Yesaya 13 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 13:1-22

Kulangidwa Kwa Babuloni

1Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:

2Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,

muwafuwulire ankhondo;

muwakodole kuti adzalowe pa zipata

za anthu olemekezeka.

3Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;

ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira

amene amadzikuza ndi chipambano changa.

4Tamvani phokoso ku mapiri,

likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!

Tamvani phokoso pakati pa maufumu,

ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!

Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera

kuchita nkhondo.

5Iwo akuchokera ku mayiko akutali,

kuchokera kumalekezero a dziko

Yehova ali ndi zida zake za nkhondo

kuti adzawononge dziko la Babuloni.

6Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

7Zimenezi zinafowoketsa manja onse,

mtima wa munthu aliyense udzachokamo.

8Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,

zowawa ndi masautso zidzawagwera;

adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.

Adzayangʼanana mwamantha,

nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.

9Taonani, tsiku la Yehova likubwera,

tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;

kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu

ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.

10Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga

sizidzaonetsa kuwala kwawo.

Dzuwa lidzada potuluka,

ndipo mwezi sudzawala konse.

11Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,

anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.

Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,

ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.

12Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.

Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.

13Tsono ndidzagwedeza miyamba

ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.

Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse

pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.

14Ngati mbawala zosakidwa,

ngati nkhosa zopanda wozikusa,

munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,

aliyense adzathawira ku dziko lake.

15Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa

adzaphedwa momubaya ndi lupanga.

16Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;

nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.

17Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva

ndipo sasangalatsidwa ndi golide,

kuti amenyane ndi Ababuloni.

18Adzapha anyamata ndi mauta awo;

sadzachitira chifundo ana

ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.

19Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.

Anthu ake amawunyadira.

Koma Yehova adzawuwononga

ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.

20Anthu sadzakhalamonso

kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;

palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,

palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.

21Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,

nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;

mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,

ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.

22Mu nsanja zake muzidzalira afisi,

mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.

Nthawi yake yayandikira

ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

New Russian Translation

Исаия 13:1-22

Пророчество о Вавилоне

1Пророчество о Вавилоне, которое видел Исаия, сын Амоца.

2Поднимите на голой вершине знамя,

кричите им;

подайте им знак рукой,

чтобы шли в ворота знатных.

3Я дал повеление Моим святым;

Я призвал Моих воинов, чтобы излить Мой гнев,

тех, кто радуется Моим победам.

4Слышен шум на горах,

как от огромной толпы!

Слышен мятежный шум царств,

народов, собравшихся вместе!

Созывает Господь Сил

войско к битве.

5Они идут из далеких земель,

от края небес;

Господь и орудия гнева Его идут,

чтобы погубить всю страну.

6Плачьте, потому что день Господа близок;

он придет, как гибель от Всемогущего13:6 Евр.: «Шаддай»..

7Из-за этого ослабнут все руки,

и у всякого дрогнет сердце.

8Они ужаснутся,

боль и судороги их схватят,

будут мучиться, словно роженица;

будут смотреть друг на друга в изумлении,

лица их будут пылать.

9Вот, наступает день Господа –

жестокий день с негодованием и пылающим гневом,

чтобы опустошить страну

и истребить в ней грешников.

10Звезды небесные и созвездия

не прольют своего света.

Восходящее солнце померкнет,

и луна не даст света своего.

11Я накажу мир за его зло,

нечестивых – за их грехи.

Я положу конец гордыне надменных

и унижу гордость безжалостных.

12Я сделаю так, что люди станут

реже чистого золота,

реже золота из Офира.

13Для этого Я сотрясу небеса,

и тронется с места своего земля

от негодования Господа Сил,

в день Его пылающего гнева.

14Тогда, как газель от погони,

как овцы без пастуха,

каждый побежит к своему народу,

устремится в свою землю.

15Но кто попадется – того пронзят,

и кто будет схвачен – падет от меча.

16Разобьют их младенцев у них на глазах;

дома их разграбят, их жен обесчестят.

17– Вот, Я подниму против них мидян,

которые серебра не ценят

и к золоту равнодушны.

18Луки их сразят юношей;

не пожалеют они младенцев,

на детей не взглянут с состраданием.

19Вавилон, жемчужина царств,

гордость и слава халдеев13:19 То есть вавилонян; евр.: «касдим»; также в остальных местах книги.,

будет Богом низвержен,

как Содом и Гоморра13:19 См. Быт. 18:20–19:29..

20Не заселится он никогда,

из поколения в поколение обитаем не будет;

не раскинет там араб свой шатер,

не остановит пастух овец на отдых.

21Там залягут звери пустыни,

шакалы наполнят его дома;

там будут жить совы

и плясать дикие козлы13:21 Дикие козлы – это же иудейское слово используется и в Лев. 17:7; 2 Пар. 11:15, где говорится об идолах в образе козла. Кроме того, в Вавилоне существовал культ поклонения козлообразному божеству. На основании вышесказанного, многие толкователи думают, что здесь говорится о демонах, которые будут обитать, вместе с ритуально нечистыми животными, на развалинах Вавилона (см. Отк. 18:2)..

22Гиены будут выть в его башнях,

шакалы – в его дворцах.