Miyambo 16 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 16:1-33

1Zolinga za mu mtima ndi za munthu,

koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.

2Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,

koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.

3Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,

ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

4Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,

ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.

5Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.

Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.

6Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;

chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.

7Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,

ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.

8Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,

kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.

9Mtima wa munthu umalingalira zochita,

koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

10Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;

ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.

11Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;

miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.

12Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,

pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.

13Mawu owona amakondweretsa mfumu.

Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.

14Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,

koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.

15Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;

ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.

16Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.

Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.

17Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;

wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.

18Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,

ndipo munthu wodzikuza adzagwa.

19Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,

kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.

20Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,

ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

21A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,

ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.

22Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,

koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.

23Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,

ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.

24Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,

amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

25Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu

koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.

26Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;

njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.

27Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa

ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.

28Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,

ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.

29Munthu wandewu amakopa mnansi wake,

ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.

30Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;

amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.

31Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;

munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.

32Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,

munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.

33Maere amaponyedwa pa mfunga,

koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

Hoffnung für Alle

Sprüche 16:1-33

Der Mensch denkt – Gott lenkt

1Der Mensch denkt über vieles nach und macht seine Pläne, das letzte Wort aber hat der Herr16,1 Oder: seine Worte aber kommen vom Herrn..

2Der Mensch hält sein Handeln für richtig, aber der Herr prüft seine Beweggründe.

3Vertraue dem Herrn deine Pläne an, er wird dir Gelingen schenken.

4Der Herr sorgt dafür, dass jeden das Los trifft, das er verdient – auch für den Gottlosen kommt der Tag des Verderbens.

5Der Herr verabscheut die Hochmütigen. Du kannst sicher sein: Keiner entkommt seiner Strafe!

6Wer dem Herrn treu ist und Liebe übt, dem wird die Schuld vergeben; und wer Ehrfurcht vor dem Herrn hat, der meidet das Böse.

7Wenn dein Handeln dem Herrn gefällt, bewegt er sogar deine Feinde dazu, mit dir Frieden zu schließen.

8Besser wenig Besitz, der ehrlich verdient ist, als großer Reichtum, durch Betrug erschlichen.

9Der Mensch plant seinen Weg, aber der Herr lenkt seine Schritte.

10Der König urteilt an Gottes Stelle, darum irrt er sich nicht, wenn er Recht spricht.

11Der Herr will, dass Waage und Gewichte stimmen, denn er selbst hat diese Ordnung aufgestellt.16,11 Wörtlich: Waagebalken und Waagschalen sind Sache des Herrn, sein Werk sind alle Gewichtssteine im Beutel.

12Königen ist das Unrecht verhasst, denn ihre Macht ist nur sicher, wenn Gerechtigkeit herrscht.

13Könige wollen die Wahrheit hören, darum achten sie ehrliche Menschen.

14Der Zorn des Königs ist ein Vorbote des Todes, deshalb versucht ein kluger Mensch, ihn freundlich zu stimmen.

15Die Gunst des Königs bedeutet Leben; seine Anerkennung ist so wohltuend wie ein sanfter Frühlingsregen.

16Weisheit und Urteilsvermögen zu erlangen ist viel kostbarer als Silber oder Gold!

17Ein aufrichtiger Mensch meidet das Böse; wer dies beachtet, wird sein Leben retten.

18Stolz führt zum Sturz, und Hochmut kommt vor dem Fall!

19Lieber bescheiden und arm sein als Beute teilen mit den Hochmütigen!

20Wer auf das hört, was ihm beigebracht wird, der hat Erfolg; und wer dem Herrn vertraut, der findet Glück.

21Man verlässt sich auf das Urteil eines vernünftigen Menschen; und wenn er dazu noch gut reden kann, wird man viel von ihm lernen.

22Wer Einsicht besitzt, für den ist sie eine Quelle des Lebens; aber ein Dummkopf wird durch seine eigene Dummheit bestraft.

23Ein weiser Mensch spricht weise Worte und kann andere damit überzeugen.

24Ein freundliches Wort ist wie Honig: angenehm im Geschmack und gesund für den Körper.

25Manch einer wähnt sich auf dem richtigen Weg – und läuft geradewegs in den Tod.

26Hunger treibt den Menschen an; er muss arbeiten, um satt zu werden.

27Ein gemeiner Mensch brütet immer neues Unheil aus; seine Worte zerstören wie Feuer.

28Ein hinterlistiger Mensch sät Zank und Streit, und ein Lästermaul bringt Freunde auseinander.

29Ein verbrecherischer Mensch beschwatzt seinen Freund und bringt ihn auf krumme Wege.

30Wer listig mit den Augen zwinkert, führt Böses im Schilde; wer entschlossen die Lippen zusammenpresst, hat es schon getan.

31Graues Haar ist ein würdevoller Schmuck – angemessen für alle, die Gottes Gebote befolgen.

32Geduld zu haben ist besser, als ein Held zu sein; und sich selbst beherrschen ist besser, als Städte zu erobern!

33Der Mensch wirft das Los, um Gott zu befragen; und der Herr allein bestimmt die Antwort.