

“Yehova wakhazikitsa Ziyoni,

ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

New Russian Translation

Исаия 14:1-32

1Время его близко,

и дни его не продлятся.

Господь пожалеет Иакова;

Он вновь изберет Израиль

и поселит их на их земле.

Чужеземцы присоединятся к ним

и пристанут к дому Иакова.

2Народы возьмут Израиля

и приведут на их место.

А дом Израиля завладеет народами

как слугами и служанками в Господней земле.

Они возьмут в плен тех, кто пленил их,

и будут править своими притеснителями.

3В тот день, когда Господь даст тебе облегчение от боли, смуты и жестокого рабства, 4ты запоешь о царе Вавилона эту язвительную песню:

Не стало гонителя!

Кончилась его ярость!14:4 Так в некоторых древних рукописях еврейского текста и в некоторых древних переводах; смысл этого слова в нормативном еврейском тексте неясен.

5Сломал Господь жезл нечестивых,

скипетр повелителей,

6который в гневе разил народы

нескончаемыми ударами

и в ярости народами правил

с безжалостным притеснением.

7Все страны в покое и мире,

запевают песни.

8Даже кипарисы и кедры Ливана

торжествуют над тобой, говоря:

«С тех пор, как ты уснул,

никто не приходит нас рубить».

9Пришел в движение мир мертвых14:9 Евр.: «шеол»; также в ст. 11 и 15.,

чтобы встретить тебя на входе.

Он будит духов умерших, чтобы тебя встречать, –

всех, кто был вождем на земле;

поднимает с престолов всех,

кто был у народов царем.

10Все они ответят, скажут тебе:

«Ты стал слаб, как мы; ты нам уподобился».

11Слава твоя сошла в мир мертвых,

вместе с пением твоих арф.

Личинки мух стелются под тобой,

черви – твой покров.

12Как пал ты с небес,

утренняя звезда, сын зари!

Низвергли на землю тебя,

того, кто попирал народы!

13А ты говорил в своем сердце:

«На небеса поднимусь,

вознесу свой престол

выше Божьих звезд,

и воссяду на горе собрания,

на краю севера14:13 Или: «на высотах (горы) Цафон»..

14Поднимусь на облачные высоты;

уподоблюсь Всевышнему».

15Но ты низведен в мир мертвых,

в глубины бездны14:12-15 В этом отрывке образ царя Вавилона сливается с образом сатаны, низверженного с небес (ср. Иез. 28:11-17; Лк. 10:18)..

16Видящие тебя всматриваются

и дивятся твоей судьбе:

«Тот ли это, кто колебал землю

и сотрясал царства,

17кто сделал мир пустыней,

разрушал его города

и не отпускал пленников домой?»

18Все цари народов почили во славе,

каждый лежит в своей гробнице14:18 Гробнице – букв.: «доме»..

19А ты – вне своей могилы,

выброшен, словно ненужная ветка14:19 Или: «мерзкая падаль».;

ты облачен убитыми,

пронзенными мечом,

нисходящими в каменистую пропасть.

Словно труп, попираемый ногами,

20ты не будешь погребен, как другие цари,

потому что ты разорил свою страну,

погубил свой народ.

Да не будут вовеки упоминаемы

потомки нечестивых!

21Готовьте бойню его сыновьям

из-за вины их отцов.

Да не поднимутся они, чтобы завладеть землей,

и не покроют мир своими городами.

22– Я поднимусь против них, –

возвещает Господь Сил, –

и отниму у Вавилона его имя и уцелевших,

его потомство и грядущие поколения, –

возвещает Господь. –

23Я превращу его во владения ежей

и в заболоченные пруды;

вымету его метлой уничтожения, –

возвещает Господь Сил.

Пророчество об Ассирии

24Господь Сил поклялся:

– Как Я задумал, так и будет;

как Я решил, так и случится:

25сокрушу ассирийцев в Моей земле;

на горах Моих растопчу их.

Будет снято их ярмо с Моего народа,

и их бремя с его плеч.

26Вот решение о всей земле;

вот рука, занесенная на все народы.

27Ведь Господь Сил решил,

и кто властен это отменить?

Рука Его занесена,

и кто властен ее удержать?

Пророчество о филистимлянах

28Следующее пророчество было в год смерти царя Ахаза14:28 Царь Ахаз умер приблизительно в 715 г. до н. э..

29Не радуйтесь, филистимляне,

что сломан поражавший вас жезл,

потому что от змеиного корня родится гадюка,

а плодом ее будет змея-стрелка14:29 Жезл и змеи символизируют ассирийских правителей, нападавших на филистимлян..

30Тогда беднейшие найдут пастбище,

и нищие будут покоиться в безопасности.

Но твой корень Я погублю голодом,

и уцелевших твоих Я убью14:30 Так в одной из древних рукописей еврейского текста и в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «он убьет»..

31Плачьте, ворота! Вой, город!

Замирайте от страха все вы, филистимляне!

Потому что облако пыли движется с севера –

это приближается войско,

и нет в его рядах отстающего.

32Что же ответить вестникам этого народа?

Что Господь утвердил Сион,

и в нем найдут убежище бедные из Его народа.