Masalimo 90 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

La Bible du Semeur

Psaumes 90:1-17

Quatrième livre

Apprends-nous à bien compter nos jours !

1Prière de Moïse, l’homme de Dieu.

O Seigneur, d’âge en âge

tu as été notre refuge.

2Avant que soient nées les montagnes,

et que tu aies créé ╵la terre et l’univers,

de toute éternité ╵et pour l’éternité, ╵toi, tu es Dieu.

3Tu fais retourner l’homme ╵à la poussière,

et tu dis aux humains : ╵« Retournez-y90.3 Voir Gn 3.19. ! »

4Car mille ans, à tes yeux,

sont comme le jour d’hier ╵qui est déjà passé90.4 Cité en 2 P 3.8.,

comme une seule veille ╵au milieu de la nuit.

5Tu les plonges dans le sommeil,

et ils sont au matin ╵comme l’herbe éphémère

6qui fleurit le matin, ╵et passe vite :

le soir, elle se fane ╵et se flétrit.

7Nous sommes consumés ╵par ta colère,

ta fureur nous effraie :

8tu as mis devant toi ╵tous nos péchés,

et tu mets en lumière ╵tout ce que nous cachons.

9Tous nos jours disparaissent ╵par ta colère,

et nous achevons nos années ╵comme un murmure…

10Le temps de notre vie ? ╵C’est soixante-dix ans,

au mieux : quatre-vingts ans ╵pour les plus vigoureux ;

et leur agitation ╵n’est que peine et misère.

Car le temps passe vite ╵et nous nous envolons.

11Qui donc connaît ╵l’intensité de ta colère,

et ton courroux ╵à la mesure de la crainte qui t’est due ?

12Oh ! Apprends-nous ╵à bien compter nos jours,

afin que notre cœur ╵acquière la sagesse !

13Tourne-toi de nouveau vers nous, ╵ô Eternel ! ╵Jusques à quand ╵tarderas-tu encore ?

Aie pitié de tes serviteurs !

14Rassasie-nous tous les matins ╵de ton amour,

et nous crierons de joie, ╵pleins d’allégresse, ╵tout au long de nos jours.

15Rends-nous en jours de joie ╵les jours de nos épreuves,

et en années de joie ╵nos années de malheur !

16Que tes serviteurs voient tes œuvres,

et que ta splendeur brille sur leurs descendants.

17Que le Seigneur, ╵notre Dieu, nous accorde sa faveur !

Fais prospérer pour nous ╵l’ouvrage de nos mains !

Oh oui ! fais prospérer ╵l’ouvrage de nos mains !