Yoweli 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

New International Reader’s Version

Joel 3:1-21

The Lord Judges the Nations

1“At that time I will bless Judah and Jerusalem

with great success again.

2I will gather together all the nations.

I will bring them down to the Valley of Jehoshaphat.

There I will put them on trial.

I will judge them for what they have done

to my people Israel.

They scattered them among the nations.

They divided up my land among themselves.

3They cast lots for my people.

They sold boys into slavery to get prostitutes.

They sold girls to buy some wine to drink.

4“Tyre and Sidon, why are you doing things like that to me? And why are you doing them, all you people in Philistia? Are you trying to get even with me for something I have done? If you are, I will pay you back for it in a quick and speedy way. 5You took my silver and gold. You carried off my finest treasures to your temples. 6You sold the people of Judah and Jerusalem to the Greeks. You wanted to send them far away from their own country.

7“But now I will stir them up into action. I will bring them back from the places you sold them to. And I will do to you what you did to them. 8I will sell your sons and daughters to the people of Judah. And they will sell them to the Sabeans. The Sabeans are a nation that is far away.” The Lord has spoken.

9Announce this among the nations.

Tell them to prepare for battle.

Nations, get your soldiers ready!

Bring all your fighting men together

and march out to attack.

10Hammer your plows into swords.

Hammer your pruning tools into spears.

Let anyone who is weak say,

“I am strong!”

11Come quickly, all you surrounding nations.

Gather together in the Valley of Jehoshaphat.

Lord, send down your soldiers from heaven!

12The Lord says,

“Stir up the nations into action!

Let them march into the valley

where I will judge them.

I will take my seat in court.

I will judge all the surrounding nations.

13My soldiers, swing your blades.

The nations are ripe for harvest.

Come and stomp on them as if they were grapes.

Crush them until the winepress of my anger is full.

Do it until the wine spills over

from the places where it is stored.

The nations have committed far too many sins!”

14Huge numbers of soldiers are gathered in the valley

where the Lord will hand down his sentence.

The day of the Lord is near in that valley.

15The sun and moon will become dark.

The stars won’t shine anymore.

16The Lord will roar like a lion from Jerusalem.

His voice will sound like thunder from Zion.

The earth and the heavens will tremble.

But the Lord will keep the people of Israel safe.

He will be a place of safety for them.

The Lord Blesses His People

17The Lord says,

“You will know that I am the Lord your God.

I live in Zion.

It is my holy mountain.

Jerusalem will be my holy city.

People from other lands

will never again attack it.

18“At that time fresh wine will drip from the mountains.

Milk will flow down from the hills.

Water will run through all Judah’s valleys.

A fountain will flow out of my temple.

It will water the places where acacia trees grow.

19But Egypt will be deserted.

Edom will become a dry and empty desert.

They did terrible harm to the people of Judah.

My people were not guilty of doing anything wrong.

But Egypt and Edom spilled their blood anyway.

20My people will live in Judah and Jerusalem forever.

The land will be their home for all time to come.

21Egypt and Edom have spilled my people’s blood.

Should I let them escape my judgment?

No, I will not.”

The Lord lives in Zion!