Miyambo 28 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 28:1-28

1Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,

koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.

2Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,

koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.

3Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake

ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.

4Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,

koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.

5Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,

koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.

6Munthu wosauka wa makhalidwe abwino

aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.

7Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,

koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.

8Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka

amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.

9Wokana kumvera malamulo

ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.

10Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa

adzagwera mu msampha wake womwe,

koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.

11Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,

koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.

12Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;

koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.

13Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,

koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.

14Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,

koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.

15Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa

ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.

16Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza

koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.

17Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu

adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;

wina aliyense asamuthandize.

18Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa

koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.

19Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.

20Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,

koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.

21Kukondera si kwabwino,

ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera

koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.

23Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake

mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.

24Amene amabera abambo ake kapena amayi ake

namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”

ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.

25Munthu wadyera amayambitsa mikangano,

koma amene amadalira Yehova adzalemera.

26Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,

koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.

27Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,

koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,

koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

New Serbian Translation

Приче Соломонове 28:1-28

1Неправедник бежи, а нико га не гони,

а праведник је као лавић храбар.

2Земља због преступа има многе главаре,

али траје дуго са човеком поученим и разумним.

3Сиромах који убогога тлачи

је као пљусак који носи, а рода не доноси.

4Злог хвале они који Закон28,4 Осим значења Закон јеврејски израз тора се односи и на поуку, упутство у смислу ширем од Мојсијевог Закона. заборављају,

а на њих су кивни они који Закон чувају.

5Злотвори не схватају правду,

а све разуме онај што Господа тражи.

6Бољи је и сиромах који часно живи

од богаташа што нечасно живи.

7Разуман је син који Закон држи,

а свог оца срамоти онај што се дружи с изелицама.

8Ко иметак себи згрће од камате и зеленаштва,

сакупља ономе који је милостив убогима.

9Ухо своје ко одврати и не слуша Закон,

његова је молитва одвратна.

10У своју ће јаму пасти

ко заводи праведне на пут зла,

а добро ће беспрекорни да наследе.

11Богати је себи самом мудар,

али га разумни сиромах истражује помно.

12Велика је слава у радости праведника,

а када се зли осиле, човек се сакрива.

13Ко сакрива сагрешења своја, нема му напретка;

помилован бива ко се због њих каје и одриче их се.

14Блажен ли је човек што је стално на опрезу,

а у зло ће пасти онај што је срце своје скаменио.

15Лав што риче, медвед распомамљен,

такав је и злобни владар убогом народу.

16Големи је изнуђивач неразборит владар,

а ко се гнуша изнуђеног добитка продужава своје дане.

17Крвопролићем оптерећен човек хрли јами

и нека му нико не помогне.

18Избављен ће бити онај што беспрекорно живи,

а у трену пашће онај што нечасно живи.

19Изобиље хране има онај који своју земљу ради,

а изобиље сиромаштва онај који тежи безвредним стварима.

20Веран ће човек обилно бити благословен,

а некажњено неће проћи ко срља да се обогати.

21Страхота је кад се гледа ко је ко,

јер ће човек да сагреши и за парче хлеба.

22Шкртица срља да се обогати,

а и не зна да му стиже оскудица.

23Већу благонаклоност напослетку налази онај који кори човека

него онај који ласка језиком.

24Ко поткрада мајку своју и оца својега,

па још каже да ту греха нема,

тај се дружи са џелатом.

25Бахат човек отпочиње свађу,

а напредује ко се узда у Господа.

26Безуман је човек што верује срцу своме,

а ко мудро живи избављен ће бити.

27Нема оскудице ко сиромаху пружа,

а ко са њега скреће поглед препун је проклетства.

28Када се осиле зликовци, свако се склања,

а када страдају, множе се праведници.