Masalimo 63 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

1Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

2Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

3Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

4Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

5Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

6Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

7Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

8Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

9Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

10Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

New Russian Translation

Псалтирь 63:1-11

Псалом 63

1Дирижеру хора. Псалом Давида.

2Боже, услышь мой голос, когда я возношу жалобы мои;

сохрани мою жизнь от угроз врага.

3Сокрой меня от замыслов нечестивых,

от шумной толпы злодеев.

4Они заострили свои языки, как мечи,

и нацелили свои слова, как смертоносные стрелы.

5Они стреляют из засады в невинного,

стреляют в него неожиданно и без страха.

6Они воодушевляют друг друга на злые замыслы

и совещаются, чтобы спрятать свои сети,

говоря: «Кто увидит их?»63:6 Или: «нас».

7Они замышляют несправедливость и говорят:

«Мы разработали идеальный план!»

Истинно, коварны разум и сердце человека.

8Но Бог пустит в них стрелы;

внезапно они будут поражены.

9Он обратит их языки против них самих

и приведет их к гибели;

все, кто увидит их,

будут с презрением качать63:9 Будут … качать своими головами; или: «удалятся». своими головами.

10Все люди устрашатся;

они будут возвещать дело Божье

и размышлять о том, что Он сделал.

11Пусть праведные возрадуются о Господе

и найдут в Нем убежище;

пусть все правые сердцем восславят Его.