Miyambo 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 1:1-33

Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu

1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:

2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;

kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;

3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,

akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.

4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,

achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.

5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,

ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,

6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,

mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.

7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.

Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Malangizo kuti Asunge Nzeru

Malangizo kwa Achinyamata

8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako

ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.

9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako

ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.

10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa

usamawamvere.

11Akadzati, “Tiye kuno;

tikabisale kuti tiphe anthu,

tikabisalire anthu osalakwa;

12tiwameze amoyo ngati manda,

ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.

13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali

ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;

14Bwera, chita nafe maere,

ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”

15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,

usatsagane nawo mʼnjira zawozo.

16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,

amathamangira kukhetsa magazi.

17Nʼkopanda phindu kutchera msampha

mbalame zikuona!

18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;

amangodzitchera okha msampha!

19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;

chumacho chimapha mwiniwake.

Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru

20Nzeru ikufuwula mu msewu,

ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;

21ikufuwula pa mphambano ya misewu,

ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,

22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?

Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?

Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?

23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.

Ine ndikukuwuzani maganizo anga

ndi kukudziwitsani mawu anga.

24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.

Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.

25Uphungu wanga munawunyoza.

Kudzudzula kwanga simunakusamale.

26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;

ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.

27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,

tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,

mavuto ndi masautso akadzakugwerani.

28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;

mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.

29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso

ndipo sanasankhe kuopa Yehova,

30popeza iwo sanasamale malangizo anga

ndipo ananyoza chidzudzulo changa.

31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo

ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.

32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,

ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.

33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;

adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

Persian Contemporary Bible

امثال 1:1-33

ارزش مثلها

1مثلهای سليمان، پادشاه اسرائيل، كه پسر داوود بود:

2اين مثلها به شما كمک خواهند كرد تا حكمت و ادب بياموزيد و بتوانيد معنی سخنان پرمغز را درک كنيد. 3آنها به شما ياد خواهند داد چگونه رفتار عاقلانه داشته باشيد و با صداقت و عدالت و انصاف عمل كنيد. 4اين مثلها به جاهلان حكمت می‌بخشند و به جوانان فهم و بصيرت. 5‏-6با شنيدن و درک اين مثلها، حتی دانايان داناتر می‌شوند و دانشمندان چاره انديشی كسب می‌كنند تا بتوانند معانی گفتار پيچيدهٔ حكيمان را بفهمند.

نصيحت به جوانان

7نخستين قدم برای كسب دانش، خداترسی است. كسی كه حكمت و ادب را خوار می‌شمارد، احمق است. 8ای جوان، نصيحت پدرت را بشنو و از تعليم مادرت رويگردان نشو، 9زيرا سخنان ايشان مانند تاج و جواهر، سيرت تو را زيبا خواهند ساخت.

10وقتی گناهكاران تو را وسوسه می‌كنند، تسليم نشو. 11اگر آنها به تو بگويند: «بيا در كمين مردم بنشينيم و آنها را بكشيم 12و مانند قبر، آنها را ببلعيم و از هستی ساقط كنيم؛ 13از اين راه ما اشیا قيمتی فراوان به چنگ خواهيم آورد و خانه‌های خود را از اين غنايم پر خواهيم ساخت؛ 14هر چه به دست بياوريم به تساوی بين خود تقسيم خواهيم كرد؛ پس بيا و با ما همدست شو!» 15پسرم تو با آنها نرو و خود را از چنين افرادی دور نگه دار؛ 16زيرا آنها هميشه در پی گناه و قتل هستند. 17يک پرنده وقتی می‌بيند برايش دام گذاشته‌اند، از آن دوری می‌كند. 18ولی اين افراد اينطور نيستند. آنها خودشان را به دام می‌اندازند و با دست خود گور خود را می‌كنند. 19اين است سرنوشت تمام كسانی كه در پی سود نامشروع هستند. چنين اشخاص خود را نابود می‌كنند.

ندای حكمت

20حكمت در كوچه‌ها ندا می‌دهد. 21مردم را كه در سر چهارراه‌ها و نزد دروازهٔ شهر جمع شده‌اند صدا كرده، می‌گويد: 22«ای احمق‌ها! تا كی می‌خواهيد احمق بمانيد؟ تا كی می‌خواهيد دانايی را مسخره كنيد و از آن متنفر باشيد؟ 23اگر سرزنش مرا می‌پذيرفتيد من روح خود را بر شما نازل می‌كردم و شما را دانا می‌ساختم. 24بارها شما را صدا كردم ولی توجه نكرديد، التماس نمودم اما اعتنا ننموديد. 25شما نصيحت و نكوهش مرا نپذيرفتيد. 26من نيز در روز مصيبتتان به شما خواهم خنديد، و هنگامی كه بلا دامنگيرتان شود شما را مسخره خواهم كرد. 27وقتی بلا مانند طوفان شما را فرا گيرد و مصيبت مثل گردباد شما را احاطه كند، و سختی و بدبختی شما را از پای درآورد، 28به داد شما نخواهم رسيد، و اگرچه با اشتياق به دنبالم بگرديد، مرا نخواهيد يافت؛ 29زيرا از دانايی متنفر بوده‌ايد و از خداوند اطاعت نكرده‌ايد. 30نصيحت مرا گوش نگرفته‌ايد و نكوهش مرا نپذيرفته‌ايد. 31بنابراين ثمرهٔ راهی را كه در پيش گرفته‌ايد خواهيد ديد. 32زيرا سركشی احمقان، ايشان را خواهد كشت و بی‌خيالی نادانان آنها را از پای در خواهد آورد. 33ولی همهٔ كسانی كه به من گوش دهند، از هيچ بلايی نخواهند ترسيد و در امنيت زندگی خواهند كرد.»