Masalimo 94 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 94:1-23

Salimo 94

1Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango,

Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.

2Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi;

bwezerani kwa odzikuza zowayenera.

3Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova,

mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?

4Amakhuthula mawu onyada;

onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.

5Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova;

amapondereza cholowa chanu.

6Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko;

amapha ana amasiye.

7Iwo amati, “Yehova sakuona;

Mulungu wa Yakobo salabadirako.”

8Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu;

zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

9Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva?

Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

10Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga?

Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?

11Yehova amadziwa maganizo a munthu;

Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.

12Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza,

munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

13mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto,

mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

14Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake;

Iye sadzasiya cholowa chake.

15Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo,

ndipo onse olungama mtima adzachitsata.

16Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa?

Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?

17Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

18Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,”

chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.

19Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga,

chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.

20Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu

umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?

21Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama

ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.

22Koma Yehova wakhala linga langa,

ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.

23Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo

ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo;

Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

New International Reader’s Version

Psalm 94:1-23

Psalm 94

1The Lord is a God who punishes.

Since you are the one who punishes, come and show your anger.

2Judge of the earth, rise up.

Pay back proud people for what they have done.

3Lord, how long will those who are evil be glad?

How long will they be full of joy?

4Proud words pour out of their mouths.

All those who do evil are always bragging.

5Lord, they crush your people.

They treat badly those who belong to you.

6They kill outsiders. They kill widows.

They murder children whose fathers have died.

7They say, “The Lord doesn’t see what’s happening.

The God of Jacob doesn’t pay any attention to it.”

8You who aren’t wise, pay attention.

You foolish people, when will you become wise?

9Does he who made the ear not hear?

Does he who formed the eye not see?

10Does he who corrects nations not punish?

Does he who teaches human beings not know anything?

11The Lord knows what people think.

He knows that their thoughts don’t amount to anything.

12Lord, blessed is the person you correct.

Blessed is the person you teach from your law.

13You give them rest from times of trouble,

until a pit is dug to trap sinners.

14The Lord won’t say no to his people.

He will never desert those who belong to him.

15He will again judge people in keeping with what is right.

All those who have honest hearts will follow the right way.

16Who will rise up for me against sinful people?

Who will stand up for me against those who do evil?

17Suppose the Lord had not helped me.

Then I would soon have been lying quietly in the grave.

18I said, “My foot is slipping.”

But Lord, your faithful love kept me from falling.

19I was very worried.

But your comfort brought me joy.

20Can you have anything to do with rulers who aren’t fair?

Can those who make laws that cause suffering be friends of yours?

21Evil people join together against those who do what is right.

They sentence to death those who aren’t guilty of doing anything wrong.

22But the Lord has become like a fort to me.

My God is my rock. I go to him for safety.

23He will pay them back for their sins.

He will destroy them for their evil acts.

The Lord our God will destroy them.