Masalimo 64 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 64:1-10

Salimo 64

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;

tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.

2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,

ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,

amaponya mawu awo olasa ngati mivi.

4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;

amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,

amayankhula zobisa misampha yawo;

ndipo amati, “Adzayiona ndani?”

6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,

“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”

Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;

mwadzidzidzi adzakanthidwa.

8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa

ndi kuwasandutsa bwinja;

onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

9Anthu onse adzachita mantha;

adzalengeza ntchito za Mulungu

ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.

10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova

ndi kubisala mwa Iye,

owongoka mtima onse atamande Iye!

New Russian Translation

Псалтирь 64:1-14

Псалом 64

1Дирижеру хора. Псалом Давида. Песнь.

2Боже, Тебе подобает хвала64:2 Или: «молчание – хвала Тебе»; или: «в молчании восхвалят Тебя». на Сионе,

пред Тобой исполним обеты свои.

3Ты слышишь молитву;

к Тебе придут все люди.

4Когда одолевают нас наши грехи,

Ты прощаешь нам беззакония.

5Блажен тот, кого Ты избрал и приблизил,

чтобы он жил при Твоем святилище64:5 Букв.: «в Твоих дворах»..

Мы насытимся благами дома Твоего,

святого храма Твоего.

6Ты отвечаешь нам устрашающими делами,

даруя избавление, Боже, Спаситель наш.

Ты – надежда всех краев земли

и самых дальних морей.

7Силой Своей утвердил Ты горы;

Ты препоясан могуществом.

8Ты усмиряешь шум морей,

шум их волн

и смуту народов.

9Живущие на краю земли

устрашатся Твоих знамений.

Ворота зари и сумерек

Ты наполнишь песнями радости.

10Ты заботишься о земле и орошаешь ее,

обильно даруя ей плодородие.

Потоки Божьи полны воды,

чтобы дать народу зерно,

потому что так Ты землю устроил.

11Ты наполняешь водой ее борозды

и уравниваешь ее гребни,

смягчая ее дождями,

благословляя ее ростки.

12Ты венчаешь год Своей щедростью,

и повозки Твои перегружены изобилием.

13Трава преображает пустыню,

и весельем одеты холмы.

14Луга покрыты стадами,

и зерном одеты долины.

Все восклицает и поет от радости!