Rute 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Rute 1:1-22

Naomi ndi Rute

1Mu nthawi imene oweruza ankalamulira Israeli, munali njala mʼdziko, ndipo munthu wina wa ku Betelehemu mʼdziko la Yuda anapita pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake aamuna awiri, kukakhala ku Mowabu kwa nthawi yochepa. 2Dzina la munthuyo linali Elimeleki, dzina la mkazi wake linali Naomi, ndipo mayina a ana awo aamuna anali Maaloni ndi Kiliyoni. Iwo anali Aefurati ochokera ku Betelehemu ku Yuda. Ndipo anapita kukakhala ku Mowabu.

3Kenaka Elimeleki, mwamuna wake wa Naomi anamwalira ndipo Naomiyo anatsala ndi ana ake aamuna awiri aja.

4Iwo anakwatira akazi a Chimowabu; wina dzina lake Oripa ndi wina Rute. Atakhala kumeneko pafupifupi zaka khumi, 5Maloni ndi Kiliyoni anamwaliranso kotero kuti Naomi anatsala yekha wopanda ana ake awiri aja ndi mwamuna wake.

6Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kubwerera kwawo kuchokera ku Mowabu popeza anali atamva ali ku Mowabuko kuti Yehova anakomera mtima anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.

7Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.

8Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, “Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.

9“Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.

10Ndipo anati kwa Naomi, “Ife tipita nawo kwa anthu akwanu.”

11Koma Naomi anati, “Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu? 12Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna, 13kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike.”

14Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.

15Naomi anati “Taona, mʼbale wako wabwerera kwawo kwa anthu ake ndi kwa milungu yake. Bwerera nawenso umulondole mʼbale wako.”

16Koma Rute anayankha kuti, “Musandikakamize kuti ndikusiyeni kapena kuti ndibwerere osakutsatani. Kumene inu mupite ine ndipita komweko, ndipo kumene mukakhale inenso ndikakhala komweko. Abale anu adzakhala abale anga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga. 17Kumene mukafere inenso ndidzafera komweko ndipo komweko ndikayikidwa mʼmanda. Yehova andichite choyipa chingakule motani, ngati china chingatirekanitse ife kupatula imfa.”

18Naomi atazindikira kuti Rute watsimikiza kupita naye, analeka kumukakamiza.

19Choncho amayi awiriwo anapitiriza ulendo wawo mpaka anakafika ku Betelehemu. Pamene ankafika mu Betelehemu, anthu onse a mʼmudzimo anatekeseka chifukwa cha iwowo ndipo amayi ambiri ankanena kuti, “Kodi uyu nʼkukhala Naomi?”

20Iye anawawuza kuti, “Musanditchenso Naomi. Muzinditchula ine kuti Mara, chifukwa Wamphamvuzonse wandizunza kwambiri. 21Ine ndinapita wolemera, koma Yehova wabwera nane wopanda kanthu. Nanga munditchulirenji Naomi pamene Yehova wandisautsa. Wamphamvuzonse uja wandigwetsera mavuto owawa.”

22Naomi anabwerera kuchoka ku dziko la Mowabu pamodzi ndi Rute mpongozi wake. Ndipo anafika ku Betelehemu nthawi yoyamba kukolola barele.

Bibelen på hverdagsdansk

Ruths Bog 1:1-22

Ruths troskab imod No’omi

1-2Engang under dommertiden i Israel blev landet ramt af en voldsom hungersnød. En mand ved navn Elimelek af Efrat-slægten flyttede derfor fra Betlehem i Juda til Moabs land for at bo der som fremmed sammen med sin kone, No’omi, og deres to sønner, Malon og Kiljon. 3Mens de boede i Moab, døde Elimelek, så No’omi sad alene tilbage med sine to sønner. 4-5De to unge mænd fandt sig hver en kone blandt moabitterne. Malon giftede sig med en pige, der hed Ruth, og Kiljon giftede sig med Orpa. Da de havde boet i Moab i hen ved ti år, døde både Malon og Kiljon, og No’omi var nu helt alene—uden mand og børn.

6-7På den tid fik hun at vide, at Herren havde forbarmet sig over sit folk, så der igen var mad at få i Juda. Derfor besluttede hun at forlade Moab og vende tilbage til sit hjem i Betlehem. Sammen med sine to svigerdøtre begav hun sig af sted ad vejen til Juda.

8Da de havde gået et stykke tid, sagde No’omi til sine svigerdøtre: „Det er bedst, I går hjem til jeres forældre. Må Herren vise jer sin godhed på grund af den godhed, I har vist mod mine to sønner og mig, 9og må han hjælpe jer begge til at blive gift igen og få et godt og trygt hjem.” Så kyssede hun dem farvel, og de brast i højlydt gråd.

10„Men vi vil gerne følge med dig hjem til dit folk!” sagde de to unge kvinder.

11„Nej, I må hellere vende tilbage til jeres eget folk,” svarede No’omi. „Jeg har jo ikke andre sønner, I kan blive gift med. 12Derfor er det bedst, at I vender tilbage til jeres familier. Jeg er for gammel til at gifte mig igen—og selv om jeg gjorde, og jeg blev gravid og fødte sønner med det samme, 13ville I så vente til de blev voksne? Nej, mine piger! For mig er det mere bittert end for jer, for det er Herrens hånd, som har ramt mig med denne tragedie!”

14Så græd de igen. Orpa kyssede nu sin svigermor farvel og vendte om for at gå tilbage til sit barndomshjem, men Ruth ville ikke forlade No’omi.

15„Se, din svigerinde er allerede på vej tilbage til sit folk og sin gud,” sagde No’omi. „Du må hellere følge med.”

16Men Ruth svarede: „Tving mig ikke til at forlade dig! Hvor du går hen, vil jeg gå med. Dit hjem skal være mit hjem, dit folk skal være mit folk, og din Gud skal være min Gud. 17Og når jeg engang dør, vil jeg begraves ved din side. Må Herren straffe mig, hvis jeg tillader noget andet end døden at skille os!”

18Da No’omi så, at Ruth var fast besluttet på at gå med, holdt hun op med at forsøge at overtale hende. 19De to fortsatte så rejsen og ankom til Betlehem.

Der blev røre i hele byen ved deres ankomst.

„Jamen, er det ikke No’omi?” udbrød byens kvinder.

20Men No’omi sagde: „Kald mig ikke længere No’omi1,20 „No’omi” betyder „dejlig, elskelig, sød”.—kald mig hellere Mara!1,20 „Mara” betyder „bitter”. Den almægtige Gud har gjort mit liv bittert. 21Da jeg rejste herfra, havde jeg hele min familie, men nu vender jeg alene tilbage. Kald mig ikke No’omi, for Herren har dømt mig og ladet denne tragedie ramme mig!”

22Således vendte No’omi tilbage til Betlehem, og hun havde sin svigerdatter med fra Moabs land. Byghøsten var netop begyndt, da de ankom.