Mateyu 11 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 11:1-30

Otumidwa ndi Yohane Mʼbatizi

1Ndipo Yesu atamaliza kulangiza ophunzira ake khumi ndi awiri aja, anachoka kumeneko kupita kukaphunzitsa ndi kukalalikira ku mizinda ya ku Galileya.

2Yohane ali mʼndende anamva zimene Khristu ankachita, ndipo anatumiza ophunzira ake kukamufunsa Iye. 3Anamufunsa kuti, “Kodi Inu ndinu uja ankanena kuti mudzabwerayu kapena tidikire wina?”

4Yesu anayankha kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwamva ndi kuona. 5Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka. 6Odala ndi munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”

7Pamene ophunzira a Yohane ankachoka, Yesu anayamba kuyankhula kwa gulu la anthu za Yohane kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kuti mukaone chiyani? Kodi bango logwedezeka ndi mphepo? 8Nanga munkapita kukaona chiyani, munthu wovala zokongola? Ayi, wovala zokongola amakhala mʼnyumba za mafumu. 9Nanga munkapita kukaona chiyani? Mneneri kodi? Inde ndikuwuzani kuti munkakaona woposa mneneri. 10Uyu ndi amene malemba akunena za iye kuti,

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu

amene adzakonza njira yanu.

11Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pakati pa obadwa ndi mkazi sipanaoneke wina aliyense wamkulu woposa Yohane Mʼbatizi; komatu amene ndi wamngʼono kwambiri mu ufumu wakumwamba ndi wamkulu koposa iye. 12Kuyambira masiku a Yohane Mʼbatizi mpaka tsopano, ufumu wakumwamba ndi wolimbirana ndipo anthu amphamvu okha ndi amene akuwulanda. 13Pakuti aneneri onse ndi malamulo ananenera kufikira nthawi ya Yohane. 14Ndipo ngati inu mufuna kulandira izi, iyeyu ndi Eliya amene ankanena kuti adzabwera uja. 15Iye amene ali ndi makutu amve.

16“Kodi mʼbado uwu ndingawufanizire ndi chiyani? Uli ngati ana opezeka mʼmisika amene akuyitana anzawo nʼkumati:

17“ ‘Tinakuyimbirani zitoliro,

koma inu simunavine;

ife tinayimba nyimbo zamaliro,

koma inu simunalire.’

18Pakuti Yohane sanabwerere kudya kapena kumwa koma iwo ankanena kuti, ‘Iye anali ndi chiwanda.’ 19Mwana wa Munthu anabwera ndi kumadya ndi kumwa koma iwo akuti, ‘Munthu wadyera, woledzera, bwenzi la amisonkho ndi bwenzi la ochimwa.’ Koma nzeru imatsimikizika kuti ndi yolondola mwa ntchito zake.”

Tsoka la Mizinda Itatu Yosatembenuka mtima

20Pamenepo Yesu anayamba kudzudzula mizinda imene zodabwitsa zake zambiri zinachitikamo, chifukwa chakuti sinatembenuke mtima. 21“Tsoka kwa iwe Korazini! Tsoka kwa iwe Betisaida! Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe zikanachitidwa mu Turo ndi Sidoni, iwo akanalapa kale atavala ziguduli ndi kudzola phulusa. 22Koma ndikuwuzani inu kuti pa tsiku lachiweruzo mlandu wa Turo ndi Sidoni udzachepako kusiyana ndi wanu. 23Ndipo iwe Kaperenawo, kodi udzakwezedwa kufika kumwamba? Ayi, udzatsitsidwa mpaka pansi kufika ku Hade. Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe, zikanachitika mu Sodomu, bwenzi iye alipo kufikira lero. 24Koma Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro mlandu wa Sodomu udzachepako kusiyana ndi wanu.”

Goli la Khristu

25Pa nthawi imeneyo Yesu anati, “Ine ndikukuyamikani Inu Atate Ambuye akumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa Inu mwawabisira zinthu izi anzeru ndi ophunzira ndi kuziwulula kwa ana angʼonoangʼono. 26Inde, Atate, ichi chinali chokukomerani Inu.

27“Zinthu zonse zapatsidwa kwa Ine ndi Atate anga. Palibe mmodzi amene adziwa Mwana kupatula Atate ndipo palibe mmodzi amene adziwa Atate kupatula Mwana ndi kwa iwo amene Mwana awasankha kuwawululira.

28“Idzani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo. 29Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wodzichepetsa. Ndipo inu mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. 30Pakuti goli langa ndi losavuta ndipo katundu wanga ndi wopepuka.”

New Russian Translation

Матфея 11:1-30

1Закончив давать наставления Своим двенадцати ученикам, Иисус пошел учить и проповедовать в городах11:1 Букв.: «их». Галилеи.

Вопрос Иоанна Крестителя и ответ Иисуса

(Лк. 7:18-30)

2Когда Иоанн, находясь в темнице, услышал о том, что делает Христос, он послал своих учеников 3спросить Его:

– Ты ли Тот, Кто должен прийти, или нам ожидать кого-то другого?

4Иисус им ответил:

– Пойдите и расскажите Иоанну о том, что вы слышите и видите: 5слепые прозревают, хромые ходят, прокаженные очищаются, глухие слышат, мертвые воскресают и бедным возвещается Радостная Весть. 6Блажен тот, кто не усомнится во Мне.

Свидетельство Иисуса об Иоанне

(Лк. 7:24-35; Лк. 16:16)

7Когда ученики Иоанна ушли, Иисус начал говорить народу об Иоанне:

– Что вы ходили смотреть в пустыню? Тростник, колеблемый ветром? 8Тогда что же вы ходили смотреть? Человека, одетого в роскошные одежды? Нет, те, кто одевается в роскошные одежды, находятся в царских дворцах. 9Тогда что же вы ходили смотреть? Пророка? Да, и говорю вам, что больше, чем пророка. 10Он тот, о ком написано:

«Вот, Я посылаю перед Тобой Моего вестника,

который приготовит перед Тобой Твой путь»11:10 См. Мал. 3:1..

11Говорю вам истину: среди рожденных женами еще не было человека более великого, чем Иоанн Креститель, но наименьший в Царстве Небесном – больше его. 12Со дней Иоанна Крестителя и доныне Царство Божье стремительно продвигается вперед, и прилагающие усилие имеют доступ в него11:12 Это очень сложное место, на которое существует много толкований. Вот другие популярные понимания этого отрывка: 1) «Царство Божье подвергается атакам, и жестокие люди пытаются овладеть им»; 2) «Чтобы войти в Царство Божье нужно приложить усилие, и прилагающие усилие имеют доступ в него»; 3) «Царство Божье стремительно продвигается вперед, а жестокие люди пытаются овладеть им»; 4) «Царство Божье вырывается на свободу, и его подданные являют его мощь» (см. Мих. 2:12-13).. 13Ведь весь Закон и пророки пророчествовали до Иоанна, 14и если вы готовы это принять, то он – Илия, который должен прийти11:14 См. Мал. 4:5.. 15У кого есть уши, пусть слышит!

16Но с кем Мне сравнить это поколение? Оно подобно детям, которые сидят на площади и кричат друг другу:

17«Мы играли вам на свирели,

а вы не плясали;

мы пели вам похоронные песни,

а вы не печалились».

18Смотрите, вот пришел Иоанн, не ест и не пьет, и они говорят: «В нем демон». 19Пришел Сын Человеческий, ест и пьет, и они говорят: «Обжора и пьяница, друг сборщиков налогов и грешников». Но мудрость оправдана ее делами.

Горе нераскаявшимся городам

(Лк. 10:13-15)

20Затем Иисус начал укорять города, в которых Он совершил больше всего чудес, но которые так и не раскаялись.

21– Горе тебе, Хоразин! Горе тебе, Вифсаида! Ведь если бы в Тире и Сидоне были совершены те же чудеса, что в вас, то они бы давно раскаялись, одевшись в рубище и посыпав себя пеплом. 22Но говорю вам: в День Суда Тиру и Сидону будет легче, чем вам. 23И ты, Капернаум, думаешь, что будешь вознесен до небес? Нет, ты будешь сброшен в ад11:23 См. Ис. 14:13-15., потому что если бы в Содоме были совершены такие чудеса, какие были совершены в тебе, то он существовал бы и до сего дня. 24Но говорю вам, что в День Суда Содому будет легче, чем тебе.

Отец и Сын

(Лк. 10:21-22)

25И Иисус продолжал:

– Я славлю Тебя, Отец, Господь неба и земли, за то, что Ты, утаив от мудрецов и ученых, открыл это младенцам. 26Да, Отец, это было угодно Тебе!

27Отец вверил Мне все. Никто не знает Сына, кроме Отца, и никто не знает Отца, кроме Сына и того, кого Сын избирает, чтобы открыть ему Отца.

28Придите ко Мне, все уставшие и обремененные, и Я успокою вас. 29Возьмите на себя ярмо Мое и научитесь у Меня, потому что Я кроток и мягок сердцем, и вы найдете покой вашим душам11:29 См. Иер. 6:16.. 30Ведь Мое ярмо не тяжело, и Моя ноша легка.