Miyambo 14 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 14:1-35

1Mkazi wanzeru amamanga banja lake,

koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.

2Amene amayenda molungama amaopa Yehova,

koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.

3Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana,

koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.

4Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya,

koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.

5Mboni yokhulupirika sinama,

koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.

6Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza,

koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.

7Khala kutali ndi munthu wopusa

chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.

8Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake.

Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.

9Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo,

koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.

10Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake,

ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.

11Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka,

koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.

12Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu,

koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.

13Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa,

ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.

14Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake,

koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.

15Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse,

koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.

16Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa,

koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.

17Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru,

ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.

18Anthu opusa amalandira uchitsiru,

koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.

19Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino,

ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.

20Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda,

koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.

21Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa

koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.

22Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera?

Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.

23Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu,

koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.

24Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe,

koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.

25Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo,

koma mboni yabodza imaphetsa.

26Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira

ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.

27Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo,

kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.

28Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu,

koma popanda anthu kalonga amawonongeka.

29Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri,

koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.

30Mtima wodekha umapatsa thupi moyo,

koma nsanje imawoletsa mafupa.

31Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake,

koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.

32Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe,

koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.

33Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu,

koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.

34Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu,

koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.

35Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru,

koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

La Bible du Semeur

Proverbes 14:1-35

1Une femme pleine de sagesse construit sa maison,

mais celle qui est insensée la renverse de ses propres mains.

2Qui craint l’Eternel se conduit avec droiture,

qui le méprise emprunte des voies perverses.

3C’est par ses propres paroles que le sot est puni de son orgueil,

mais les paroles des sages sont leur sauvegarde.

4Là où il n’y a pas de bétail, la mangeoire reste nette,

mais la vigueur des bœufs assure d’abondants revenus.

5Un témoin honnête ne ment pas ;

mais le faux témoin profère des mensonges.

6Le moqueur a beau chercher la sagesse : elle lui échappe,

alors que la connaissance est facilement à la portée de l’homme de bon sens.

7Eloigne-toi de l’insensé,

car il n’a aucun savoir à te communiquer.

8La sagesse de l’homme réfléchi lui fait discerner sa voie14.8 Autre traduction : le rend attentif à sa conduite.,

mais la folie des insensés les égare.

9Réparer un tort : les insensés s’en moquent,

mais entre gens droits, la bonne volonté l’emporte14.9 Autres traductions : mais les justes ont de la bonne volonté ou mais les justes cherchent à obtenir la faveur..

10Le cœur connaît son propre chagrin,

et personne ne peut partager sa joie.

11La maison des méchants sera détruite,

mais la demeure des gens droits sera florissante14.11 Voir 3.33..

12Bien des hommes pensent être sur le bon chemin,

et pourtant, ils se trouvent sur une voie qui, finalement, mène à la mort.

13Le rire peut masquer la tristesse du cœur,

et la gaieté peut finir en chagrin.

14L’homme au cœur perfide sera gavé des fruits de sa conduite,

mais l’homme de bien jouira des fruits de la sienne14.14 Autre traduction : mais la situation de l’homme de bien est meilleure que la sienne (ou supérieure à la sienne)..

15L’inexpérimenté croit tout ce qu’on lui dit,

mais l’homme réfléchi avance avec prudence.

16Le sage craint le mal et s’en écarte,

mais l’insensé, sûr de lui, s’emporte.

17L’homme coléreux fait des sottises ;

qui a de mauvais desseins s’attire la haine.

18La folie, voilà ce qu’héritent ceux qui manquent d’expérience,

mais la connaissance est la couronne des gens réfléchis.

19Les méchants auront à baisser la tête devant ceux qui sont bons,

et les hommes mauvais à la porte des justes.

20Personne n’aime le pauvre, même pas son compagnon,

mais le riche a beaucoup d’amis.

21Qui méprise son prochain commet une faute,

mais heureux celui qui a compassion des affligés.

22Ceux qui manigancent le mal font fausse route,

mais ceux qui projettent le bien trouvent l’amour véritable.

23A tout travail il y a du profit,

mais le bavardage mène au dénuement.

24La richesse des sages est leur couronne,

mais la folie des insensés reste de la folie.

25Un témoin véridique sauve des vies14.25 Celles des accusés traduits injustement devant les tribunaux et calomniés par leurs accusateurs.,

mais qui profère des mensonges est un trompeur.

26Celui qui craint l’Eternel possède une solide assurance,

et il sera un refuge pour ses enfants14.26 Pour les v. 26-27, voir 10.27..

27La crainte de l’Eternel est une source de vie,

elle fait éviter les pièges de la mort.

28La gloire d’un roi dépend du nombre de ses sujets,

et la dépopulation ruine le prince.

29Celui qui garde son sang-froid fait preuve d’une grande intelligence,

mais l’homme coléreux étale sa sottise.

30Un cœur paisible contribue à la vie du corps ;

mais l’envie est comme une maladie qui ronge les os.

31Opprimer le pauvre, c’est outrager son Créateur,

mais avoir de la compassion pour les indigents, c’est l’honorer.

32Le méchant est terrassé par sa perversité,

mais le juste reste plein de confiance jusque dans la mort14.32 L’ancienne version grecque et la syriaque ont lu : mais l’intégrité du juste est pour lui source d’assurance, ce qui suppose une simple inversion de deux lettres du texte hébreu traditionnel..

33La sagesse repose dans un esprit intelligent :

elle sera reconnue même parmi les sots14.33 Selon le texte hébreu traditionnel. L’ancienne version grecque et la version syriaque ont : mais le cœur des sots ne la connaît pas..

34La justice grandit une nation,

mais le péché est une honte pour tout peuple.

35Le roi accorde sa faveur à ceux qui le servent avec intelligence,

mais sa colère atteint celui qui fait honte.