Mateyu 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 22:1-46

Fanizo la Phwando la Ukwati

1Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati, 2“Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna. 3Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.

4“Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’

5“Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake. 6Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha. 7Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.

8“Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera. 9Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’ 10Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.

11“Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati. 12Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.

13“Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’

14“Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”

Za Kupereka Msonkho

15Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake. 16Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani? 17Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”

18Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa? 19Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari, 20ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”

21Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.”

Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”

22Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.

Ukwati ndi za Kuuka kwa Akufa

23Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso. 24Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo. 25Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo. 26Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri. 27Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso. 28Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”

29Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu. 30Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba. 31Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti, 32‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”

33Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.

Lamulo Lalikulu Koposa

34Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi. 35Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati, 36“Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?” 37Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse. 38Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse. 39Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ 40Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”

Kodi Khristu ndi Mwana wa Ndani?

41Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti, 42“Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?”

Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”

43Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,

44“Ambuye anati kwa Ambuye wanga:

‘Khala pa dzanja langa lamanja

mpaka ndiyike adani ako

pansi pa mapazi ako.’

45Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?” 46Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.

New Russian Translation

Матфея 22:1-46

Притча о свадебном пире

(Лк. 14:16-24)

1Иисус продолжал учить народ в притчах, говоря:

2– Царство Небесное можно сравнить со свадебным пиром, который один царь приготовил для своего сына. 3Он разослал к приглашенным своих слуг, чтобы позвать их на свадьбу, но приглашенные не хотели прийти. 4Тогда царь послал других слуг, наказав им: «Пойдите и скажите им, что мой пир уже готов, зарезаны быки и другой откормленный скот, все угощение готово, пусть приходят на свадебный пир». 5Приглашенные, однако, не обратили на это никакого внимания и разошлись. Один пошел на свое поле, другой торговать, 6а некоторые даже схватили посланных слуг, унизили и убили их. 7Царь был разгневан. Он послал свое войско, уничтожил тех убийц и сжег их город.

8Потом он сказал своим слугам: «Свадебный пир готов, но те, кого я пригласил, не заслужили чести быть на нем. 9Пойдите теперь на перекрестки дорог и приглашайте на пир всех, кого вы встретите». 10Слуги пошли по улицам и стали созывать всех, кого встречали, злых и добрых, и пиршественный зал наполнился гостями, которые возлежали за столами. 11Когда же царь пришел посмотреть на возлежащих, он заметил человека, на котором не было свадебной одежды. 12«Друг, – спросил царь, – как это ты вошел сюда без свадебной одежды?» Человеку нечего было сказать. 13Тогда царь приказал слугам: «Свяжите его по рукам и ногам и выбросьте вон, во тьму, где будет плач и скрежет зубов».

14Ведь приглашенных много, но избранных мало.

Вопрос об уплате налогов

(Мк. 12:13-17; Лк. 20:20-26)

15После этого фарисеи стали советоваться, как бы им поймать Иисуса на слове. 16Они подослали к Нему своих учеников и иродиан22:16 Иродиане составляли политическую группировку, преданную Ироду Антипе и поддерживавшую римлян..

– Учитель, – спросили они, – мы знаем, что Ты Человек честный и истинно учишь пути Божьему. Ты беспристрастен и не стремишься никому угодить. 17Скажи нам, как Ты считаешь, следует ли платить налог кесарю или нет?

18Иисус, зная их коварные намерения, сказал:

– Лицемеры, вы хотите поймать Меня на слове? 19Покажите Мне монету, которой платится дань.

Они принесли Ему динарий. 20Иисус спросил их:

– Кто на ней изображен, и чье на ней имя?

21– Кесаря, – ответили они.

Тогда Иисус сказал им:

– Так и отдавайте кесарево кесарю, а Божье – Богу.

22Услышав это, они удивились, и, оставив Иисуса, они ушли.

Саддукеи задают Иисусу вопрос о воскресении мертвых

(Мк. 12:18-27; Лк. 20:27-40)

23В тот же день саддукеи, которые утверждают, что нет воскресения мертвых, подошли к Иисусу. Они спросили Его:

24– Учитель, Моисей сказал, что если кто-либо умрет, не оставив детей, то его брат должен жениться на вдове и восстановить род22:24 Букв.: «семя». своему брату22:24 См. Втор. 25:5-6.. 25Так вот, у нас тут было семь братьев. Первый женился и умер бездетным, и вдова стала женой его брата. 26То же самое произошло и со вторым, и с третьим, и со всеми семью братьями. 27После всех умерла и женщина. 28Итак, после воскресения, которому из семи братьев она будет женой? Ведь все были ее мужьями.

29Иисус ответил:

– Вы заблуждаетесь, потому что не знаете ни Писаний, ни силы Божьей. 30Воскреснув, люди не будут ни жениться, ни выходить замуж, а будут как ангелы на небесах. 31Что же касается воскресения мертвых, то разве вы не читали, что сказал вам Бог: 32«Я – Бог Авраама, Бог Исаака и Бог Иакова»?22:32 Исх. 3:6. Он Бог не мертвых, а живых.

33Люди слушали и удивлялись Его учению.

Самая главная заповедь

(Мк. 12:28-31; Лк. 10:25-28)

34Фарисеи же, услышав, как Иисус заставил замолчать саддукеев, собрались вокруг Него. 35Один из них, учитель Закона, чтобы поймать Иисуса на слове, спросил:

36– Учитель, какая заповедь в Законе самая важная?

37Иисус ответил:

– «Люби Господа, Бога твоего, всем сердцем твоим и всей душой твоей и всем разумом твоим»22:37 Втор. 6:5.. 38Это первая и самая важная заповедь. 39Вторая же подобна ей: «Люби ближнего твоего, как самого себя»22:39 Лев. 19:18.. 40Весь Закон и учение пророков основаны на этих двух заповедях.

Кем является Христос?

(Мк. 12:35-37; Лк. 20:41-44)

41Когда фарисеи собрались вместе, Иисус спросил их:

42– Что вы думаете о Христе? Чей Он Сын?

– Сын Давида, – ответили Ему.

43Иисус говорит им:

– Почему же тогда Давид, вдохновляемый Духом, называет Его Господом? Ведь он говорит:

44«Сказал Господь Господу моему:

Сядь по правую руку от Меня,

пока Я не повергну врагов Твоих

к ногам Твоим»22:44 Пс. 109:1..

45Итак, если Давид называет Его Господом, то как же в таком случае Он может быть ему Сыном?

46В ответ никто не мог сказать ни слова, и с этого дня они больше не решались задавать Ему вопросы.