Miyambo 15 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 15:1-33

1Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,

koma mawu ozaza amautsa ukali.

2Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru,

koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.

3Maso a Yehova ali ponseponse,

amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.

4Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,

koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.

5Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake,

koma wochenjera amasamala chidzudzulo.

6Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri,

zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.

7Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru;

koma mitima ya zitsiru sitero.

8Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova,

koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.

9Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova

koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.

10Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa.

Odana ndi chidzudzulo adzafa.

11Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova,

nanji mitima ya anthu!

12Wonyoza sakonda kudzudzulidwa;

iye sapita kwa anthu anzeru.

13Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe,

koma mtima wosweka umawawitsa moyo.

14Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru,

koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.

15Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa,

koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.

16Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova,

kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.

17Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi,

kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.

18Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano,

koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.

19Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga,

koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.

20Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.

21Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru,

koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.

22Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka,

koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.

23Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera,

ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.

24Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo

kuti apewe malo okhala anthu akufa.

25Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada

koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.

26Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova,

koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.

27Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake,

koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.

28Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.

29Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa,

koma amamva pemphero la anthu olungama.

30Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima

ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.

31Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo

adzakhala pakati pa anthu anzeru.

32Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha,

koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.

33Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru,

ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

La Bible du Semeur

Proverbes 15:1-33

1Une réponse douce apaise la colère,

mais une parole blessante excite l’irritation.

2Qui enseigne avec sagesse rend le savoir attrayant,

mais la bouche des sots ne répand que des sottises.

3L’Eternel voit ce qui se passe en tout lieu ;

il observe tous les hommes, méchants et bons.

4Des paroles réconfortantes sont comme un arbre de vie,

mais la langue malfaisante démoralise.

5Seul un insensé méprise ce que son père lui a enseigné,

qui tient compte des avertissements est un homme avisé.

6Il y a de nombreux trésors dans la maison du juste,

mais les profits du méchant sont source d’ennuis15.6 Autre traduction : sont troubles..

7Les lèvres des sages répandent le savoir,

mais il n’en est pas ainsi du cœur des insensés.

8L’Eternel a en horreur les sacrifices offerts par les méchants,

mais les prières des hommes droits lui sont agréables.

9L’Eternel a en horreur la conduite du méchant,

mais il aime celui qui recherche ce qui est juste.

10Une dure leçon attend celui qui s’écarte du droit chemin ;

qui déteste être repris périra.

11L’Eternel connaît le séjour des morts, le lieu des disparus,

combien plus le cœur des humains est-il à découvert devant lui !

12Le moqueur n’aime pas qu’on le reprenne,

c’est pourquoi il ne demande pas l’avis des sages.

13Un cœur joyeux rend le visage aimable,

mais quand le cœur est triste, l’esprit est abattu.

14L’homme intelligent cherche toujours à apprendre,

alors que les sots se repaissent de sottises.

15Pour l’affligé, tous les jours sont mauvais,

mais celui qui a le contentement dans son cœur est toujours en fête.

16Mieux vaut avoir peu et craindre Dieu

que de posséder une grande fortune avec du tourment.

17Mieux vaut un plat de légumes là où règne l’amour

qu’un bœuf gras assaisonné de haine.

18L’homme irascible suscite des querelles,

mais celui qui garde son sang-froid apaise les disputes.

19Le chemin du paresseux est une haie de ronces,

mais le sentier des hommes droits est une route bien aplanie.

20Un fils sage fait la joie de son père ;

seul un homme insensé a du mépris pour sa mère.

21La sottise ravit l’homme dépourvu de sens ;

un homme intelligent marche droit.

22Quand on ne consulte personne, les projets échouent,

mais lorsqu’il y a beaucoup de conseillers, ils se réalisent.

23Savoir donner la bonne réponse est une source de joie,

et combien est agréable une parole dite à propos.

24L’homme avisé suit le sentier qui mène en haut vers la vie

et qui le fait échapper au séjour des morts en bas.

25L’Eternel renverse la maison des orgueilleux,

mais il protège la propriété de la veuve.

26Les projets malveillants sont en horreur à l’Eternel,

mais les paroles aimables sont pures.

27Qui veut s’enrichir à tout prix entraîne sa famille dans le malheur,

mais qui déteste les pots-de-vin vivra longtemps.

28Le juste réfléchit bien avant de répondre,

mais la bouche des méchants répand le mal.

29L’Eternel se tient loin des méchants,

mais il entend la prière des justes.

30Un regard lumineux met le cœur en joie ;

une bonne nouvelle fortifie jusqu’aux os.

31Qui prête une oreille attentive aux critiques constructives

habitera parmi les sages.

32Qui refuse d’être repris se méprise lui-même,

mais qui écoute les avertissements acquiert du bon sens.

33La crainte de l’Eternel est une école de la sagesse15.33 Voir 1.7 et note. ;

avant d’être honoré, il faut savoir être humble15.33 Voir 18.12..