Oweruza 20 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 20:1-48

Aisraeli Achita Nkhondo ndi Fuko la Benjamini

1Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa. 2Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga. 3Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”

4Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko. 5Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa. 6Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli. 7Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”

8Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake. 9Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene. 10Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.” 11Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.

12Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani? 13Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.”

Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo. 14Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli. 15Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa. 16Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.

17Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.

18Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?”

Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”

19Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya. 20Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya. 21A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko. 22Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja. 23Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?”

Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”

24Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo. 25Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.

26Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova. 27Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko. 28Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?”

Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”

29Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya. 30Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba. 31Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.

32Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”

33Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba. 34Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera. 35Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo. 36Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa.

Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya. 37Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga. 38Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo, 39ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo.

Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.” 40Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba. 41Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera. 42Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo. 43Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya. 44Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa. 45Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.

46Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa. 47Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi. 48Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.

Bibelen på hverdagsdansk

Dommerbogen 20:1-48

Benjaminitterne straffes

1Da samledes alle Israels mænd—fra Dan i nord til Be’ersheba i syd og fra Gilead i øst—for Herrens ansigt i Mitzpa. 2Alle Israels stammeledere mødte op, og alle stammerne mønstrede tilsammen 400.000 bevæbnede krigere. 3-4(Benjaminitterne hørte, at alle de andre stammer havde forsamlet sig i Mitzpa.)

„Fortæl os nu, hvordan den forbrydelse gik til,” sagde folkets ledere til den myrdede kvindes mand.

„Jeg og min medhustru ankom til Gibea i Benjamins land for at overnatte,” begyndte han. 5„Om natten omringede nogle af byens mænd huset i den hensigt at slå mig ihjel, og de voldtog min medhustru, indtil hun døde. 6Derefter skar jeg hendes lig i 12 stykker og sendte stykkerne ud til Israels 12 stammer for at vise, hvilken afskyelig forbrydelse disse israelitter havde begået. 7Nu må det være op til forsamlingen her at beslutte, hvad der skal gøres.”

8-11Alle rejste sig, og deres beslutning var enstemmig: „Ingen af os vender hjem, før vi har udført en hævnaktion mod Gibea. Vi vil udtage en tiendedel af hæren til at sørge for forsyningslinierne—og resten af os vil udslette Gibea for den afskyelige forbrydelse, der er begået blandt Israels folk. Hvem der skal være hærens fortrop, vil blive bestemt ved lodkastning.”

12Så sendte man delegationer ud til hele Benjaminstammens område med følgende besked: „Hvad er det dog for en skamløs handling, der er blevet begået hos jer? 13Udlever de onde mænd fra Gibea til os, så vi kan henrette dem og på den måde udrydde det onde fra Israels midte.” Men benjaminitterne ville ikke høre på dem. 14-15I stedet samlede de en hær på 26.000 mand og sendte hæren til Gibea for at hjælpe byens 700 våbenføre mænd imod den israelitiske hær. 16I hæren var der 700 udvalgte, venstrehåndede skarpskytter, der med deres stenslynger kunne ramme plet hver eneste gang. 17Over for dem stod de 400.000 krigere fra de øvrige stammer.

18Før slaget gik israelitterne til Betel for at rådspørge Gud. „Hvilken stamme skal danne fortrop i slaget mod benjaminitterne?” spurgte de. Herren svarede: „Judas stamme skal gå forrest.”

19-20Tidligt næste morgen drog hæren af sted og slog lejr tæt ved Gibea. Derfra gik de til angreb mod byen, 21men benjaminitterne stormede ud af byen og dræbte den dag 22.000 israelitter. 22-24Da gik israelitterne op til Betel og græd for Herrens ansigt indtil aften. „Skal vi fortsætte kampen imod benjaminitterne, som dog er en del af vores eget folk?” spurgte de. Herren svarede: „Ja, gå i kamp imod dem igen!”

Så opmuntrede israelitterne hinanden og gjorde klar til at fortsætte kampen samme sted næste dag. 25Men denne gang gik det ikke meget bedre, for benjaminitterne dræbte yderligere 18.000 krigere.

26Da gik hele hæren op til Betel. De græd og fastede indtil aften og bragte brænd- og takofre til Herren. 27-28På det tidspunkt var Guds Ark flyttet til Betel, og Pinehas, en søn af Arons søn Eleazar, var præst ved helligdommen. Israelitterne spurgte atter Herren: „Skal vi fortsætte kampen imod benjaminitterne?” Herren svarede: „Fortsæt! I morgen vil jeg give jer sejr over dem.”

29Så lagde en del af israelitterne sig i baghold på markerne rundt om byen. 30Næste morgen gik den øvrige del af hæren frontalt til angreb mod Gibea som de øvrige dage. 31Da benjaminitterne nu stormede ud af byen for at gå til modangreb, trak israelitterne sig tilbage i tre retninger og lokkede benjaminitterne væk fra byen. Benjaminitterne forfulgte de israelitiske soldater og huggede 30 af dem ned dels ude på markerne, dels langs vejen mod nordvest til Gibeon20,31 På hebraisk ligner de to navne „Gibea” og „Gibeon” hinanden meget. Selvom den hebraiske tekst, vi har adgang til, siger „Gibea”, er det sandsynligt, at originalen har sagt „Gibeon”, da det passer bedre i sammenhængen. og mod nord til Betel. 32Det fik dem til at tænke: „Vi slår dem også denne gang!” Men israelitternes slagplan gik jo ud på, at deres hær skulle flygte og derved lokke modstanderne bort fra byen. 33Da deres hovedstyrker nåede Ba’al-Tamar, forskansede de sig og gik til modangreb. I mellemtiden kom de andre frem fra deres baghold og indtog Gibea uden at møde væsentlig modstand. 34Det drejede sig om 10.000 af israelitternes bedste krigere. Samtidig var der voldsom kamp mellem hovedstyrken og Benjamins hær, der var uvidende om, at det snart var ude med dem. 35Den dag gav Herren israelitterne sejr over Benjamins hær, der med et tab på 25.100 mand blev næsten totalt udslettet. 36Da måtte benjaminitterne acceptere, at de var blevet slået.

Bagholdsangrebet og kampens afslutning foregik på følgende måde: Den israelitiske hovedstyrke havde jo trukket sig væk fra benjaminitterne, da de satsede på deres bagholdsstrategi. 37Den øvrige hærstyrke kom nu frem fra sit baghold, stormede Gibea og huggede indbyggerne ned. 38Det var aftalt, at de skulle sætte ild til byen, og det gjorde de så. 39Da israelitternes hovedstyrke så røgen, standsede de flugten og gik til modangreb på benjaminitternes hær. Da benjaminitterne allerede havde hugget 30 israelitiske soldater ned, og hele hæren var flygtet, var de overbeviste om, at sejren var en realitet ligesom de to foregående dage, 40-41men da de så sig tilbage mod byen fik de et chok, for byen var i brand, og fjenderne kom imod dem både fra syd og nord. 42Deres eneste udvej var at flygte i retning af ørkenen, men hovedstyrken og krigerne fra bagholdet, som nu havde sluttet sig til dem, satte efter benjaminitterne. 43-44Et godt stykke øst for Gibea blev de indhentet, og mere end 18.000 af Benjamins krigere blev slået ihjel dér. 45Resten af hæren flygtede videre mod nord ind i ørkenen i retning af Rimmons klippe, og endnu 5000 mand blev hugget ned undervejs. 2000 mand nåede frem til Gidom, inden de blev dræbt.

46Den dag mistede Benjamins stamme mere end 25.000 dygtige krigere. 47De eneste overlevende var 600 mænd, der undslap til Rimmons klippe og gemte sig i ørkenområdets klippehuler. Her levede de i fire måneder.

48Efter slaget gik israelitterne en runde til hver eneste by i Benjamins land. De dræbte alt levende, både mennesker og husdyr, og derefter brændte de byerne ned til grunden.