Phindu Lina la Nzeru
1Mwana wanga, usayiwale malangizo anga,
mtima wako usunge malamulo anga.
2Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka
ndipo udzakhala pa mtendere.
3Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere.
Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda
ndi kuwalemba pa mtima pako.
4Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino
pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse
ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,
ndipo Iye adzawongola njira zako.
7Usamadzione ngati wa nzeru.
Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino
ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse;
zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri,
ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova,
ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda,
monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13Wodala munthu amene wapeza nzeru,
munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva,
phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali;
ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali;
mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17Njira zake ndi njira zosangalatsa,
ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa;
wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru.
Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka
ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino.
Zimenezi zisakuchokere.
22Zimenezi zidzakupatsa moyo,
moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu,
ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24pamene ugona pansi, sudzachita mantha;
ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi
kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima
ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino,
pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28Usanene kwa mnansi wako kuti,
“Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa”
pamene uli nazo tsopano.
29Usamukonzere chiwembu mnansi wako,
amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa
pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31Usachite naye nsanje munthu wachiwawa
kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa
koma amayanjana nawo anthu olungama.
33Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa,
koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34Anthu onyoza, Iye amawanyoza,
koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35Anthu anzeru adzalandira ulemu,
koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
نصيحت به جوانان
1-2پسرم، چيزهايی را كه به تو آموختهام هرگز فراموش نكن. اگر میخواهی زندگی خوب و طولانی داشته باشی، به دقت از دستورات من پيروی كن. 3محبت و راستی را هرگز فراموش نكن بلكه آنها را بر گردنت بياويز و بر صفحهٔ دلت بنويس، 4اگر چنين كنی هم خدا از تو راضی خواهد بود هم انسان. 5با تمام دل خود به خداوند اعتماد كن و بر عقل خود تكيه منما. 6در هر كاری كه انجام میدهی خدا را در نظر داشته باش و او در تمام كارهايت تو را موفق خواهد ساخت.
7به حكمت خود تكيه نكن بلكه از خداوند اطاعت نما و از بدی دوری كن، 8و اين مرهمی برای زخمهايت بوده، به تو سلامتی خواهد بخشيد.
9از دارايی خود برای خداوند هديه بياور، نوبر محصولت را به او تقديم نما و به اين وسيله او را احترام كن. 10آنگاه انبارهای تو پر از وفور نعمت خواهد شد و خمرههايت از شراب تازه لبريز خواهد گرديد.
11پسرم، وقتی خداوند تو را تأديب و تنبيه میكند، از او آزرده خاطر نشو، زيرا تنبيه كردن او دليل محبت اوست. 12همانطور كه هر پدری پسر محبوب خود را تنبيه میكند تا او را اصلاح نمايد، خداوند نيز تو را تأديب و تنبيه میكند.
13خوشا به حال كسی كه حكمت و بصيرت پيدا میكند؛ 14او از كسی كه طلا و نقره يافته خوشبختتر است! 15ارزش حكمت از جواهرات بيشتر است و آن را نمیتوان با هيچ گنجی مقايسه كرد. 16حكمت به انسان زندگی خوب و طولانی، ثروت و احترام میبخشد. 17حكمت زندگی تو را از خوشی و سلامتی لبريز میكند. 18خوشا به حال كسی كه حكمت را به چنگ آورد، زيرا حكمت مانند درخت حيات است.
19خداوند به حكمت خود زمين را بنياد نهاد و به عقل خويش آسمان را برقرار نمود. 20به علم خود چشمهها را روی زمين جاری ساخت و از آسمان بر زمين باران بارانيد.
21پسرم، حكمت و بصيرت را نگاه دار و هرگز آنها را از نظر خود دور نكن؛ 22زيرا آنها به تو زندگی و عزت خواهند بخشيد، 23و تو در امنيت خواهی بود و در راهی كه میروی هرگز نخواهی لغزيد؛ 24با خيال راحت و بدون ترس خواهی خوابيد؛ 25از بلايی كه به طور ناگهانی بر بدكاران نازل میشود، نخواهی ترسيد؛ 26و خداوند تو را حفظ كرده، نخواهد گذاشت در دام بلا گرفتار شوی.
27اگر میتوانی به داد كسی كه محتاج است برسی، كمک خود را از او دريغ مدار. 28هرگز به همسايهات مگو: «برو فردا بيا»، اگر همان موقع میتوانی به او كمک كنی. 29عليه همسايهات كه با خيال راحت در جوار تو زندگی میكند توطئه نچين. 30با كسی كه به تو بدی نكرده است بیجهت دعوا نكن. 31به اشخاص ظالم حسادت نكن و از راه و روش آنها پيروی ننما، 32زيرا خداوند از اشخاص كجرو نفرت دارد، اما به درستكاران اعتماد میكند.
33لعنت خداوند بر بدكاران است، اما بركت و رحمت او شامل حال درستكاران میباشد. 34خداوند مسخرهكنندگان را مسخره میكند، اما اشخاص فروتن را ياری میدهد. 35دانايان از عزت و احترام برخوردار خواهند گرديد، ولی نادانان رسوا خواهند شد.