Mlaliki 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 4:1-16

Matsoka ndi Mavuto a Moyo Uno

1Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:

ndinaona misozi ya anthu opsinjika,

ndipo iwo alibe owatonthoza;

mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo

ndipo iwonso analibe owatonthoza.

2Ndipo ndinanena kuti akufa,

amene anafa kale,

ndi osangalala kuposa amoyo,

amene akanalibe ndi moyo.

3Koma wopambana onsewa

ndi amene sanabadwe,

amene sanaone zoyipa

zimene chimachitika pansi pano.

4Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

5Chitsiru chimangoti manja ake lobodo

ndi kudzipha chokha ndi njala.

6Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,

kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto,

ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.

7Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:

8Panali munthu amene anali yekhayekha;

analibe mwana kapena mʼbale.

Ntchito yake yolemetsa sinkatha,

ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.

Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?

Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?”

Izinso ndi zopandapake,

zosasangalatsa!

9Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,

chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:

10Ngati winayo agwa,

mnzakeyo adzamudzutsa.

Koma tsoka kwa munthu amene agwa

ndipo alibe wina woti amudzutse!

11Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.

Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?

12Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,

koma anthu awiri akhoza kudziteteza.

Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.

Kutukuka Nʼkopandapake

13Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo. 14Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo. 15Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu. 16Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

傳道書 4:1-16

1於是,我又觀察日光之下的一切欺壓之事。我看見受欺壓的淚流滿面,無人安慰。因為欺壓者有權有勢,所以無人安慰他們。 2我為那已死的人慶幸,因為他們比活著的人幸福。 3不過,比以上兩種人更幸運的是那從未出生的人,他們從未見過日光之下各樣的惡行。 4我又看見人的一切勞碌和成就原是出於爭強好勝。這也是虛空,如同捕風。 5愚人遊手好閒,最後只能餓死。 6擁有不多,心裡安寧,勝過擁有很多,仍勞碌捕風。 7我又看見日光之下一件虛空的事: 8有一個人孤孤單單,沒有兒子也沒有兄弟,卻終身勞碌。他雖然家道豐裕,仍不滿足,從未想過「我不停地勞碌,放棄一切享受,究竟是為了誰?」這也是虛空,是一種悲哀。 9兩個人總比一個人好,因為二人勞碌同得美好的成果。 10一人跌倒,總有同伴相扶。但孤身一人、跌倒了無人相扶的真悲慘! 11還有,二人同睡會暖和,一人獨睡怎能暖和呢? 12遭遇攻擊,一人獨自不能抵擋,二人並肩就能對付。三股擰成的繩子不容易斷。 13貧窮但有智慧的青年,勝過年老、愚昧、不再納諫的君王。 14雖然這青年在本國出身貧寒,卻能從囚犯成為君王。 15我看見所有日光之下的人都起來擁護這位代替老君王的青年。 16擁護他的人不計其數,以後的世代卻對他不滿。這也是虛空,如同捕風。