Masalimo 92 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 92:1-15

Salimo 92

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

1Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

2Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

3kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi

ndi mayimbidwe abwino a zeze.

4Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;

Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.

5Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,

maganizo anu ndi ozamadi!

6Munthu wopanda nzeru sadziwa,

zitsiru sizizindikira,

7kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu

ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,

adzawonongedwa kwamuyaya.

8Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

9Zoonadi adani anu Yehova,

zoonadi adani anu adzawonongeka;

onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.

10Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;

mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.

11Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,

makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,

adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

13odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,

adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.

14Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,

adzakhala anthete ndi obiriwira,

15kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;

Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

La Bible du Semeur

Psaumes 92:1-16

Il est bon de louer l’Eternel

1Psaume à chanter le jour du sabbat.

2Il est bon de louer l’Eternel,

de te célébrer ╵par des chants, ╵ô Très-Haut !

3Et de proclamer, ╵dès le point du jour, ╵ton amour,

tout au long des nuits, ╵ta fidélité,

4sur la cithare à dix cordes92.4 Terme de sens incertain.,

sur le luth et sur la lyre92.4 Sens incertain..

5Ce que tu fais, Eternel, ╵me remplit de joie

et j’acclamerai

les ouvrages de tes mains.

6Que tes œuvres sont grandioses, ╵Eternel !

Que tes pensées sont profondes !

7L’insensé n’y connaît rien,

le sot ne peut les comprendre.

8Si les malfaisants ╵croissent comme l’herbe,

si tous les méchants ╵sont si florissants,

c’est pour périr à jamais.

9Mais toi, tu es tout là-haut,

Eternel, ╵pour toujours.

10Car voici tes ennemis, ╵Eternel,

car voici tes ennemis périssent,

et tous ceux qui font le mal ╵seront dispersés !

11Mais tu me remplis de force, ╵je suis comme un buffle,

je me suis enduit ╵d’huile fraîche.

12Je regarde tous mes détracteurs,

j’entends tous mes adversaires ╵qui s’emploient au mal.

13Car les justes poussent ╵comme le palmier,

ils grandissent ╵comme un cèdre du Liban92.13 Symbole de la prospérité durable opposée à la croissance rapide mais éphémère du méchant (v. 8). Le palmier résiste à la chaleur du désert, le cèdre aux neiges du Liban..

14Bien plantés ╵dans la demeure de l’Eternel,

ils fleurissent ╵sur les parvis du temple, ╵de notre Dieu.

15Ils seront féconds ╵jusqu’en leur vieillesse

et ils resteront ╵pleins de sève et de vigueur,

16ils proclameront ╵combien l’Eternel est droit :

il est mon rocher, ╵on ne trouve en lui ╵aucune injustice.