Masalimo 96 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

New International Reader’s Version

Psalm 96:1-13

Psalm 96

1Sing a new song to the Lord.

All you people of the earth, sing to the Lord.

2Sing to the Lord. Praise him.

Day after day tell about how he saves us.

3Tell the nations about his glory.

Tell all people about the wonderful things he has done.

4The Lord is great. He is really worthy of praise.

People should have respect for him as the greatest God of all.

5All the gods of the nations are like their statues.

They can’t do anything.

But the Lord made the heavens.

6Glory and majesty are all around him.

Strength and glory can be seen in his temple.

7Praise the Lord, all you nations.

Praise the Lord for his glory and strength.

8Praise the Lord for the glory that belongs to him.

Bring an offering and come into the courtyards of his temple.

9Worship the Lord because of his beauty and holiness.

All you people of the earth, tremble when you are with him.

10Say to the nations, “The Lord rules.”

The world is firmly set in place. It can’t be moved.

The Lord will judge the people of the world fairly.

11Let the heavens be full of joy. Let the earth be glad.

Let the ocean and everything in it roar.

12Let the fields and everything in them be glad.

Let all the trees in the forest sing for joy.

13Let all creation be full of joy in front of the Lord,

because he is coming to judge the earth.

He will faithfully judge the people of the world

in keeping with what is right.