Mlaliki 11 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 11:1-10

Kuponya Chakudya pa Madzi

1Ponya chakudya chako pa madzi,

udzachipezanso patapita masiku ambiri.

2Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu,

pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.

3Ngati mitambo yadzaza ndi madzi,

imagwetsa mvula pa dziko lapansi.

Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto,

ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.

4Amene amayangʼana mphepo sadzadzala;

amene amayangʼana mitambo sadzakolola.

5Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo,

kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi,

momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu,

Mlengi wa zinthu zonse.

6Dzala mbewu zako mmawa

ndipo madzulo usamangoti manja lobodo,

pakuti sudziwa chimene chidzapindula,

mwina ichi kapena icho,

kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.

Kumbukira Mlengi Wako

7Kuwala nʼkwabwino,

ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.

8Munthu akakhala wa zaka zambiri,

mulekeni akondwerere zaka zonsezo,

koma iye azikumbukira masiku a mdima,

pakuti adzakhala ochuluka.

Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.

9Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono,

ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako.

Tsatira zimene mtima wako ukufuna,

ndiponso zimene maso ako akuona,

koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo

Mulungu adzakuweruza.

10Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako,

upewe zokupweteka mʼthupi mwako,

pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.

King James Version

Ecclesiastes 11:1-10

1Cast thy bread upon the waters: for thou shalt find it after many days.11.1 upon…: Heb. upon the face of the waters 2Give a portion to seven, and also to eight; for thou knowest not what evil shall be upon the earth. 3If the clouds be full of rain, they empty themselves upon the earth: and if the tree fall toward the south, or toward the north, in the place where the tree falleth, there it shall be. 4He that observeth the wind shall not sow; and he that regardeth the clouds shall not reap. 5As thou knowest not what is the way of the spirit, nor how the bones do grow in the womb of her that is with child: even so thou knowest not the works of God who maketh all. 6In the morning sow thy seed, and in the evening withhold not thine hand: for thou knowest not whether shall prosper, either this or that, or whether they both shall be alike good.11.6 shall prosper: Heb. shall be right

7¶ Truly the light is sweet, and a pleasant thing it is for the eyes to behold the sun: 8But if a man live many years, and rejoice in them all; yet let him remember the days of darkness; for they shall be many. All that cometh is vanity.

9¶ Rejoice, O young man, in thy youth; and let thy heart cheer thee in the days of thy youth, and walk in the ways of thine heart, and in the sight of thine eyes: but know thou, that for all these things God will bring thee into judgment. 10Therefore remove sorrow from thy heart, and put away evil from thy flesh: for childhood and youth are vanity.11.10 sorrow: or, anger