Miyambo 27 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 27:1-27

1Usamanyadire za mawa,

pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.

2Munthu wina akutamande, koma osati wekha;

mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.

3Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri,

koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.

4Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa.

Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.

5Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino

kuposa chikondi chobisika.

6Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino,

koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.

7Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi,

koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.

8Munthu amene wasochera ku nyumba kwake,

ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.

9Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima,

ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.

10Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako,

ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto;

mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.

11Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga;

pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.

12Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.

13Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;

ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.

14Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri,

anthu adzamuyesa kuti akutemberera.

15Mkazi wolongolola ali ngati

mvula yamvumbi.

16Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo

kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.

17Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake,

chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.

18Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake,

ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.

19Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi,

chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.

20Manda sakhuta,

nawonso maso a munthu sakhuta.

21Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo,

chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.

22Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo

ndi musi ngati chimanga,

uchitsiru wakewo sudzachoka.

23Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili.

Kodi usamalire bwino ziweto zako?

24Paja chuma sichikhala mpaka muyaya,

ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.

25Pamene udzu watha, msipu nʼkumera;

ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,

26ana ankhosa adzakupatsani chovala

ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.

27Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri

kuti muzidya inuyo ndi banja lanu

ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

New Serbian Translation

Приче Соломонове 27:1-27

1Не хвали се сутрашњим даном,

јер не знаш шта доноси тај дан.

2Други нек те хвали, а не ти себе самог;

незнанац, а не усне твоје.

3Тежак је камен и песак је тежак,

али од обоје је тежи безобразлук безочнога.

4Окрутан је бес, срџба је горопадна

и са љубомором ко да се суочи?

5Јавни укор је бољи

од тајне љубави.

6Поузданије су модрице од онога који те воли

од многих пољубаца онога који те мрзи.

7Сита душа саће меда гази,

а гладној је души слатко и све горко.

8Попут птице протеране из гнезда,

такав је и човек протеран из свог завичаја.

9Уље и мирис драги су срцу

и сладак је пријатељ који од срца саветује.

10Не напуштај пријатеља и пријатеља свог оца;

не одлази у дом свога брата на дан своје невоље;

бољи је сусед који је близу, него брат који је далеко.

11Мудар буди, сине мој, и срце ми развесели,

па да могу подругљивцу речју да узвратим.

12Обазрив човек примети невољу, па се скрије,

а лаковерни иду даље и буду кажњени.

13Узми хаљину ономе што јамчи за туђинца,

и залог му узми кад јамчи за туђинку.

14Ко од раног јутра свога ближњег благосиља на сав глас,

то ће му се рачунати као клетва.

15Жена свадљива је попут сталног прокишњавања

по кишном дану.

16Ко њу обуздава, ветар обуздава

и као да држи уље у десници.

17Гвожђе се о гвожђе оштри,

а човек се оштри о човека.

18Од смоквиног плода јешће ко се за њу брине;

поштован ће бити онај који штити свога господара.

19Као што се лице одсликава у води

тако се и срце човека у човеку види.

20Као што су и Свет мртвих и трулеж мртвих незасити,

тако су незасите и очи човека.

21Топионица је за сребро и пећ је за злато,

а човек се искушава похвалама које прима.

22Истуцаш ли тучком неразумног

са прекрупом у авану,

његова се лудост неће скинути са њега.

23Своје стадо добро пази,

побрини се добро за крда своја;

24јер иметак не траје довека,

а ни круна кроз сва поколења.

25Коси се трава да нова никне,

сакупи се сено по брдима;

26јагњад те облаче,

а јарцима плаћаш за поља.

27Тад имаш обиље козјег млека себи за храну,

за храну укућана, за живот слушкиња својих.