Masalimo 91 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 91:1-16

Salimo 91

1Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba

adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.

2Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,

Mulungu wanga amene ndimadalira.”

3Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje

ndi ku mliri woopsa;

4Adzakuphimba ndi nthenga zake,

ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;

kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.

5Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,

kapena muvi wowuluka masana,

6kapena mliri umene umayenda mu mdima,

kapena zowononga za pa nthawi ya masana.

7Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,

anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,

koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.

8Udzapenya ndi maso ako

ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.

9Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;

wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.

10Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,

zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.

11Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,

kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;

12ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.

13Udzapondaponda mkango ndi njoka,

udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

14“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;

ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.

15Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;

ndidzakhala naye pa mavuto,

ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.

16Ndidzamupatsa moyo wautali

ndi kumupulumutsa.”

La Bible du Semeur

Psaumes 91:1-16

Un refuge sûr

1Qui s’abrite auprès du Très-Haut,

repose sous la protection ╵du Tout-Puissant.

2Je dis à l’Eternel91.2 L’ancienne version grecque a : il dira. : ╵« Tu es mon refuge et ma forteresse,

mon Dieu en qui je me confie ! »

3C’est lui qui te délivre du filet ╵de l’oiseleur,

et de la peste qui fait des ravages.

4Il te couvre sous son plumage,

tu es en sécurité sous son aile,

sa fidélité te protège ╵comme un grand bouclier.

5Tu n’as donc pas à craindre ╵les terreurs de la nuit,

ni les flèches qui volent ╵dans la journée,

6ou bien la peste ╵qui rôde dans l’obscurité,

ou encore le coup fatal ╵qui frappe à l’heure de midi.

7Que mille tombent à côté de toi,

et dix mille à ta droite,

toi, tu ne seras pas atteint.

8Il te suffira de regarder de tes yeux

pour constater ╵la rétribution des méchants.

9Oui, tu es mon refuge ╵ô Eternel !

Si toi, tu fais ╵du Très-Haut ton abri,

10aucun malheur ne t’atteindra,

nulle calamité ╵n’approchera de ta demeure ;

11car à ses anges, ╵il donnera des ordres à ton sujet

pour qu’ils te protègent sur tes chemins91.11 Les v. 11-12 ont été cités par Satan à Jésus lors de la tentation (Mt 4.6 ; Lc 4.10-11). Sur les anges chargés de veiller sur les hommes, voir Gn 24.7 ; Ex 23.20 ; Ps 34.8..

12Ils te porteront sur leurs mains,

de peur que ton pied ne heurte une pierre.

13Tu pourras marcher sur le lion ╵et la vipère,

et piétiner ╵le jeune lion et le serpent91.13 Voir Lc 10.19..

14Oui, celui qui m’est attaché, ╵je le délivrerai

et je protègerai ╵celui qui entretient ╵une relation avec moi.

15Lui, il m’invoquera, ╵et je lui répondrai,

je serai avec lui ╵au jour de la détresse,

je le délivrerai ╵et je l’honorerai,

16je le comblerai d’une longue vie

et lui ferai expérimenter mon salut.