Yeremiya 46 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 46:1-28

1Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.

Uthenga Wonena za Igupto

2Kunena za Igupto:

Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,

3anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo,

ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!

4Mangani akavalo,

ndipo kwerani inu okwerapo!

Khalani pa mzere

mutavala zipewa!

Nolani mikondo yanu,

valani malaya anu ankhondo!

5Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani?

Achita mantha

akubwerera,

ankhondo awo agonjetsedwa.

Akuthawa mofulumirapo

osayangʼananso mʼmbuyo,

ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,”

akutero Yehova.

6Waliwiro sangathe kuthawa

ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka.

Akunka napunthwa ndi kugwa

kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.

7“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo,

ngati mtsinje wa madzi amkokomo?

8Igupto akusefukira ngati Nailo,

ngati mitsinje ya madzi amkokomo.

Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi;

ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’

9Tiyeni, inu akavalo!

Thamangani inu magaleta!

Tulukani, inu ankhondo,

ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango,

ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.

10Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse;

tsiku lolipsira, lolipsira adani ake.

Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi,

lidzaledzera ndi magazi.

Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe

mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.

11“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala

iwe namwali Igupto.

Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira;

palibe mankhwala okuchiritsa.

12Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako;

kulira kwako kwadzaza dziko lapansi.

Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana,

onse awiri agwa pansi limodzi.”

13Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:

14“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli.

Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi.

Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza,

chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’

15Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa?

Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.

16Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa.

Aliyense akuwuza mnzake kuti,

‘Tiyeni tibwerere kwathu,

ku dziko kumene tinabadwira,

tithawe lupanga la adani athu.’

17Kumeneku iwo adzafuwula kuti,

‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti,

Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’

18“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu,

imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse,

“wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena,

ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.

19Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo

inu anthu a ku Igupto,

pakuti Mefisi adzasanduka chipululu

ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.

20“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola,

koma chimphanga chikubwera

kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.

21Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye

ali ngati ana angʼombe onenepa.

Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi.

Palibe amene wachirimika.

Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira;

ndiyo nthawi yowalanga.

22Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa

pamene adani abwera ndi zida zawo,

abwera ndi nkhwangwa

ngati anthu odula mitengo.

23Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,”

akutero Yehova,

“ngakhale kuti ndi yowirira.

Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe,

moti sangatheke kuwerengeka.

24Anthu a ku Igupto achita manyazi

atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”

25Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira. 26Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.

27“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha;

usataye mtima, iwe Israeli.

Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali,

ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo.

Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere,

ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.

28Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha,

pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova.

“Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu

a ku mayiko kumene ndakupirikitsira,

Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu.

Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera;

sindidzakulekerera osakulanga.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 46:1-28

Пророчество о Египте

1Вот слово Вечного, которое было к Иеремии о судьбах других народов.

2О Египте, о войске египетского фараона Нехо46:2 Нехо II, правивший Египтом с 610 по 595 гг. до н. э., пошёл на помощь Ашшурубаллиту II, последнему царю Ассирии, воевавшему с Вавилоном., которое было разбито Навуходоносором, царём Вавилона, при Каркемише на реке Евфрат в четвёртом году правления иудейского царя Иоакима, сына Иосии (в 605 г. до н. э.).

3– Готовьте щиты, и большие, и малые,

и выступайте в бой!

4Седлайте коней и садитесь на них!

Надевайте шлемы и становитесь в строй!

Точите копья и надевайте кольчуги!

5Но что Я вижу?

Они испугались,

они отступают,

их воины побеждены.

Они бегут без оглядки,

и ужас со всех сторон, –

возвещает Вечный. –

6Быстрый не сможет убежать,

и сильный не спасётся.

На севере у реки Евфрат

они споткнутся и упадут.

7Кто там вздымается, как Нил,

как реки с бурными водами?

8Египет вздымается, как Нил,

как реки с бурными водами,

говоря: «Поднимусь и покрою землю;

погублю города и их жителей».

9Скачите, кони!

Мчитесь, колесничие!

Выступайте, сильные воины:

воины Эфиопии и Ливии46:9 Букв.: «Пута»., держащие щиты,

и воины Лидии, натягивающие луки.

10Это день Владыки Вечного, Повелителя Сил,

день возмездия для отмщения Его врагам.

Будет меч пожирать, пока не насытится,

пока не утолит жажду кровью.

Это жертва Владыке Вечному, Повелителю Сил,

в северных землях у реки Евфрат.

11– Пойди в Галаад и возьми бальзам46:11 Галаад славился своим целебным бальзамом из смолы мастикового дерева.,

девственная дочь Египта46:11 Девственная дочь Египта – олицетворение Египта. Также в ст. 24..

Напрасно ты лечишься многими снадобьями –

нет тебе исцеления.

12Народы услышали про твой позор;

твой крик наполнил землю.

Споткнулся о воина воин,

и упали оба разом.

13Вот слово, которое Вечный сказал пророку Иеремии о будущем вторжении Навуходоносора, царя Вавилона, в Египет:

14– Объявляйте в Египте,

возвещайте в Мигдоле;

возвещайте и в Мемфисе46:14 Букв.: «Нофе»; так же в ст. 19., и в Тахпанхесе:

«Становись и готовься, Египет:

меч уже пожирает тех, кто вокруг тебя».

15Почему твои воины будут повержены?

Они не смогут выстоять,

потому что Вечный повергнет их.

16Они будут спотыкаться снова и снова,

будут падать один на другого и говорить:

«Вставайте, давайте вернёмся

к своему народу, на нашу родину,

подальше от меча притеснителя».

17Они воскликнут:

«Фараон, царь Египта, – крикун,

упустивший свою возможность».

18Верно, как и то, что Я живу, – возвещает Царь,

Чьё имя Вечный, Повелитель Сил, –

придёт тот, кто велик, как гора Фавор среди гор

и как гора Кармил у моря.

19Собирайте свои пожитки

и готовьтесь к изгнанию, жители Египта,

потому что Мемфис подвергнется разорению,

станет необитаемой развалиной.

20Египет – прекрасная телица,

но с севера летит к ней слепень.

21Даже наёмники в войске Египта

как тучные быки.

Но они повернутся и вместе пустятся в бегство

и не устоят,

потому что настал день их бедствий,

время их наказания.

22Зашипит Египет, как уползающий змей,

так как близятся вражьи войска,

и пойдут они на него с топорами,

как дровосеки.

23Они вырубят его лес, –

возвещает Вечный, –

как бы ни был он густ,

ведь они многочисленнее саранчи,

нет им числа.

24Дочь Египта будет опозорена,

отдана в руки северного народа.

25Вечный, Повелитель Сил, Бог Исроила говорит:

– Я накажу Амона, бога города Фивы46:25 Букв.: «города Но»., и фараона, и Египет, и всех его богов и царей, и тех, кто полагается на фараона. 26Я отдам их в руки тех, кто ищет их смерти, – Навуходоносору, царю Вавилона, и его слугам. Потом Египет будет снова населён людьми, как и в прежние времена, – возвещает Вечный.

27– А ты не бойся, раб Мой Якуб;

не пугайся, Исроил.

Я вызволю тебя из далёкого края,

твоё потомство – из земли его пленения.

Якуб вернётся к спокойной и мирной жизни,

и никто не будет его устрашать.

28Не бойся же, раб Мой Якуб,

потому что Я с тобой, –

возвещает Вечный. –

Я истреблю все народы,

среди которых рассеял тебя,

а тебя не истреблю.

Я накажу тебя по справедливости,

но безнаказанным не оставлю тебя.