Nyimbo ya Solomoni 6 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 6:1-13

Abwenzi

1Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?

Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti

kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

2Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,

ku timinda ta zokometsera zakudya,

akukadyetsa ziweto zake ku minda,

ndiponso akuthyola maluwa okongola.

3Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;

amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

Mwamuna

4Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,

wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,

ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.

5Usandipenyetsetse;

pakuti maso ako amanditenga mtima.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

6Mano ako ali ngati gulu la nkhosa

zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,

iliyonse ili ndi ana amapasa,

palibe imene ili yokha.

7Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,

masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.

8Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,

ndi azikazi 80,

ndi anamwali osawerengeka;

9koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;

mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,

mwana wapamtima wa amene anamubereka.

Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;

akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.

Abwenzi

10Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,

wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,

wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?

Mwamuna

11Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi

kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,

kukaona ngati mpesa waphukira

kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.

12Ndisanazindikire kanthu,

ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.

Abwenzi

13Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;

bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!

Mwamuna

Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,

pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

雅歌 6:1-13

耶路撒冷的少女:

1絕色的佳人啊,

你的良人去了何處?

你的良人轉往何方?

我們好幫你尋找他。

女子:

2我的良人下到自己的園中,

在香草花圃中牧放他的羊群,

採集百合花。

3我屬於我的良人,

我的良人也屬於我。

他在百合花間牧放羊群。

男子:

4我的愛人啊,

你像得撒一樣秀麗,

耶路撒冷一樣佳美,

像旌旗飄揚的軍隊一樣威嚴。

5求你把視線移開吧,

因為你的眼波使我迷亂。

你的秀髮像從基列山坡下來的山羊群。

6你的牙齒白得像一群洗乾淨的母羊,

成雙成對,

一顆也沒有脫落。

7你面紗下的雙頰如兩瓣石榴。

8雖有六十個王后,

八十個妃嬪和無數的宮女,

9但我完美無瑕的小鴿子獨一無二,

她是她母親的獨女和最愛。

眾女子看見她都誇她有福,

王后和妃嬪見了也連連稱讚她,說:

10「這位燦爛似晨光,

皎潔如明月,耀眼如太陽,

亮麗如佈滿天際之星辰6·10 佈滿天際之星辰」希伯來文是「威嚴如旌旗飄揚的軍隊」,希伯來人常把星星比作天上的軍隊。的是誰呢?」

11我下到核桃園中,

要看看谷中嫩綠的植物,

看看葡萄樹是否已發芽,

石榴樹是否正在開花。

12不知不覺,

我的心把我帶到我尊長的車上。

耶路撒冷的少女:

13回來吧,回來吧,

書拉密的少女!

回來吧,回來吧,

好讓我們再看看你!

男子:

你們為何目不轉睛地看著書拉密的少女,

好像觀看瑪哈念的舞蹈呢?