Nyimbo ya Solomoni 7 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 7:1-13

1Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola

mu nsapato wavalazo!

Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,

ntchito ya manja ya mmisiri waluso.

2Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino

chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.

Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu

utazunguliridwa ndi maluwa okongola.

3Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,

ngati mphoyo zamapasa.

4Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.

Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,

amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.

Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,

yoyangʼana ku Damasiko.

5Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.

Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;

mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.

6Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,

iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!

7Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,

ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.

8Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;

ndidzathyola zipatso zake.”

Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,

fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,

9ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,

ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.

10Wokondedwayo ine ndine wake,

ndipo chilakolako chake chili pa ine.

11Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,

tikagone ku midzi.

12Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,

tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,

ngati maluwa ake ayamba kuoneka,

komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.

Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.

13Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,

ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,

zatsopano ndi zakale zomwe,

zimene ndakusungira wokondedwa wanga.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom Mu Dwom 7:1-13

1Wo nan ne mpaboa yɛ fɛ,

Ao, ɔdehyeɛ babaa!

Wʼanantuo a wogyina so te sɛ abohemaa,

odwumfoɔ nsa ano adwuma.

2Wo funuma yɛ kuruwa a ɛnni nsa

a nsã pa wɔ mu ɛberɛ biara.

Wo sisi yɛ atokoɔ a wɔaboa ano

na sukooko atwa ho ahyia.

3Wo nufu te sɛ aforoteɛ mma mmienu,

adabɔ mma ntafoɔ.

4Wo kɔn te sɛ asonse abantenten.

Wʼaniwa aba te sɛ Hesbon ntadeɛ

a ɛwɔ Bat Rabim ɛpono nkyɛn.

Wo hwene te sɛ Lebanon abantenten

a ɛkyerɛ Damasko no.

5Wo tiri si so sɛ Karmel Bepɔ.

Wo tirinwi te sɛ adehyetoma a wɔadi mu adwinneɛ;

wo tirinwi tentene no dwomfa ɔhene.

6Wo ho yɛ fɛ, Ao ɔdɔ,

wo ho anikadeɛ ma wo ho yɛ ahomeka.

7Wo siberɛ te sɛ abɛ dua,

na wo nufu te sɛ aduaba siaka.

8Mekaa sɛ, “Mɛforo abɛ dua no;

na masɔ nʼaba mu.”

Wo nufu nyɛ sɛ bobe siaka,

na wo homeɛ mu hwa nyɛ sɛ aprɛ.

9Na wʼanomu hwa nyɛ sɛ bobesa papa.

Ababaawa:

Ma bobesa no nkɔ me dɔfoɔ hɔ tee,

ɛntene mfa nʼanofafa ne ne se no so brɛoo.

10Meyɛ me dɔfoɔ dea,

na nʼapɛdeɛ ne me.

11Bra, me dɔfoɔ; ma yɛnkɔ nkuraase,

ma yɛnkɔda nkuraase anadwo baako.

12Ma yɛnkɔ bobefuo mu ntɛm

nkɔhwɛ sɛ bobe no agu nhyerɛnne,

sɛ nhyerɛnne no apaapae,

anaasɛ ateaa no ayɛ frɔmm.

Ɛhɔ na mede me dɔ bɛma wo.

13Adasoa yi ne hwa,

na akɔnnɔduane nyinaa bɛgu yɛn ɛpono ano,

foforɔ ne dada,

a mede asie ama woɔ, me dɔfoɔ.