Mlaliki 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 3:1-22

Chilichonse Chili ndi Nthawi

1Chinthu chilichonse chili ndi nthawi yake,

ndi nyengo yake yomwe anayika Mulungu:

2Nthawi yobadwa ndi nthawi yomwalira,

nthawi yodzala ndi nthawi yokolola.

3Nthawi yakupha ndi nthawi yochiritsa,

nthawi yogwetsa ndi nthawi yomanga.

4Nthawi yomva chisoni ndi nthawi yosangalala,

nthawi yolira maliro ndi nthawi yovina.

5Nthawi yotaya miyala ndi nthawi yokundika miyala,

nthawi yokumbatirana ndi nthawi yoleka kukumbatirana.

6Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna,

nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.

7Nthawi yongʼamba ndi nthawi yosoka,

nthawi yokhala chete ndi nthawi yoyankhula.

8Nthawi yokondana ndi nthawi yodana,

nthawi ya nkhondo ndi nthawi ya mtendere.

9Kodi wantchito amapeza phindu lanji pa ntchito yake yolemetsa? 10Ine ndinaona chipsinjo chimene Mulungu anayika pa anthu. 11Iye anapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthawi yake. Anayika nzeru zamuyaya mʼmitima ya anthu; komabe anthuwo sangathe kuzindikira zomwe Mulungu wachita kuyambira pa chiyambi mpaka chimaliziro. 12Ine ndikudziwa kuti palibenso kanthu kabwino kwa anthu kopambana kusangalala ndi kuchita zabwino pamene ali ndi moyo. 13Ndi mphatso ya Mulungu kwa munthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ndi ntchito zake zolemetsa. 14Ndikudziwa kuti chilichonse chimene Mulungu amachita chidzakhala mpaka muyaya; palibe zimene zingawonjezedwe kapena kuchotsedwa. Mulungu amazichita kuti anthu azimuopa.

15Chilichonse chimene chilipo chinalipo kale,

ndipo chimene chidzakhalapo chinalipo poyamba;

Mulungu amabwezanso zakale zimene zinapita kuti zichitikenso.

16Ndipo ndinaona chinthu chinanso pansi pano:

ku malo achiweruzo, kuyipa mtima kuli komweko,

ku malo achilungamo, kuyipa mtima kuli komweko.

17Ndinalingalira mu mtima mwanga kuti;

“Mulungu adzaweruza

olungama pamodzi ndi oyipa omwe,

pakuti anayika nthawi yochitikira chinthu chilichonse,

nthawi ya ntchito iliyonse.”

18Ndinalingaliranso kuti, “Kunena za anthu, Mulungu amawayesa ndi cholinga choti awaonetse kuti iwo ali ngati nyama. 19Zimene zimachitikira munthu, zomwezonso zimachitikira nyama; chinthu chimodzi chomwecho chimachitikira onse: Monga munthu amafa momwemonso nyama imafa. Zonsezi zimapuma mpweya umodzimodzi omwewo; munthu saposa nyama. Zonsezi ndi zopandapake. 20Zonse zimapita kumodzimodzi; zonsezi zimachokera ku fumbi, ndipo zimabwereranso ku fumbi komweko. 21Kodi ndani amene amadziwa ngati mzimu wa munthu umakwera kumwamba, ndipo mzimu wa nyama umatsikira kunsi kwa dziko?”

22Kotero ndinaona kuti palibe chinthu chabwino kwa munthu kuposa kuti munthu azisangalala ndi ntchito yake, pakuti ichi ndiye chake chenicheni. Pakuti ndani amene angamubweretse kuti adzaone zimene zidzamuchitikira iye akadzamwalira?

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

傳道書 3:1-22

萬物有時

1天下萬物都有定期,

凡事都有定時。

2出生有時,死亡有時;

耕種有時,拔出有時;

3殺戮有時,醫治有時;

拆毀有時,建造有時;

4哭泣有時,歡笑有時;

哀傷有時,雀躍有時;

5拋石有時,堆石有時3·5 拋石有時,堆石有時」意義不明,有猶太拉比說是「同房有時,分房有時」。

擁抱有時,避開有時;

6尋找有時,遺失有時;

保存有時,丟棄有時;

7撕裂有時,縫合有時;

沉默有時,發言有時;

8愛慕有時,憎惡有時;

爭戰有時,和好有時。

9那麼,人勞碌做工有什麼益處呢? 10我察覺上帝給世人重擔,使他們忙碌不休。 11祂使萬事各按其時變得美好,又把永恆的意識放在人心裡,人卻不能測透上帝從始至終的作為。 12我認識到,人生在世沒有什麼比歡樂、享受更好。 13人人都該吃喝、享受自己勞苦的成果,這是上帝的恩賜。 14我知道,上帝所做的都會存到永遠,誰也不能增減。祂這樣安排是叫人敬畏祂。 15現在的事並不是新事,未來的事也早已發生過。上帝使過去的事再次出現。

世間的不公

16我又看到日光之下,即使在公道和正義之地也有邪惡。 17我心裡想:「不論義人或惡人,上帝必審判,因為萬事萬務都有受審之時。」 18我又想:「至於世人,上帝試驗他們,是要他們知道自己與獸類無異。 19因為人和獸的際遇並無分別,兩者都難逃一死,活著都靠一口氣。人並不比獸強,一切都是虛空。 20兩者都同歸一處,出於塵土,也歸於塵土。 21誰知道人的氣息3·21 氣息」或譯「靈」,本節同。會向上升,獸的氣息會降到地下呢?」 22因此,我覺得沒有什麼比人享受工作之樂更好,因為這是人當得的。人死後,誰能使他看到世間的事呢?