Masalimo 77 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 77:1-20

Salimo 77

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

1Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;

ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.

2Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;

usiku ndinatambasula manja mosalekeza

ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

3Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;

ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.

Sela

4Munagwira zikope zanga kuti ndisagone

ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.

5Ndinaganizira za masiku akale,

zaka zamakedzana;

6Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.

Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

7“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?

Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?

8Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?

Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?

9Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?

Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:

zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.

11Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;

Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.

12Ndidzakumbukira ntchito zanu

ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13Njira zanu Mulungu ndi zoyera.

Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?

14Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;

Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.

15Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,

zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.

Sela

16Madzi anakuonani Mulungu,

madzi anakuonani ndipo anachita mantha;

nyanja yozama inakomoka.

17Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,

mu mlengalenga munamveka mabingu;

mivi yanu inawuluka uku ndi uku.

18Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,

mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;

dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19Njira yanu inadutsa pa nyanja,

njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,

ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa

mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

La Bible du Semeur

Psaumes 77:1-21

Dieu aurait-il changé ?

1Au chef de chœur, selon Yedoutoun77.1 Voir note 39.1.. Un psaume d’Asaph77.1 Voir note 50.1..

2J’appelle Dieu, ╵je crie vers lui ;

j’appelle Dieu, ╵et il m’écoute.

3Au jour de ma détresse, ╵je m’adresse au Seigneur

tout au long de la nuit, sans cesse, ╵je tends les mains vers lui,

je reste inconsolable.

4Dès que je pense à Dieu, ╵je me mets à gémir,

et quand je réfléchis, ╵j’ai l’esprit abattu.

Pause

5Quand je veux m’endormir, ╵tu me tiens en éveil.

Me voici dans le trouble : ╵je ne sais plus que dire.

6Je songe aux jours passés,

aux années d’autrefois,

7j’évoque mes cantiques, ╵au milieu de la nuit,

je médite en moi-même,

et les questions me viennent :

8« L’abandon du Seigneur ╵va-t-il durer toujours ?

Ne redeviendra-t-il ╵plus jamais favorable ?

9Son amour serait-il ╵épuisé à jamais ?

Sa parole va-t-elle pour toujours ╵rester sans suite ?

10Dieu a-t-il oublié ╵de manifester sa faveur ?

A-t-il, dans sa colère, ╵éteint sa compassion ? »

Pause

11Voici, me dis-je, ╵ce qui fait ma souffrance :

« Le Très-Haut n’agit plus ╵comme autrefois. »

12Je me rappellerai ╵ce qu’a fait l’Eternel.

Oui, je veux évoquer ╵tes prodiges passés,

13je veux méditer sur toutes tes œuvres,

et réfléchir à tes hauts faits.

14Dieu, tu agis saintement !

Quel dieu est aussi grand que Dieu ?

15Car toi, tu es le Dieu ╵qui réalise des prodiges !

Tu as manifesté ╵ta puissance parmi les peuples.

16Et tu as libéré ton peuple,

les enfants de Jacob, ╵comme ceux de Joseph,

en mettant en œuvre ta force.

Pause

17Les eaux77.17 Les eaux de la mer des Roseaux lors de l’Exode que rappellent les v. 17-20. t’ont vu, ô Dieu,

les eaux t’ont vu, ╵et elles se sont mises ╵à bouillonner,

et même les abîmes ╵ont été ébranlés.

18Les nuées déversèrent ╵de la pluie en torrents,

et dans le ciel d’orage, ╵retentit le tonnerre.

Tes flèches77.18 C’est-à-dire les éclairs (18.15 ; 97.4 ; 144.6). sillonnaient ╵le ciel dans tous les sens.

19Au vacarme de ton tonnerre, ╵du sein de la tornade,

l’éclat de tes éclairs ╵illuminait le monde,

et la terre en fut ébranlée, ╵et se mit à trembler.

20Au milieu de la mer, ╵tu as frayé ta route

et tracé ton sentier ╵parmi les grandes eaux77.20 Voir Ex 14 et 15..

Et nul n’a discerné ╵la trace de tes pas.

21Tu as conduit ton peuple ╵comme un troupeau

Par le moyen ╵du ministère de Moïse ╵et d’Aaron.