Miyambo 15 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 15:1-33

1Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,

koma mawu ozaza amautsa ukali.

2Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru,

koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.

3Maso a Yehova ali ponseponse,

amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.

4Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,

koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.

5Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake,

koma wochenjera amasamala chidzudzulo.

6Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri,

zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.

7Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru;

koma mitima ya zitsiru sitero.

8Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova,

koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.

9Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova

koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.

10Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa.

Odana ndi chidzudzulo adzafa.

11Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova,

nanji mitima ya anthu!

12Wonyoza sakonda kudzudzulidwa;

iye sapita kwa anthu anzeru.

13Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe,

koma mtima wosweka umawawitsa moyo.

14Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru,

koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.

15Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa,

koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.

16Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova,

kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.

17Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi,

kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.

18Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano,

koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.

19Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga,

koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.

20Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.

21Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru,

koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.

22Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka,

koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.

23Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera,

ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.

24Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo

kuti apewe malo okhala anthu akufa.

25Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada

koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.

26Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova,

koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.

27Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake,

koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.

28Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.

29Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa,

koma amamva pemphero la anthu olungama.

30Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima

ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.

31Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo

adzakhala pakati pa anthu anzeru.

32Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha,

koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.

33Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru,

ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

Hoffnung für Alle

Sprüche 15:1-33

Der Weise hat ein Ziel vor Augen

1Eine freundliche Antwort vertreibt den Zorn, aber ein kränkendes Wort lässt ihn aufflammen.

2Wenn kluge Menschen sprechen, wird Wissen begehrenswert; ein Dummkopf gibt nur Geschwätz von sich.

3Dem Herrn entgeht nichts auf dieser Welt; er sieht auf gute und böse Menschen.

4Ein freundliches Wort heilt und belebt15,4 Wörtlich: ist ein Baum des Lebens., aber eine böse Zunge raubt jeden Mut.

5Nur ein unverständiger Mensch verachtet die Erziehung seiner Eltern; wer sich ermahnen lässt, ist klug.

6Wer Gott gehorcht, hat immer mehr als genug; wer von ihm nichts wissen will, dem wird sein Besitz zum Verhängnis.

7Ein verständiger Mensch gibt sein Wissen weiter, aber ein Dummkopf hat nichts Gutes zu sagen.

8Die Opfergaben gottloser Menschen sind dem Herrn zuwider, aber er freut sich über die Gebete der Aufrichtigen.

9Der Herr verabscheut die Lebensweise der Menschen, die ihn missachten; aber er liebt den, der seine Gebote befolgt.

10Wer krumme Wege geht, wird hart bestraft; wer jede Ermahnung verwirft, schaufelt sich sein eigenes Grab.

11Der Herr sieht hinab bis in den Abgrund des Totenreiches – erst recht durchschaut er, was in den Herzen der Menschen vorgeht!

12Ein Lästermaul will nicht ermahnt werden, darum geht er klugen Menschen aus dem Weg.

13Ein fröhlicher Mensch strahlt über das ganze Gesicht, aber einem verbitterten fehlt jede Lebensfreude.

14Vernünftige Menschen wollen ihr Wissen vergrößern, Dummköpfe haben nur am Unsinn ihren Spaß.

15Für den Niedergeschlagenen ist jeder Tag eine Qual, aber für den Glücklichen ist das Leben ein Fest.

16Lieber arm und Gott gehorsam als reich und voller Sorgen.

17Lieber eine einfache Mahlzeit mit guten Freunden als ein Festessen mit Feinden!

18Ein Hitzkopf schürt Zank und Streit, aber ein besonnener Mensch schlichtet ihn.

19Der Weg eines Faulpelzes ist dornenreich, dem Zuverlässigen aber stehen alle Wege offen.

20Ein kluger Sohn macht seinen Eltern Freude, ein Dummkopf zeigt ihnen keinen Respekt.

21Wer unvernünftig ist, hat Spaß an Dummheiten; ein weiser Mensch dagegen geht zielstrebig seinen Weg.

22Ohne Ratgeber sind Pläne zum Scheitern verurteilt; aber wo man gemeinsam überlegt, hat man Erfolg.

23Jeder freut sich, wenn er treffend zu antworten weiß – wie gut ist das richtige Wort zur rechten Zeit!

24Wer klug ist, folgt dem Weg aufwärts zum Leben; er meidet den Weg hinab ins Verderben.

25Der Herr zerstört das Haus der Hochmütigen, aber den Grund und Boden der Witwen verteidigt er.

26Böse Pläne sind dem Herrn verhasst, aber aufrichtige Worte erfreuen ihn.

27Wer sich auf unehrliche Weise Gewinn verschafft, stürzt seine Familie ins Unglück; doch wer keine Bestechungsgelder annimmt, wird mit dem Leben belohnt.

28Ein rechtschaffener Mensch überlegt sich, was er sagt; ein gewissenloser platzt mit giftigen Worten heraus.

29Der Herr ist denen fern, die von ihm nichts wissen wollen; aber er hört auf das Gebet derer, die ihn lieben.

30Ein freundlicher Blick erfreut das Herz, und eine gute Nachricht gibt neue Kraft.

31Wer auf hilfreiche Ermahnung hört, den kann man klug nennen!

32Wenn du jeden Tadel in den Wind schlägst, schadest du dir selbst. Wenn du dir etwas sagen lässt, gewinnst du Einsicht.

33Wer Ehrfurcht vor dem Herrn hat, erlangt Weisheit; bevor man zu Ehren kommt, muss man Bescheidenheit lernen.