Ubwino Wanzeru
1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga
ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru
ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3ngati upempha kuti uzindikire zinthu
inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva
ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;
ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,
ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.
Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.
Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,
kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,
kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;
kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,
kwa anthu amabodza,
13amene amasiya njira zolungama
namayenda mʼnjira zamdima,
14amene amakondwera pochita zoyipa
namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,
ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;
kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake
ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;
njira zake zimamufikitsa ku manda.
19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera
kapena kupezanso njira zamoyo.
20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,
uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko
ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,
ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
پاداش حكمت
1ای پسرم، اگر به سخنانم گوش بدهی و دستوراتم را اطاعت كنی، 2به حكمت گوش فرا دهی و طالب دانايی باشی، 3و اگر به دنبال فهم و بصيرت بگردی 4و آن را مانند نقره بطلبی تا به چنگ آری، 5آنگاه خدا را خواهی شناخت و اهميت خداترسی را خواهی آموخت. 6خداوند بخشندهٔ حكمت است و سخنان دهان او به انسان فهم و دانش میبخشد. 7او به آدمهای خوب و درستكار كمک میكند و از آنها محافظت مینمايد. 8او از اشخاص با انصاف و خداشناس حمايت میكند.
9اگر به سخنانم گوش بدهی، خواهی فهميد كه عدالت، انصاف و صداقت چيست و راه درست كدام است. 10حكمت جزو وجود تو خواهد شد و دانش به تو لذت خواهد بخشيد. 11بصيرت و فهم تو، از تو محافظت خواهد كرد. 12و تو را از افراد بدكار دور نگه خواهد داشت افرادی كه سخنانشان انسان را منحرف میسازد، 13افرادی كه از راه راست برگشتهاند و در ظلمت گناه زندگی میكنند، 14افرادی كه از كارهای نادرست لذت میبرند و از كجروی و شرارت خرسند میشوند، 15و هر کاری كه انجام میدهند از روی حقهبازی و نادرستی است.
16حكمت میتواند تو را از زنان بدكاره و سخنان فريبندهشان نجات دهد. 17اين گونه زنان، شوهران خود را رها نموده، پيمان مقدس زناشويی را شكستهاند. 18-19مردانی كه به خانههای چنين زنانی قدم میگذارند، به سوی مرگ و نيستی پيش میروند و ديگر به زندگی سابق خود باز نمیگردند.
20اما تو راه خداشناسان را پيش بگير و از راه راست منحرف نشو، 21زيرا درستكاران و خداشناسان در زمين زندگی خواهند كرد، 22ولی بدكاران و خدانشناسان از زمين ريشهكن خواهند شد.