Miyambo 23 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 23:1-35

1Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira,

uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,

2ngati ndiwe munthu wadyera

udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.

3Usasirire zakudya zake,

pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.

4Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma,

ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.

5Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo.

Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi

ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.

6Usadye chakudya cha munthu waumbombo,

usalakalake zakudya zake zokoma;

7paja iye ndi munthu amene

nthawi zonse amaganizira za mtengo wake

ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,”

koma sakondweretsedwa nawe.

8Udzasanza zimene wadyazo

ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.

9Usayankhule munthu wopusa akumva,

pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.

10Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale

kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,

11paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;

iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.

12Mtima wako uzikhala pa malangizo

ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.

13Usaleke kumulangiza mwana;

ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.

14Ukamukwapula ndi tsatsa

udzapulumutsa moyo wake.

15Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru,

inenso mtima wanga udzakondwera.

16Mtima wanga udzakondwera

pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.

17Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa,

koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.

18Ndithu za mʼtsogolo zilipo

ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.

19Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru,

mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.

20Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera

kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.

21Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi

ndipo aulesi adzavala sanza.

22Mvera abambo ako amene anakubala,

usanyoze amayi ako pamene akalamba.

23Gula choonadi ndipo usachigulitse;

ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.

24Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu;

Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25Abambo ndi amayi ako asangalale;

amene anakubereka akondwere!

26Mwana wanga, undikhulupirire

ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.

27Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama;

ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.

28Amabisala ngati mbala yachifwamba,

ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.

29Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni?

Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo?

Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?

30Ndi amene amakhalitsa pa mowa,

amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.

31Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo,

pamene akuwira mʼchikho

pamene akumweka bwino!

32Potsiriza pake amaluma ngati njoka,

ndipo amajompha ngati mphiri.

33Maso ako adzaona zinthu zachilendo

ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.

34Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja,

kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.

35Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe!

Andimenya koma sindinamve kanthu!

Kodi ndidzuka nthawi yanji?

Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

New Serbian Translation

Приче Соломонове 23:1-35

Седма прича

1Кад са владаром седаш да једеш

пажљиво размотри шта је пред тобом;

2нож ћеш ставити под грло своје

ако си алав.

3Не жуди за његовим ђаконијама,

јер је то варљива храна.

Осма прича

4Не напињи се да стекнеш богатство

и своје се памети прођи.

5Пустиш ли на њега очи своје, гле њега нема,

јер је себи начинило крила попут орла,

што се вине у небеса.

Девета прича

6Не једи храну саможивца,

не пожели ђаконије његове.

7Јер како се он у себи прерачунава,

баш је такав када ти каже –

„Једи и пиј!“ –

а срце му није с тобом.

8Избљуваћеш залогај који си појео,

проћердаћеш све љубазне речи своје.

Десета прича

9Не говори ушима безумног,

јер ће презрети поруку твојих речи.

Једанаеста прича

10Не помичи древни међаш,

не залази у њиве сирочади.

11Јер је јак њихов Откупитељ,

одбраниће њихов случај од тебе.

Дванаеста прича

12Срце своје предај опомени,

своје уши поучним речима.

Тринаеста прича

13Не ускраћуј казну детету,

јер неће да умре ако га и удариш шибом.

14Туци га шибом

и душу му од Света мртвих спаси.

Четрнаеста прича

15О, мој сине, ако ти је срце мудро

и моје се срце радује;

16радује се нутрина моја,

кад ти усне честито говоре.

Петнаеста прича

17Нек ти срце грешницима не завиди,

у богобојазности ти поваздан буди.

18Нема сумње, будућност постоји,

твоја нада неће пропасти.

Шеснаеста прича

19Сине мој, послушај и мудар буди,

своје срце ти на пут усмери.

20Не дружи се са онима што се вином опијају,

са онима који ждеру месо.

21Јер, осиромашиће и пијаница и изелица,

мамурлук ће их обући у дроњке.

Седамнаеста прича

22Слушај оца свога што те је родио,

мајку своју не презири ни када остари.

23Истину купуј и не продаји

мудрост, прекор и поуку.

24Јако се радује отац праведног сина,

ко је родио мудрог сина ужива у њему.

25Нека се радују и отац твој и мајка твоја,

нека се весели она која те је родила.

Осамнаеста прича

26Срце ми своје дај, сине мој,

и нека ти очи почивају на путевима мојим.

27Јер блудница је дубока јама,

туђинка је узано ждрело.

28Она је ко лопов што вреба из потаје

и међу мушкарцима умножава неверне.

Деветнаеста прича

29Ко то кука? Ко то јечи?

Ко се свађа? Ко то приговара?

Ко има ране безразложне

и коме су закрвављене очи?

30Онима што се излежавају крај вина,

онима што иду да пробају вино измешано.

31Не гледај вино док се румени,

док се светлуца у чаши,

док лагано клизи.

32Као змија на крају уједа,

као отровница убада.

33Чудне ће призоре да виде очи твоје

и срце говориће лудорије.

34Бићеш као онај што лежи усред мора,

као онај што лежи наврх јарбола.

35И рећи ћеш: „Ударили су ме, а болестан нисам,

тукли су ме, осетио нисам.

Када ћу се пробудити

да поново потражим пиће?“