Amosi 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 1:1-15

1Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.

2Amosi anati:

“Yehova akubangula mu Ziyoni

ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;

msipu wa abusa ukulira,

ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”

Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli

3Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anapuntha Giliyadi

ndi zopunthira za mano achitsulo,

4Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.

5Ndidzathyola chipata cha Damasiko;

ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,

ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.

Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”

akutero Yehova.

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu

ndi kuwugulitsa ku Edomu,

7ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

8Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi

komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.

Ndidzalanga Ekroni,

mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”

akutero Ambuye Yehova.

9Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,

osasunga pangano laubale lija,

10Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”

11Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,

popanda nʼchifundo chomwe.

Popeza mkwiyo wake unakulabe

ndipo ukali wake sunatonthozeke,

12Ine ndidzatumiza moto pa Temani

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”

13Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi

nʼcholinga choti akuze malire awo,

14Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,

kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.

15Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,

iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

New International Reader’s Version

Amos 1:1-15

1These are the words of Amos. He was a shepherd from the town of Tekoa. Here is the vision he saw concerning Israel. It came to him two years before the earthquake. At that time Uzziah was king of Judah. Jeroboam, the son of Jehoash, was king of Israel. Here are the words of Amos.

2He said,

“The Lord roars like a lion from Jerusalem.

His voice sounds like thunder from Zion.

The grasslands of the shepherds turn brown.

The top of Mount Carmel dries up.”

The Lord Judges Israel’s Neighbors

3The Lord says,

“The people of Damascus have sinned again and again.

So I will judge them.

They used threshing sleds with iron teeth

to crush Gilead’s people.

4So I will send fire to destroy the palace of King Hazael.

It will burn up the forts of his son Ben-Hadad.

5I will break down the city gate of Damascus.

I will kill the king

who lives in the Valley of Aven, that evil place.

He holds the ruler’s scepter in Beth Eden.

The people of Aram will be taken away to Kir as prisoners,”

says the Lord.

6The Lord says,

“The people of Gaza have sinned again and again.

So I will judge them.

They captured whole communities.

They sold them to Edom.

7So I will send fire to destroy the walls of Gaza.

It will burn up its forts.

8I will kill the king of Ashdod.

He holds the ruler’s scepter in Ashkelon.

I will use my power against Ekron.

Every single Philistine will die,”

says the Lord and King.

9The Lord says,

“The people of Tyre have sinned again and again.

So I will judge them.

They captured whole communities.

They sold them to Edom.

They did not honor the treaty

of friendship they had made.

10So I will send fire to destroy the walls of Tyre.

It will burn up its forts.”

11The Lord says,

“The people of Edom have sinned again and again.

So I will judge them.

They chased Israel with swords

that were ready to strike them down.

They killed the women of the land.

They were angry all the time.

Their anger was like a fire that blazed out.

It could not be stopped.

12So I will send fire to destroy the city of Teman.

It will burn up Bozrah’s forts.”

13The Lord says,

“The people of Ammon have sinned again and again.

So I will judge them.

They ripped open the pregnant women in Gilead.

They wanted to add land to their territory.

14So I will set fire to destroy the walls of Rabbah.

It will burn up its forts.

War cries will be heard on that day of battle.

Strong winds will blow on that stormy day.

15Ammon’s king will be carried away.

So will his officials,”

says the Lord.