Masalimo 95 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 95:1-11

Salimo 95

1Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,

tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu

2Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko

ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

3Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,

mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.

4Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,

ndipo msonga za mapiri ndi zake.

5Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,

ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

6Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,

tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;

7pakuti Iye ndiye Mulungu wathu

ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,

ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,

monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.

9Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,

ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.

10Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;

ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera

ndipo sanadziwe njira zanga.”

11Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,

“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

New International Reader’s Version

Psalm 95:1-11

Psalm 95

1Come, let us sing for joy to the Lord.

Let us give a loud shout to the Rock who saves us.

2Let us come to him and give him thanks.

Let us praise him with music and song.

3The Lord is the great God.

He is the greatest King.

He rules over all the gods.

4He owns the deepest parts of the earth.

The mountain peaks belong to him.

5The ocean is his, because he made it.

He formed the dry land with his hands.

6Come, let us bow down and worship him.

Let us fall on our knees in front of the Lord our Maker.

7He is our God.

We are the sheep belonging to his flock.

We are the people he takes good care of.

If only you would listen to his voice today.

8He says, “Don’t be stubborn as you were at Meribah.

Don’t be stubborn as you were that day at Massah in the desert.

9There your people of long ago really tested me.

They did it even though they had seen what I had done for them.

10For 40 years I was angry with them.

I said, ‘Their hearts are always going astray.

They do not know how I want them to live.’

11So when I was angry, I made a promise.

I said, ‘They will never enjoy the rest I planned for them.’ ”