Yona 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 1:1-17

Yona Athawa Yehova

1Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti, 2“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”

3Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.

4Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.

5Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato. 6Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”

7Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.

8Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”

9Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”

10Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).

11Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”

12Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”

13Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja 14Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.” 15Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata. 16Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.

17Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

New International Reader’s Version

Jonah 1:1-17

Jonah Runs Away From the Lord

1A message from the Lord came to Jonah, the son of Amittai. The Lord said, 2“Go to the great city of Nineveh. Preach against it. The sins of its people have come to my attention.”

3But Jonah ran away from the Lord. He headed for Tarshish. So he went down to the port of Joppa. There he found a ship that was going to Tarshish. He paid the fare and went on board. Then he sailed for Tarshish. He was running away from the Lord.

4But the Lord sent a strong wind over the Mediterranean Sea. A wild storm came up. It was so wild that the ship was in danger of breaking apart. 5All the sailors were afraid. Each one cried out to his own god for help. They threw the ship’s contents into the sea. They were trying to make the ship lighter.

But Jonah had gone below deck. There he lay down and fell into a deep sleep. 6The captain went down to him and said, “How can you sleep? Get up and call out to your god for help! Maybe he’ll pay attention to what’s happening to us. Then we won’t die.”

7Here is what the sailors said to one another. “Someone is to blame for getting us into all this trouble. Come. Let’s cast lots to find out who it is.” So they did. And Jonah was picked. 8They asked him, “What terrible thing have you done to bring all this trouble on us? Tell us. What do you do for a living? Where do you come from? What is your country? What people do you belong to?”

9He answered, “I’m a Hebrew. I worship the Lord. He is the God of heaven. He made the sea and the dry land.”

10They found out he was running away from the Lord. That’s because he had told them. Then they became terrified. So they asked him, “How could you do a thing like that?”

11The sea was getting rougher and rougher. So they asked him, “What should we do to you to make the sea calm down?”

12“Pick me up and throw me into the sea,” he replied. “Then it will become calm. I know it’s my fault that this terrible storm has come on you.”

13But the men didn’t do what he said. Instead, they did their best to row back to land. But they couldn’t. The sea got even rougher than before. 14Then they cried out to the Lord. They prayed, “Please, Lord, don’t let us die for taking this man’s life. After all, he might not be guilty of doing anything wrong. So don’t hold us responsible for killing him. Lord, you always do what you want to.” 15Then they took Jonah and threw him overboard. And the stormy sea became calm. 16The men saw what had happened. Then they began to have great respect for the Lord. They offered a sacrifice to him. And they made promises to him.

Jonah Prays to the Lord

17Now the Lord sent a huge fish to swallow Jonah. And Jonah was in the belly of the fish for three days and three nights.