Miyambo 16 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 16:1-33

1Zolinga za mu mtima ndi za munthu,

koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.

2Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,

koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.

3Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,

ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

4Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,

ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.

5Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.

Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.

6Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;

chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.

7Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,

ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.

8Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,

kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.

9Mtima wa munthu umalingalira zochita,

koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

10Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;

ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.

11Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;

miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.

12Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,

pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.

13Mawu owona amakondweretsa mfumu.

Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.

14Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,

koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.

15Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;

ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.

16Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.

Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.

17Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;

wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.

18Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,

ndipo munthu wodzikuza adzagwa.

19Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,

kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.

20Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,

ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

21A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,

ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.

22Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,

koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.

23Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,

ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.

24Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,

amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

25Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu

koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.

26Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;

njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.

27Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa

ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.

28Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,

ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.

29Munthu wandewu amakopa mnansi wake,

ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.

30Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;

amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.

31Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;

munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.

32Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,

munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.

33Maere amaponyedwa pa mfunga,

koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

La Bible du Semeur

Proverbes 16:1-33

1L’homme fait des projets,

mais celui qui a le dernier mot, c’est l’Eternel.

2Vous pouvez penser que tout ce que vous faites est bien,

mais c’est l’Eternel qui apprécie vos motivations.

3Recommande tes œuvres à l’Eternel,

et tes projets se réaliseront.

4L’Eternel a tout fait pour un but,

même le méchant pour le jour du malheur.

5Tout homme orgueilleux est en horreur à l’Eternel ;

soyez-en certain : il ne restera pas impuni.

6La faute est expiée par la bonté et la fidélité

et, par crainte de l’Eternel, on se détourne du mal.

7Quand la conduite d’un homme est agréable à l’Eternel,

il lui concilie même ses ennemis.

8Mieux vaut le peu honnêtement obtenu

que de gros revenus mal acquis.

9L’homme projette de suivre tel chemin,

et Dieu dirige ses pas.

10Quand le roi se prononce, ses paroles ont valeur de déclaration divine :

que sa bouche n’aille donc pas à l’encontre du droit.

11L’Eternel veut des balances et des plateaux justes,

et les poids, il en fait son affaire16.11 Voir 11.1 et note..

12Faire le mal est une chose abominable pour un roi,

car le pouvoir ne devient fort que s’il est juste.

13Ceux dont les paroles sont justes obtiennent la faveur du roi,

et il aime ceux qui parlent avec droiture.

14Quand un roi se met en colère, sa fureur est comme une messagère de mort,

mais l’homme sage saura l’apaiser.

15Quand le visage du roi s’éclaire, c’est un gage de vie,

et sa faveur est comme un nuage annonçant l’ondée printanière16.15 Les pluies de printemps marquent le retour de la végétation, elles sont signes de prospérité et de joie (Dt 11.14)..

16Acquérir la sagesse vaut bien mieux que l’or pur,

et gagner en discernement est bien préférable à l’argent16.16 Voir 2.4..

17Les hommes droits cheminent sur des routes qui évitent le mal,

qui surveille sa conduite préserve sa vie.

18L’orgueil précède la ruine ;

un esprit fier annonce la chute.

19Mieux vaut avoir un esprit humble et frayer avec les gens de condition modeste

que de partager le butin avec les orgueilleux.

20Qui agit prudemment dans une affaire s’en trouvera bien16.20 Autres traductions : qui agit intelligemment dans une affaire s’en trouvera bien, ou : qui a l’intelligence de ce qu’on dit trouvera le bonheur, ou : qui parle avec intelligence obtiendra le bonheur..

Heureux celui qui met sa confiance en l’Eternel !

21Qui a le cœur sage sera reconnu comme intelligent,

et les paroles aimables sont d’autant plus persuasives.

22Le discernement est une source de vie pour celui qui en est pourvu ;

les sots trouvent leur châtiment dans leur sottise même.

23Si le cœur d’un homme est pénétré de sagesse,

il parlera de façon avisée, et ses paroles seront d’autant plus persuasives.

24D’aimables paroles sont comme un rayon de miel :

douces pour l’âme et bienfaisantes pour le corps.

25Bien des hommes pensent être sur le bon chemin,

et pourtant, ils se trouvent sur une voie qui, finalement, mène à la mort.

26La faim du travailleur est une bonne collaboratrice :

sa bouche le pousse à travailler.

27Le vaurien projette le malheur,

et ses paroles sont comme un feu dévorant.

28Le fourbe sème la discorde,

et qui colporte des rumeurs jette la brouille entre des amis.

29L’homme violent circonvient son prochain

et l’entraîne sur une mauvaise voie.

30Qui ferme les yeux pour méditer des desseins pervers

et qui serre les lèvres a déjà commis le mal.

31Les cheveux blancs sont une couronne honorifique :

elle s’obtient par une vie droite.

32Mieux vaut un homme lent à la colère qu’un bon guerrier,

mieux vaut savoir se dominer que de conquérir des villes.

33On jette le sort dans les pans du vêtement du prêtre16.33 Il s’agit de l’ourim et du toummim dont on se servait pour connaître la volonté de Dieu (voir Ex 28.30 et note).,

mais c’est de l’Eternel que dépend toute décision.