Mateyu 27 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 27:1-66

Yudasi Adzimangirira

1Mmamawa, akulu a ansembe onse ndi akuluakulu anavomerezana kuti aphe Yesu. 2Anamumanga, napita naye kukamupereka kwa bwanamkubwa Pilato.

3Yudasi, amene anamupereka Iye, ataona kuti Yesu waweruzidwa kuti akaphedwe, anatsutsika mu mtima mwake nakabweza ndalama zamasiliva makumi atatu zija kwa akulu a ansembe ndi kwa akuluakulu. 4Iye anati, “Ndachimwa pakuti ndapereka munthu wosalakwa.”

Iwo anayankha nati, “Ife tilibe nazo kanthu izo ndi zako.”

5Pamenepo Yudasi anaponya ndalamazo mʼNyumba ya Mulungu nachoka. Kenaka anapita nakadzimangirira.

6Akulu a ansembe anatola ndalamazo nati, “Sikololedwa ndi lamulo kuti ndalamazi tiziyike mosungira chuma cha Mulungu, popeza ndi ndalama za magazi.” 7Choncho anagwirizana kuti ndalamazo azigwiritse ntchito pogulira munda wa wowumba mbiya kuti ukhale manda alendo. 8Ndi chifukwa chake umatchedwa munda wamagazi mpaka lero lino. 9Pamenepo zimene anayankhula mneneri Yeremiya zinakwaniritsidwa kuti, “Anatenga ndalama zamasiliva makumi atatu mtengo umene anamuyikira Iye anthu a Israeli. 10Ndipo anazigwiritsa ntchito kugula munda wa wowumba mbiya monga mmene Ambuye anandilamulira ine.”

Yesu kwa Pilato

11Pa nthawi yomweyo Yesu anayimirira pamaso pa bwanamkubwa ndipo bwanamkubwayo anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndiwe Mfumu ya Ayuda?”

Koma Yesu anayankha kuti, “Mwanena ndinu.”

12Pamene akulu a ansembe ndi akuluakulu ankamuneneza, sanayankhe kanthu. 13Kenaka Pilato anamufunsa Iye kuti, “Kodi sukumva zinthu zimene akukunenerazi?” 14Koma Yesu sanayankhe ngakhale mawu amodzi mpaka bwanamkubwa anadabwa kwambiri.

15Pa nthawiyi chinali chizolowezi cha bwanamkubwa kuti pachikondwerero cha Paska amamasula wamʼndende wosankhidwa ndi anthu. 16Pa nthawiyo anali ndi wamʼndende woyipa kwambiri dzina lake Baraba. 17Gulu la anthu litasonkhana, Pilato anawafunsa kuti, “Ndi ndani amene mufuna kuti ndikumasulireni; Baraba kapena Yesu wotchedwa Khristu?” 18Pakuti anadziwa kuti anamupereka Yesu chifukwa cha kaduka.

19Pamene Pilato anakhala pa mpando woweruza, mkazi wake anamutumizira uthenga uwu, “Musachite kanthu ndi munthuyo, ndi wosalakwa pakuti ndavutika kwambiri lero mʼmaloto chifukwa cha munthuyo.”

20Koma akulu a ansembe ndi akuluakulu ananyengerera gulu la anthu kuti apemphe Baraba ndi kuti Yesu aphedwe.

21Bwanamkubwayo anafunsa kuti, “Ndi ndani mwa awiriwa amene mufuna ine ndikumasulireni?”

Iwo anayankha kuti, “Baraba.”

22Pilato anafunsa kuti, “Nanga ndichite chiyani ndi Yesu wotchedwa Khristu?”

Onse anayankha kuti “Mpachikeni!”

23Pilato anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani? Wachita choyipa chotani?”

Koma anachita phokoso nafuwula kwambiri kuti, “Mpachikeni!”

24Pilato ataona kuti samaphulapo kanthu, koma mʼmalo mwake chiwawa chimayambika, anatenga madzi nasamba mʼmanja mwake pamaso pa gulu la anthu. Iye anati “Ine ndilibe chifukwa ndi magazi a munthu uyu, ndipo uwu ndi udindo wanu!”

25Anthu onse anayankha nati, “Magazi ake akhale pa ife ndi pa ana athu!”

26Pamenepo anawamasulira Baraba koma analamula kuti Yesu akakwapulidwe, ndipo anamupereka kuti akapachikidwe.

Asilikali Amuchita Chipongwe Yesu

27Pamenepo asilikali abwanamkubwayo anamutenga nalowa naye ku bwalo la milandu ndipo anasonkhanitsa gulu lonse la asilikali namuzungulira Iye. 28Anamuvula malaya ake namuveka Iye malaya ofiira aufumu. 29Ndipo kenaka analuka chipewa chaminga nachiyika pa mutu pake. Anamugwiritsa ndodo mʼdzanja lake lamanja nagwada pamaso pake namuchitira chipongwe nati, “Tikulonjereni Mfumu ya Ayuda.” 30Anamuthira malovu ndipo anatenga ndodo namumenya nayo pa mutu mobwerezabwereza. 31Atamaliza kumuchitira chipongwe, anamuvula malaya aja namuveka malaya ake aja napita naye kokamupachika.

Amupachika Yesu

32Pamene gululi linkatuluka ndi Yesu, anakumana ndi munthu wochokera ku Kurene dzina lake Simoni ndipo anamuwumiriza kunyamula mtanda. 33Anafika ku malo wotchedwa Gologota amene atanthauza kuti malo a bade la mutu. 34Pamenepo anamupatsa vinyo wosakaniza ndi ndulu kuti amwe; koma atalawa anakana kumwa. 35Atamupachika Iye, anagawana zovala zake pochita maere. 36Ndipo anakhala pansi namulonda Iye. 37Pamwamba pa mutu wake analembapo mawu osonyeza mlandu wake akuti, “uyu ndi yesu, mfumu ya ayuda.” 38Achifwamba awiri anapachikidwa pamodzi ndi Iye, mmodzi kudzanja lamanja wina kudzanja lamanzere. 39Ndipo amene amadutsa anamunenera mawu a chipongwe, akupukusa mitu yawo. 40Ndipo anati, “Iwe amene ungapasule Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanga masiku atatu, dzipulumutse wekha! Tsika pa mtandapo ngati ndiwe Mwana wa Mulungu!”

41Chimodzimodzinso akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anamuchitira chipongwe. 42Iwo anati, “Anapulumutsa ena koma sangathe kudzipulumutsa yekha! Ndi mfumu ya Israeli! Mulekeni atsike pa mtanda ndipo tidzamukhulupirira Iye. 43Amadalira Mulungu, mulekeni Mulunguyo amupulumutse tsopano ngati akumufuna pakuti anati, ‘Ndine Mwana wa Mulungu.’ ” 44Momwemonso mbala zimene zinapachikidwa naye pamodzi zinamuneneranso zachipongwe.

Kufa kwa Yesu

45Kuyambira 12 koloko masana mpaka 3 koloko, kunachita mdima pa dziko lonse. 46Ndipo nthawi ili ngati 3 koloko, Yesu analira mofuwula nati, “Eloi, Eloi, lama sabakitani!” Kutanthauza kuti, “Mulungu Wanga, Mulungu Wanga, mwandisiyiranji Ine?”

47Ena a oyimirira pamalopo atamva izi anati, “Akuyitana Eliya.”

48Mmodzi wa iwo anathamanga natenga chinkhupule. Anachidzaza ndi vinyo wosasa, nachizika ku mtengo namupatsa Yesu kuti amwe. 49Koma ena onse anati, “Mulekeni tiyeni tione ngati Eliyayo abwere kudzamupulutsa.”

50Ndipo pamene Yesu analiranso mofuwula, anapereka mzimu wake.

51Pa nthawi imeneyo chinsalu chotchinga cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati kuyambira pamwamba mpaka pansi. Dziko linagwedezeka ndipo miyala inangʼambika. 52Manda anatsekuka ndipo mitembo yambiri ya anthu oyera mtima amene anafa inaukitsidwa. 53Anatuluka mʼmanda mwawo, ndipo chitachitika chiukitso cha Yesu, anapita mu mzinda woyera naonekera kwa anthu ambiri.

54Mkulu wa asilikali ndi amene ankalondera Yesu ataona chivomerezi ndi zonse zinachitika, anachita mantha, ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali Mwana wa Mulungu!”

55Amayi ambirimbiri amene ankasamalira Yesu ankaonerera ali patali. Iwo anamutsatira Yesu kuchokera ku Galileya. 56Pakati pawo panali Mariya wa ku Magadala, Mariya amayi ake Yakobo ndi Yosefe ndi amayi a ana a Zebedayo.

Yesu Ayikidwa Mʼmanda

57Pamene kumada, kunabwera munthu wolemera wa ku Arimateyu dzina lake Yosefe amene anali wophunzira wa Yesu. 58Anapita kwa Pilato kukapempha mtembo wa Yesu, ndipo Pilato analamula kuti uperekedwe kwa iye. 59Yosefe anatenga mtembowo, nawukulunga nsalu yabafuta. 60Ndipo anawuyika mʼmanda ake atsopano amene anasema mu thanthwe, natsekapo ndi mwala waukulu pa khomo la mandawo nachokapo. 61Mariya wa Magadala ndi Mariya wina anakhala pansi moyangʼanizana ndi mandawo.

Alonda a pa Manda

62Litapita tsiku lokonzekera Sabata, mmawa mwake, akulu a ansembe ndi Afarisi anapita kwa Pilato. 63Iwo anati, “Bwana takumbukira kuti munthu wonyenga uja akanali ndi moyo anati, ‘Pakatha masiku atatu ndidzauka.’ 64Choncho lamulirani kuti manda ake atetezedwe mpaka pa tsiku lachitatu. Chifukwa tikapanda kutero, ophunzira ake angabwere kudzaba mtembo wake ndipo angawuze anthu kuti waukitsidwa kwa akufa. Ndipo chinyengo chomalizachi chidzakhala choyipa kwambiri kusiyana ndi choyamba chija.”

65Pilato anayankha kuti, “Tengani mlonda kalondereni monga mudziwira.” 66Tsono anapita nakatseka manda kolimba ndi kuyikapo chizindikiro ndipo anayikapo mlonda.

New Russian Translation

Матфея 27:1-66

Совет религиозных вождей осуждает Иисуса

(Мк. 15:1; Лк. 23:1; Ин. 18:28)

1Рано утром все первосвященники и старейшины народа вынесли Иисусу смертный приговор. 2Они, связав Его, отвели и передали римскому наместнику Пилату27:2 Пилат – Понтий Пилат был римским наместником в Иудее с 26 по 36 гг..

Самоубийство Иуды

(Деян. 1:16-20)

3Когда Иуда, предавший Иисуса, увидел, что Иисус осужден, он раскаялся и вернул тридцать серебряных монет первосвященникам и старейшинам.

4– Я согрешил, – сказал он, – я предал на смерть невинного Человека.

– А нам-то что за дело? – ответили те. – Смотри сам.

5Бросив деньги в храме, Иуда ушел и повесился. 6А первосвященники собрали деньги и сказали:

– Положить эти деньги в сокровищницу храма нельзя, так как это плата за кровь.

7И, посоветовавшись, они решили купить на них поле горшечника и использовать его под кладбище для чужеземцев. 8Поэтому то поле и называется до сегодняшнего дня «кровавое поле». 9Так исполнилось сказанное пророком Иеремией: «Они взяли тридцать шекелей серебра – цену, назначенную Ему израильским народом, 10и купили на них землю горшечника, как повелел мне Господь»27:9-10 См. Иер. 19:1-13; 32:6-9; Зах. 11:12-13..

Иисус на суде у Пилата

(Мк. 15:2-5; Лк. 23:2-5; Ин. 18:29-38)

11Тем временем Иисуса поставили перед наместником, и тот спросил Его:

– Ты Царь иудеев?

– Ты сам так говоришь, – отвечал Иисус.

12Когда же Его обвиняли первосвященники и старейшины, Он ничего не отвечал. 13Пилат спросил:

– Ты что, не слышишь, сколько против Тебя обвинений?

14Но Он, к удивлению наместника, не отвечал ни на одно из обвинений.

Пилат осуждает Иисуса на распятие

(Мк. 15:6-15; Лк. 23:13-25; Ин. 18:39–19:16)

15У наместника был обычай на праздник отпускать одного из заключенных, по выбору народа. 16В то время под стражей находился известный узник по имени Иисус Варавва27:16 Варавва – это имя переводится как «сын отца». В некоторых рукописях имя Вараввы Иисус отсутствует. То же в ст. 17.. 17Поэтому, когда собрался народ, Пилат спросил:

– Кого вы хотите, чтобы я вам отпустил: Иисуса Варавву или Иисуса, называемого Христом?

18Он знал, что Иисуса предали ему из зависти. 19К тому же, когда Пилат сидел в судейском кресле, его жена послала сказать ему: «Не делай ничего этому праведнику, я сильно страдала сегодня во сне из-за Него».

20Но первосвященники и старейшины убедили толпу просить освобождения Вараввы и казни Иисуса.

21– Так кого же из этих двоих вы хотите, чтобы я вам отпустил? – спросил наместник.

– Варавву! – сказали они.

22– Что же мне тогда делать с Иисусом, Которого называют Христом? – спросил Пилат.

Все в один голос закричали:

– Пусть Он будет распят!

23– За что? Какое зло сделал Он? – спросил Пилат. Однако толпа кричала все громче:

– Пусть Он будет распят!

24Когда Пилат увидел, что ничего не может сделать и что волнение в народе лишь нарастает, он взял воды, вымыл руки перед всем народом и сказал:

– Смотрите сами. Я же не виновен в крови Этого Человека.

25И весь народ сказал:

– Кровь Его на нас и на наших детях!

26Тогда Пилат освободил им Варавву, а Иисуса велел бичевать и затем отдать на распятие.

Римские солдаты издеваются над Иисусом

(Мк. 15:16-20; Ин. 19:2-3)

27Солдаты отвели Иисуса в резиденцию наместника и собрали вокруг Него весь полк. 28Они раздели Его и надели на Него алую мантию. 29И сплетя венок из терновника, надели Ему на голову, дали Ему в правую руку трость и стали насмехаться над Ним, становясь перед Ним на колени и говоря:

– Да здравствует Царь иудеев!

30И плевали на Него и, взяв трость, били Его по голове. 31Вдоволь наиздевавшись, они сняли с Него мантию, одели Иисуса в Его собственную одежду и вывели на распятие.

Иисуса ведут на распятие

(Мк. 15:21-23; Лк. 23:26-31; Ин. 19:17)

32Когда они выходили, им повстречался человек из Кирены по имени Симон, и солдаты заставили его нести крест. 33Когда они пришли на место, называемое Голгофа (что означает «Лобное место»27:33 Лобное место – букв.: «Череп». Этот холм имел такое название, по всей вероятности, из-за своей формы, напоминавшей человеческий череп.), 34они дали Ему вино, смешанное с желчью. Попробовав, Он не стал пить27:34 См. Пс. 68:22..

Иисус пригвожден к кресту

(Мк. 15:24-32; Лк. 23:32-43; Ин. 19:18-24)

35Распяв Иисуса, солдаты по жребию разделили Его одежду между собой27:35 См. Пс. 21:19. 36и сели стеречь Его. 37Над головой Иисуса прибили табличку с указанием Его вины: «ЭТО ИИСУС, ЦАРЬ ИУДЕЕВ». 38Вместе с Ним были распяты и два разбойника27:38 Или: «мятежника». Также в ст. 44., один по правую, а другой по левую сторону от Него. 39Проходившие мимо бранили Его. Качая головами27:39 См. Пс. 21:8., 40они говорили:

– Ты ведь собирался разрушить храм и в три дня отстроить его! Спаси Себя, если Ты Сын Бога! Сойди с креста!

41Первосвященники, учители Закона и старейшины тоже насмехались над Иисусом.

42– Спасал других, – говорили они, – а Себя спасти не может! Царь Израиля! Пусть Он сойдет с креста, и тогда мы поверим в Него. 43Он полагался на Бога, так пусть Бог теперь избавит Его, если Он Ему угоден27:43 Пс. 21:9.; ведь Он же называл Себя Сыном Бога!

44Теми же словами оскорбляли Его и преступники27:44 Или: «мятежники»., распятые вместе с Ним.

Смерть Иисуса на кресте

(Мк. 15:33-41; Лк. 23:44-49; Ин. 19:28-30)

45От шестого часа по всей земле стало темно, и это продолжалось до девятого часа27:45 То есть до трех часов дня.. 46Около девятого часа Иисус громко крикнул:

– Эли, Эли, лема савахтани?27:46 Эти слова произнесены Иисусом на арамейском языке. – (что значит: «Боже Мой, Боже Мой, почему Ты Меня оставил?»27:46 Пс. 21:2.)

47Некоторые из стоявших поблизости, услышав это, сказали:

– Он зовет Илию27:47 На еврейском языке имя Илия и выражение «Бог мой» звучат очень похоже..

48Один из них тут же подбежал, взял губку, пропитал ее кислым вином, насадил на палку и дал Ему пить. 49Другие же говорили:

– Подожди, давай посмотрим, придет Илия спасти Его или нет.

50Иисус снова громко закричал и испустил дух. 51И тут завеса храма разорвалась надвое сверху донизу27:51 Это была внутренняя завеса храма, которая отделяла «Святое» от «Святого Святых» (см. Исх. 26:31-35). См. Евр. 10:19-22.. Затряслась земля, и раскололись скалы. 52Раскрылись могилы, и многие умершие праведники воскресли. 53Они вышли из могил и, уже после того, как воскрес Сам Иисус, вошли в святой город, где их видело много людей. 54Сотник и те, кто вместе с ним стерегли Иисуса, увидев землетрясение и все, что произошло, очень испугались и сказали:

– Он действительно был Сыном Бога!

55Там также было и много женщин, которые издали наблюдали за происходящим. Они следовали за Иисусом из самой Галилеи, помогая Ему. 56Среди них были Мария Магдалина, Мария, мать Иакова и Иосии, и мать сыновей Зеведея.

Погребение Иисуса

(Мк. 15:42-47; Лк. 23:50-56; Ин. 19:38-42)

57Вечером к месту казни пришел один богатый человек из Аримафеи, по имени Иосиф. Он тоже был учеником Иисуса. 58Иосиф пошел к Пилату и попросил тело Иисуса. Пилат приказал, чтобы ему отдали тело. 59Иосиф взял его, обернул чистым льняным полотном 60и положил в свою новую гробницу, которая была вырублена в скале. Привалив ко входу большой камень, он ушел. 61А Мария Магдалина и другая Мария остались сидеть напротив гробницы.

Стража у могилы

62На следующий день, это была суббота27:62 Это была суббота – букв.: «после (дня) приготовления (к субботе)»., первосвященники и фарисеи собрались у Пилата.

63– Господин, – обратились они к нему, – мы вспомнили, что когда этот обманщик еще был жив, Он сказал: «Через три дня Я воскресну». 64Поэтому прикажи, чтобы могила три дня охранялась, иначе Его ученики могут прийти, выкрасть тело и сказать народу, что Он воскрес из мертвых. Этот последний обман будет еще хуже первого.

65– Возьмите стражу27:65 Или: «У вас есть стража»., – ответил Пилат, – идите и охраняйте, как знаете.

66Они пошли, опечатали камень и выставили у гробницы стражу.