Miyambo 14 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 14:1-35

1Mkazi wanzeru amamanga banja lake,

koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.

2Amene amayenda molungama amaopa Yehova,

koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.

3Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana,

koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.

4Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya,

koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.

5Mboni yokhulupirika sinama,

koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.

6Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza,

koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.

7Khala kutali ndi munthu wopusa

chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.

8Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake.

Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.

9Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo,

koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.

10Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake,

ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.

11Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka,

koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.

12Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu,

koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.

13Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa,

ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.

14Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake,

koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.

15Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse,

koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.

16Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa,

koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.

17Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru,

ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.

18Anthu opusa amalandira uchitsiru,

koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.

19Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino,

ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.

20Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda,

koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.

21Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa

koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.

22Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera?

Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.

23Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu,

koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.

24Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe,

koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.

25Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo,

koma mboni yabodza imaphetsa.

26Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira

ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.

27Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo,

kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.

28Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu,

koma popanda anthu kalonga amawonongeka.

29Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri,

koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.

30Mtima wodekha umapatsa thupi moyo,

koma nsanje imawoletsa mafupa.

31Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake,

koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.

32Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe,

koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.

33Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu,

koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.

34Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu,

koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.

35Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru,

koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

Hoffnung für Alle

Sprüche 14:1-35

Der Kluge überlegt, bevor er handelt

1Eine weise Frau sorgt für Haus und Familie, eine leichtfertige aber zerstört alles.

2Wer aufrichtig lebt, nimmt den Herrn ernst; wer krumme Wege geht, missachtet ihn.

3Ein Narr schadet sich selbst mit seiner Besserwisserei, ein verständiger Mensch weiß sich mit seinen Worten zu schützen.

4Ein leerer Stall bleibt zwar sauber – aber ohne Rinder gibt es keinen Ertrag!

5Ein ehrlicher Zeuge sagt immer die Wahrheit aus, ein falscher Zeuge verbreitet Lügen.

6Wer für alles nur Spott übrig hat, wird die Weisheit vergeblich suchen; wer aber vernünftig ist, dem fällt es leicht, sie zu finden.

7Gib dich nicht mit Dummköpfen ab – von ihnen hörst du nichts Vernünftiges!

8Der Kluge weiß, was er tut, und findet den richtigen Weg. Ein Dummkopf läuft mit seinem Betrug in die Irre.

9Leichtfertige Menschen nehmen ihre Sünde nicht ernst; wer dagegen aufrichtig ist, findet Gefallen bei Gott.

10Deine innersten Gefühle kannst du mit niemandem teilen – im tiefsten Leid und in der höchsten Freude ist jeder Mensch ganz allein!

11Das Haus des Gottlosen wird abgerissen, aber die Familie des Aufrichtigen blüht auf.

12Manch einer wähnt sich auf dem richtigen Weg – und läuft geradewegs in den Tod.

13Auch hinter Lachen kann sich Kummer verbergen. Wenn die Freude verrauscht ist, bleibt die Trauer zurück.

14Wer krumme Wege geht, bekommt, was er verdient; und auch der Gute wird für seine Taten belohnt.

15Nur ein gedankenloser Mensch glaubt jedes Wort! Der Vernünftige prüft alles, bevor er handelt.

16Der Kluge ist vorsichtig, um Unrecht zu vermeiden; ein Dummkopf braust schnell auf und fühlt sich auch noch im Recht.

17Wer jähzornig ist, richtet viel Schaden an. Wer hinterlistige Pläne schmiedet, macht sich verhasst.

18Ein unverständiger Mensch kann nur Unwissenheit vorweisen, ein Kluger gewinnt Ansehen durch sein Wissen.

19Der Böse wird sich vor dem Guten beugen, und der Gottlose muss sich erniedrigen vor dem, der Gott gehorcht.

20Mit einem Armen will noch nicht einmal sein Nachbar etwas zu tun haben; der Reiche aber hat viele Freunde.

21Wer seinen Mitmenschen verachtet, der sündigt. Doch glücklich ist, wer den Hilflosen beisteht!

22Wer Böses plant, gerät auf Abwege; wer Gutes im Sinn hat, wird Liebe und Treue erfahren.

23Wer hart arbeitet, bekommt seinen Lohn – wer nur dasteht und redet, wird arm!

24Verständige Menschen werden mit Reichtum belohnt; doch wer keinen Verstand annehmen will, dem bleibt bloß seine Dummheit.

25Ein ehrlicher Zeuge kann Leben retten, aber ein falscher Zeuge ist ein gefährlicher Betrüger.

26Wer den Herrn ehrt, lebt sicher und geborgen; auch seine Kinder finden Zuflucht bei ihm.

27Die Ehrfurcht vor dem Herrn ist eine Quelle des Lebens; sie bewahrt vor tödlichen Fallen.

28Stark und mächtig ist der König, der ein großes Volk regiert, aber wie kläglich steht ein Herrscher ohne Untertanen da!

29Wer seine Gefühle beherrscht, hat Verstand. Der Jähzornige stellt nur seine Unvernunft zur Schau.

30Wer gelassen und ausgeglichen ist, lebt gesund. Doch der Eifersüchtige wird von seinen Gefühlen zerfressen.

31Wer den Armen unterdrückt, verhöhnt dessen Schöpfer. Wer dem Hilflosen beisteht, der ehrt Gott.

32Wer sich von Gott lossagt, kommt durch seine eigene Bosheit um. Wer Gott vertraut, ist selbst im Tod noch geborgen.

33Ein vernünftiger Mensch ist tief in der Weisheit verwurzelt, sogar die Unvernünftigen können das erkennen.

34Gerechtigkeit macht ein Volk groß, doch Sünde ist für jedes Volk eine Schande.

35Ein kluger Diener erntet den Dank des Königs; aber für wen er sich schämen muss, den trifft sein Zorn.