Yeremiya 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 1:1-19

1Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. 2Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. 3Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

4Yehova anayankhula nane kuti,

5“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,

iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;

ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

6Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

7Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. 8Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

9Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu

polowera pa zipata za Yerusalemu;

iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake

ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.

16Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo

chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.

Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,

ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

New Russian Translation

Иеремия 1:1-19

Пролог

1Слова Иеремии, сына Хелкии, одного из священников Анатота, что в земле Вениамина. 2Слово Господа было к нему в тринадцатом году1:2 В 627 г. до н. э. правления Иосии, сына Амона, царя Иудеи. 3Господь продолжал возвещать ему Свое слово во времена правления Иоакима, сына Иосии, царя Иудеи, до пятого месяца одиннадцатого года правления Цедекии1:3 В августе 586 г. до н. э., сына Иосии, царя Иудеи, когда жители Иерусалима были уведены в плен.

Призвание Иеремии

4И было ко мне слово Господне:

5– Прежде чем Я образовал тебя во чреве, Я уже знал1:5 Или: «избрал». тебя,

прежде чем ты вышел из утробы, Я избрал тебя;

Я назначил тебя пророком для народов.

6Я ответил:

– О Владыка Господь!1:6 Евр.: «Адонай ЙГВГ». Я не умею говорить, ведь я слишком молод.

7Но Господь сказал мне:

– Не говори: «Я еще молод». Ты пойдешь ко всем, к кому Я пошлю тебя, и будешь говорить все, что Я повелю тебе. 8Не бойся их, потому что Я с тобой, и Я спасу тебя, – сказал Господь.

9Господь простер руку, коснулся моих уст и сказал мне:

– Вот, Я вложил слова Мои в твои уста. 10Смотри, сегодня Я поставлю тебя над народами и царствами, чтобы искоренять и ломать, губить и разрушать, строить и насаждать.

11И было ко мне слово Господне:

– Что ты видишь, Иеремия?

– Вижу ветку миндального1:11 Евр.: «шакед». дерева, – ответил я.

12– Верно разглядел, – сказал мне Господь, – ведь Я бодрствую1:12 На языке оригинала: «шокед», что близко по звучанию к слову «шакед» – «миндаль». над Моим словом, чтобы его исполнить.

13Вновь было ко мне слово Господне:

– Что ты видишь?

– Вижу кипящий котел – он движется с севера, – ответил я.

14– С севера хлынет беда на всех, кто живет в этой стране, – сказал мне Господь. – 15Ведь Я призываю все народы северных царств, – возвещает Господь. –

Они придут и поставят свои престолы

у ворот Иерусалима,

вокруг всех окружающих его стен,

у всех городов Иудеи.

16Я оглашу приговор им

за все их злодеяния: они оставили Меня,

и возжигали благовония чужим богам,

и поклонялись делам своих рук.

17Соберись! Встань и скажи им все, что Я тебе повелю. Не бойся их, не то Я сокрушу тебя перед ними. 18Сегодня Я сделал тебя укрепленным городом, железной колонной и бронзовой стеной, чтобы дать отпор всей этой земле – царям Иудеи, ее вельможам, священникам и народу этой страны. 19Они будут воевать против тебя, но не одолеют, потому что Я с тобой и спасу тебя, – возвещает Господь.