Nyimbo ya Solomoni 8 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom Mu Dwom 8:1-14

1Sɛ anka woyɛɛ me nuabarima

a wonum me maame nufu ano,

ɛna mehunuu wo wɔ abɔntene so a,

anka mɛfe wʼano,

a obiara ntumi mmu me animtiaa.

2Anka mɛdi wʼanim

na mede wo aba me maame efie,

ɔno a woakyerɛkyerɛ me.

Anka mɛma wo bobesa a wɔde pɛprɛ afra mu,

me ateaa mu nsuo dɔkɔ dɔkɔ no bi.

3Ne nsa benkum da mʼatikɔ

na ne nsa nifa aka me afam ne bo.

4Yerusalem mmammaa, mehyɛ mo sɛ,

morennyane na morenhwanyane ɔdɔ mu

kɔsi ɛberɛ a ɛsɛ mu.

Nnamfonom:

5Hwan na ɔfiri ɛserɛ so reba a

ɔtwere ne dɔfoɔ kokom yi?

Ababaawa:

Mekanyanee wo wɔ aprɛ dua no ase;

ɛhɔ na wo maame nyinsɛnee woɔ,

ɛhɔ na deɛ ɔkoo awoɔ no woo woɔ.

6Fa me to wʼakoma so sɛ nsɔanodeɛ,

sɛ nsɔanodeɛ wɔ wʼabasa so,

ɛfiri sɛ ɔdɔ ano yɛ den sɛ owuo,

ne ninkunutweɛ tim hɔ sɛ damena.

Ɛhyehye sɛ ogyadɛreɛ,

sɛ ogyaframa a ano yɛ den pa ara.

7Nsuo dodoɔ rentumi nnum ɔdɔ;

nsubɔntene rentumi nhohoro nkɔ.

Sɛ obi de ne fie ahonya nyinaa bɛsesa ɔdɔ a

anka wɔremmu no adeɛ a ɛsom bo.

Nnamfonom:

8Yɛwɔ nuabaa akumaa bi a,

ne nufu mmobɔeɛ.

Ɛdeɛn na yɛbɛyɛ ama yɛn nuabaa yi

wɔ da a wɔbɛbisa no ase?

9Sɛ ɔyɛ ɔfasuo a,

yɛbɛsi dwetɛ abantenten abɔ ne ho ban.

Sɛ ɔyɛ ɛpono a,

yɛde ntweneduro bɛsi ne ɛpono no kwan.

Ababaawa:

10Meyɛ ɔfasuo,

na me nufu te sɛ abantenten.

Enti nʼani so no mayɛ sɛ obi a

ɔde deɛ ɛsɔ ani reba.

11Na Salomo wɔ bobeturo wɔ Baal-Hamon;

ɔde ne bobeturo no maa apaafoɔ.

Na ɛsɛ sɛ wɔn mu biara tua no

nnwetɛbena apem.

12Nanso me bobeturo yi yɛ me dea.

Me deɛ, meremfa mma;

Salomo de ne deɛ gye nnwetɛbena apem,

na ɔtua nʼapaafoɔ nnwetɛbena ahaanu ma wɔhwɛ ne nnuaba no so.

Aberanteɛ:

13Wo a wote turo no mu

ne nnamfonom a wɔka wo ho,

ma mente wo nne.

Ababaawa:

14Bra ma yɛnkɔ, me dɔfoɔ,

na yɛ wo ho sɛ ɔdabɔ ba

anaasɛ ɔforoteɛ ba a

ɔwɔ mmepɔ a nnuhwam ahyɛ so ma so.