BUKU LOYAMBA
Masalimo 1–41
Salimo 1
1Wodala munthu
amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4Sizitero ndi anthu oyipa!
Iwo ali ngati mungu
umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Књига Прва
Псалми 1–41
Псалам 1
1Блажен човек који не следи савет опаких,
не стоји на грешничком путу,
нити седа у друштво ругача,
2већ ужива у Закону Господњем,
дан и ноћ му о Закону мисли.
3Он је као дрво усађено крај поточних вода,
које род свој даје када му је време,
а лишће му никада не вене.
Све што ради, на добро му иде.
4Нису такви опаки!
Они су као плева што је ветар носи.
5Зато опаки неће опстати на суду,
ни грешници на збору праведних.
6Јер зна Господ пут праведника,
а пут опаких води у пропаст.