Yeremiya 45 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 45:1-5

Uthenga kwa Baruki

1Uwu ndi uthenga umene mneneri Yeremiya anawuza Baruki mwana wa Neriya mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa mwana ya Yosiya kuti alembe mʼbuku. 2“Yehova Mulungu wa Israeli, akunena kwa iwe Baruki kuti: 3Iwe unati, ‘Kalanga ine! Yehova wawonjezera chisoni pa mavuto anga. Ine ndatopa ndi kubuwula ndipo sindikupeza mpumulo.’ ”

4Koma Yehova akukuwuza kuti, “Ndidzagwetsa chimene ndinamanga ndipo ndidzazula chimene ndinadzala. Ndidzachita zimenezi mʼdziko lonse. 5Kodi tsono ukudzifunira wekha zinthu zazikulu? Usadzifunire. Pakuti ndidzagwetsa mavuto pa anthu onse, koma ndidzasunga moyo wako kulikonse kumene ungadzapite.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 45:1-5

Послание Баруху

1Вот что сказал пророк Иеремия Баруху, сыну Нерии, в четвёртом году правления иудейского царя Иоакима, сына Иосии (в 605 г. до н. э.), после того, как Барух записал в свиток слова, которые продиктовал ему Иеремия45:1 См. 36:1-4, 32.:

2– Так говорит Вечный, Бог Исроила, тебе, Барух: 3«Ты говорил: „Горе мне! Вечный прибавил скорбь к моим мукам; я устал от стонов и не нахожу покоя“».

4Скажи ему: «Так говорит Вечный: Я разрушу то, что построил, и искореню то, что насадил, во всей этой стране. 5Тебе ли искать для себя чудес? Не ищи. Я насылаю беду на всякую плоть, – возвещает Вечный, – но куда бы ты ни отправился, Я спасу тебя».