Miyambo 24 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 24:1-34

1Usachitire nsanje anthu oyipa,

usalakalake kuti uzikhala nawo,

2pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.

3Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,

ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;

4Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake

ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.

5Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,

ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.

6Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.

Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.

7Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;

chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.

8Amene amakonzekera kuchita zoyipa

adzatchedwa mvundulamadzi.

9Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,

ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.

10Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti

mphamvu yako ndi yochepadi!

11Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;

uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.

12Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”

kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi?

Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi?

Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?

13Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;

uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.

14Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;

ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo,

ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.

15Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.

Usachite nayo nkhondo nyumba yake;

16paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.

Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.

17Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.

Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.

18Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,

angaleke kukwiyira mdaniyo.

19Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa

kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,

20paja munthu woyipa alibe tsogolo.

Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.

21Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,

ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,

22awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.

Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?

Malangizo Enanso a Anthu Anzeru

23Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:

Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:

24Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”

anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.

25Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino

ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.

26Woyankhula mawu owona

ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

27Ugwiriretu ntchito zako zonse,

makamaka za ku munda

ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.

28Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,

kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.

29Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;

ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”

30Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi

ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.

31Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,

mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,

ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.

32Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga

ndipo ndinatolapo phunziro ili:

33Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”

kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”

34umphawi udzafika pa iwe ngati mbala

ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

New Serbian Translation

Приче Соломонове 24:1-34

Двадесета прича

1Не завиди злима,

не пожели да си с њима;

2јер у срцу своме смишљају насиље,

најављују уснама невољу.

Двадесет прва прича

3Мудрошћу се подиже кућа,

а разборитошћу је основана;

4знањем су јој собе напуњене

сваким благом пожељним и вредним.

Двадесет друга прича

5Човек ратник је јак,

али онај који зна јача снагу своју;

6јер ћеш рат добити мудрим саветима

и победа је у многим саветницима.

Двадесет трећа прича

7Висока је мудрост немудроме,

он уста своја не отвара на судским вратима.

Двадесет четврта прича

8Ко је предан да зло смишља

назваће га сплеткарошем.

9Грех су безумни науми

и подругљивац је одуран људима.

Двадесет пета прича

10Клонеш ли у дану невоље,

клонуће и твоја снага.

11Спасавај оне које у смрт вуку,

извлачи оне што тетурају на погубљење.

12Јер, кажеш ли – „Али, ми то нисмо знали!“ –

неће ли схватити онај што прониче срца?

Неће ли знати онај који ти живот чува

и узвратити човеку по делу његовом?

Двадесет шеста прича

13Једи мед, сине мој, јер је здрав

и непцу је твоме сладак мед из саћа.

14Такво је познање мудрости души твојој

ако је пронађеш; тада будућност постоји

и твоја нада неће пропасти.

Двадесет седма прича

15Не вребај ко зликовац у потаји на дом праведника

и коначиште његово не руши.

16Јер падне ли праведник и седам пута, устаће,

а зликовац ће посрнути у невољи.

Двадесет осма прича

17Не радуј се док се руши душманин твој,

кад посрне нека ти се срце не весели;

18да Господ то не види и то буде зло пред њиме,

па са душманина повуче свој гнев.

Двадесет девета прича

19Не жести се због злотвора,

не завиди зликовцима;

20јер будућност не припада злотвору,

догорева светиљка зликовцу.

Тридесета прича

21Бој се Господа, сине мој, баш као и цара;

не дружи се с бунтовнима;

22јер изненадна долази њихова пропаст

и ко да зна који је крај ове двојице?

Остале мудре приче

23И ово се тиче мудрих људи:

Страхота је кад се гледа ко је ко на суду.

24Наиме, ко каже зломе – „Ти си праведан!“ –

људи ће га проклињати,

народи га презирати.

25А онима који га прекоре уживање ће бити,

на њих ће доћи благослов добра.

26Усне воли онај ко узвраћа праведним речима.

27Посао свој на пољу заврши,

припреми њиву своју, а онда изгради кућу своју.

28Не сведочи без разлога против ближњег свога,

зар ћеш да обмањујеш уснама својим?

29Не реци – „Како је он урадио мени, тако ћу и ја да урадим њему.

Узвратићу му по делу његовом!“

30Прошао сам поред поља ленштине

и поред винограда безумника.

31И гле, у трње је све зарасло,

копривама све обрасло,

зид камени беше срушен.

32Када сам то видео, срцем сам схватио,

видео сам и прихватио поуку:

33Још мало снова, још мало дремежа,

још мало доконо да склопиш руке;

34и доћи ће твоје сиромаштво као скитница

и немаштина као насилник.