Obadiya 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Obadiya 1:1-21

Masomphenya a Obadiya

1Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,

“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;

udzanyozedwa kwambiri.

3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe

ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,

iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,

‘Ndani anganditsitse pansi?’

4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga

ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,

kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,

aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!

Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

Ngati anthu othyola mphesa akanafika,

kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,

chuma chake chobisika chidzabedwa!

7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;

abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;

amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,

koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,

kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,

anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?

9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,

ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau

adzaphedwa pa nkhondo.

10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,

udzakhala wamanyazi;

adzakuwononga mpaka muyaya.

11Pamene adani

ankamulanda chuma chake

pamene alendo analowa pa zipata zake

ndi kuchita maere pa Yerusalemu,

pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.

12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako

pa nthawi ya tsoka lake,

kapena kunyogodola Ayuda

chifukwa cha chiwonongeko chawo,

kapena kuwaseka pa nthawi ya

mavuto awo.

13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga

pa nthawi ya masautso awo,

kapena kuwanyogodola

pa tsiku la tsoka lawo,

kapena kulanda chuma chawo

pa nthawi ya masautso awo.

14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu

kuti uphe Ayuda othawa,

kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka

pa nthawi ya mavuto awo.”

15“Tsiku la Yehova layandikira

limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.

Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;

zochita zako zidzakubwerera wekha.

16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,

koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;

iwo adzamwa ndi kudzandira

ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;

phirilo lidzakhala lopatulika,

ndipo nyumba ya Yakobo

idzalandira cholowa chake.

18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto

ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;

nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,

ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.

Sipadzakhala anthu opulumuka

kuchokera mʼnyumba ya Esau.”

Yehova wayankhula.

19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala

ku mapiri a Esau,

ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri

adzatenga dziko la Afilisti.

Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,

ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.

20Aisraeli amene ali ku ukapolo

adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;

a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi

adzalandira mizinda ya ku Negevi.

21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni

ndipo adzalamulira mapiri a Esau.

Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

New International Reader’s Version

Obadiah 1:1-21

Obadiah’s Vision

1This is the vision about Edom that Obadiah had.

Here is what the Lord and King says about Edom.

We’ve heard a message from the Lord.

A messenger was sent to the nations.

The Lord told him to say,

“Get up! Let us go and make war against Edom.”

2The Lord says to Edom,

“I will make you weak among the nations.

They will look down on you.

3You live in the safety of the rocks.

You make your home high up in the mountains.

But your proud heart has tricked you.

So you say to yourself,

‘No one can bring me down to the ground.’

4You have built your home as high as an eagle does.

You have made your nest among the stars.

But I will bring you down from there,”

announces the Lord.

5“Edom, suppose robbers came to you at night.

They would steal only as much as they wanted.

Suppose grape pickers came to harvest your vines.

They would still leave a few grapes.

But you are facing horrible trouble!

6People of Esau, everything will be taken away from you.

Your hidden treasures will be stolen.

7All those who are helping you

will force you to leave your country.

Your friends will trick you and overpower you.

Those who eat bread with you

will set a trap for you.

But you will not see it.”

8Here is what the Lord announces. “At that time

I will destroy the wise men of Edom.

I will wipe out the men of understanding

in the mountains of Esau.

9People of Teman, your soldiers will be terrified.

Everyone in Esau’s mountains

will be cut down by swords.

10You did harmful things to the people of Jacob.

They are your relatives.

So you will be covered with shame.

You will be destroyed forever.

11Outsiders entered the gates of Jerusalem.

They cast lots to see what each one would get.

Strangers carried off its wealth.

When that happened, you just stood there and did nothing.

You were like one of them.

12That was a time of trouble for your relatives.

So you shouldn’t have been happy about what happened to them.

The people of Judah were destroyed.

So you should not have been happy about it.

You should not have laughed at them so much

when they were in trouble.

13You should not have marched

through the gates of my people’s city

when they were in trouble.

You shouldn’t have been happy about what happened to them.

You should not have stolen their wealth

when they were in trouble.

14You waited where the roads cross.

You wanted to cut down those who were running away.

You should not have done that.

You handed over to their enemies

those who were still left alive.

You should not have done that.

They were in trouble.

15“The day of the Lord is near

for all the nations.

Others will do to you

what you have done to them.

You will be paid back

for what you have done.

16You Edomites made my holy mountain of Zion impure

by drinking and celebrating there.

So all the nations will drink

from the cup of my anger.

And they will keep on drinking from it.

They will vanish.

It will be as if they had never existed.

17But on Mount Zion some of my people will be left alive.

I will save them.

Zion will be my holy mountain once again.

And the people of Jacob

will again receive the land as their own.

18They will be like a fire.

Joseph’s people will be like a flame.

The nation of Edom will be like straw.

Jacob’s people will set Edom on fire and burn it up.

No one will be left alive

among Esau’s people.”

The Lord has spoken.

19Israelites from the Negev Desert

will take over Esau’s mountains.

Israelites from the western hills

will possess the land of the Philistines.

They’ll take over the territories

of Ephraim and Samaria.

Israelites from the tribe of Benjamin

will possess the land of Gilead.

20Some Israelites were forced to leave their homes.

They’ll come back to Canaan and possess

it all the way to the town of Zarephath.

Some people from Jerusalem were taken

to the city of Sepharad.

They’ll return and possess

the towns of the Negev Desert.

21Leaders from Mount Zion will go

and rule over the mountains of Esau.

And the kingdom will belong to the Lord.